< Josue 1 >

1 Ita, kalpasan iti ipapatay iti adipen ni Yahweh a ni Moises, nagsao ni Yahweh iti katulongan ni Moises a ni Josue nga anak ni Nun, a kinunana,
Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
2 “Natayen ti adipenko a ni Moises. Ballasiwenyo ngarud ita iti Karayan Jordan, sika ken amin dagitoy a tattao, nga agturong iti daga nga it-itedko kadakuada —kadagiti tattao ti Israel.
“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
3 Intedko kadakayo ti tunggal disso a mapagnaanto iti dapanyo. Intedko daytoy kadakayo a kas inkarik kenni Moises.
Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
4 Manipud idiay let-ang ken Libano, agingga iti nalawa a karayan a Eufrates, iti amin a daga dagiti Hitteo, ken agingga iti Dakkel a Baybay a paglennekan ti init, isunto ti agbalinto a dagayo.
Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
5 Awanto iti makabael nga agtakder iti sangoanam iti amin nga aldaw ti panagbiagmo. Addaakto kenka a kas iti kaaddak idi kenni Moises. Saankanto a baybay-an wenno panawan.
Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6 Pumigsaka ken tumuredka. Idauloamto dagitoy tattao a mangtawid iti daga nga inkarik kadagiti kapuonanda nga ited kadakuada.
“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
7 Pumigsa ken tumuredka iti kasta unay. Tungpalem a nasayaat dagiti amin a linteg nga imbilin kenka iti adipenko a ni Moises. Surotem a naan-anay dagitoy tapno agballigika iti sadinoman a papanam.
Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
8 Kanayonmonto a saritaen ti maipanggep iti daytoy a libro ti linteg. Utobemto daytoy iti aldaw ken rabii tapno matungpalmo dagiti amin a naisurat iti daytoy. Ket agbalinkanto a narang-ay ken naballigi.
Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
9 Saan kadi nga imbilinko kenka? Pumigsa ken tumuredka! Saanka nga agbuteng. Saanka a maupay. Adda kenka ni Yahweh a Diosmo iti sadinoman a papanam.”
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10 Binilin ngarud ni Josue dagiti mangidadaulo kadagiti tattao,
Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
11 “Mapankayo idiay kampo ket ibilinyo kadagiti tattao, 'Mangisaganakayo kadagiti taraon para kadagiti bagbagiyo. Kalpasan iti tallo nga aldaw ballasiwenyonto iti Karayan Jordan ket serken ken tagikuaenyo ti daga nga it-ited ni Yahweh a Diosyo kadakayo.'”
“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
12 Kinuna ni Josue kadagiti Rubenita, dagiti Gadita ken kadagiti kagudua iti tribu ni Manases,
Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
13 “Laglagipenyo ti sao nga imbilin iti adipen ni Yahweh a ni Moises idi kinunana, 'It-ited kadakayo ni Yahweh a Diosyo ti inana, ket it-itedna daytoy a daga kadakayo.'
“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
14 Agtalinaedto dagiti assawayo, dagiti annakyo ken dagiti tarakenyo iti daga nga inted kadakayo ni Moises iti labes ti Jordan. Ngem mapan nga umuna kadakayo dagiti maingel a lallaki tapno tulonganda dagiti kakabsatyo
Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
15 agingga nga ited ni Yahweh kadagiti kakabsatyo ti inana a kas intedna kadakayo. Ket tagikuaendanto met ti daga nga ited kadakuada ni Yahweh a Diosyo. Ket agsublikayonto iti bukodyo a daga ket tagikuaenyo daytoy, ti daga nga inted kadakayo iti adipen ni Yahweh a ni Moises iti labes ti Jordan, a pagsingsingisingan ti init.
Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16 Ket simmungbatda kenni Josue a kinunada, “Aramindenmi amin nga imbilinmo kadakami, ken mapankami iti sadinoman a pangibaonam kadakami a papananmi.
Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
17 Agtulnogkami kenka a kas panagtulnogmi kenni Moises. Adda koma kenka ni Yahweh a Diosmo a kas kaaddana kenni Moises.
Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
18 Matay ti siasinoman nga agsukir kadagiti bilinmo ken manglabsing kadagiti sasaom. Pumigsaka laeng ken tumuredka.”
Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”

< Josue 1 >