< Uk-ukom 14 >

1 Simmalog ni Samsom idiay Timna, ket sadiay, nakitana ti maysa a babai, maysa kadagiti annak dagiti Filisteo.
Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
2 Idi nagawid isuna, imbagana iti ama ken inana, “Nakitak ti maysa a babai idiay Timna, maysa kadagiti annak a babbai dagiti Filisteo. Ita, alaenyo isuna para kaniak tapno agbalin nga asawak.”
Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
3 Ngem kinuna ti ama ken inana kenkuana, “Awan kadi ti babai kadagiti annak dagiti kabagiam, wenno kadagiti amin a tattaotayo? Mangalaka kadi iti asawaem manipud kadagiti saan a nakugit a Filisteo?” Kinuna ni Samson iti amana, “Alaem isuna para kaniak, ta tunggal makitak isuna, maay-ayoak kenkuana.”
Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
4 Ngem saan nga ammo ti ama ken inana a nagtaud kenni Yahweh daytoy a banag, ta kayatna a mangparnuay iti riri kadagiti Filisteo (ta dagiti Filisteo ti mangiturturay iti Israel iti dayta a tiempo).
(Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
5 Kalpasanna, kadua ni Samson ti ama ken inana a simmalog idiay Timna, ket nakagtengda kadagiti kaubasan ti Timna. Ket rimmuar sadiay ti maysa a bumaro a leon nga agngerngernger kenkuana.
Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
6 Immay a dagus kenkuana ti Espiritu ni Yahweh, ket rinangrangkayna ti leon a kas kalaka iti panangrangkayna iti bassit a kalding, ket awan ti iggemna. Ngem saanna nga imbaga iti ama wenno inana ti inaramidna.
Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
7 Napanna kinasarita ti babai, ket idi kinitana ti babai, naay-ayo ni Samson kenkuana.
Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
8 Kalpasan ti sumagmamano nga aldaw idi nagsubli ni Samson tapno asawaenna isuna, simmiasi isuna tapno kitaenna ti bangkay ti leon. Ket adda maysa a pangen dagiti ayukan ken diro iti nabatbati a bagi ti leon.
Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
9 Inakuyna ti diro babaen kadagiti imana ket mangmangan bayat a magmagna. Idi nakagteng iti ayan ti ama ken iti inana, intedna ti dadduma kadagitoy, ket nanganda. Ngem saanna nga imbaga nga innalana ti diro iti nabatbati a bagi ti leon.
Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
10 Simmalog ti ama ni Samson iti ayan ti babai, ket nagparambak ni Samson sadiay, ta daytoy ti kaugalian dagiti agtutubo a lallaki.
Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
11 Apaman a nakita dagiti kabagian ti babai isuna, nangiyegda kenkuana iti tallopulo a gagayyemda a mangkadua kenkuana.
Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
12 Kinuna ni Samson kadakuada, “Adda burburtiak kadakayo. No adda kadakayo ti makaibaga kaniak iti sungbat daytoy kabayatan ti pito nga aldaw iti panagrambak, mangtedakto iti tallopulo a lino a kagay ken tallopulo a pagan-anay.”
Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
13 Ngem no saanyo a maibaga kaniak ti sungbat, ket ikkandakto iti tallopulo a lino a kagay ken tallopulo a pagan-anay.” Kinunada kenkuana, “Ibagam kadakami ti burburtiam, tapno mangngegmi daytoy.”
Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
14 Kinunana kadakuada, “Manipud iti mangmangan, adda maysa a banag a makan; manipud iti napigsa, adda maysa a banag a nasam-it.” Ngem saan a napugtoan dagiti sangailina ti sungbat iti las-ud ti tallo nga aldaw.
Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
15 Iti maika-uppat nga aldaw, kinunada iti asawa ni Samson, “Sikapam ti asawam tapno ibagana kadakami ti sungbat ti burburtia, ta no saan puorandaka ken ti balay ti amam. Inawisdakami kadi ditoy tapno papanglawendakami?”
Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
16 Ket rinugian ti asawa ni Samson ti agsangit iti sangoananna: kinunana, “Kagurguranak! Saannak nga ay-ayaten. Nangibagaka iti maysa a burburtia iti sumagmamano kadagiti tattaok, ngem saanmo nga imbaga kaniak ti sungbatna.” Kinuna ni Samson kenkuana, “Kitaem, no saanko nga imbaga iti ama wenno iti inak, rumberng kadi nga ibagak kenka?”
Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
17 Nagsangsangit isuna kabayatan ti pito nga aldaw a kabayag ti panagrambakda. Iti maikapito nga aldaw, imbaga ni Samson ti sungbat iti asawana gapu ta kasta unay ti panangpilitna kenkuana. Imbaga ti asawana ti sungbat kadagiti kabagian dagiti tattaona.
Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
18 Ket kinuna dagiti lallaki iti siudad kenni Samson iti maikapito nga aldaw sakbay a lumnek ti init, “Ania ti nasamsam-it ngem iti diro? Ania ti napigpigsa ngem ti leon?” Kinuna ni Samson kadakuada, “No saanyo a pinagarado ti bakak, saanyo koma a naammoan ti sungbat iti burburtiak.”
Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
19 Ket kellaat nga immay kenni Samson ti pannakabalin ti Espiritu ni Yahweh. Simmalog ni Samson idiay Askelon ket pinatayna ti tallopulo a lallaki kadagiti tattao. Innalana ti nasamsamda, ket intedna dagiti pagan-anay kadagiti nakasungbat iti burburtiana. Kasta unay ti ungetna ket simmang-at isuna iti balay ti amana.
Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
20 Ket naited ti asawana iti nasinged a gayyemna.
Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.

< Uk-ukom 14 >