< Joel 2 >

1 Pagunienyo ti trumpeta idiay Sion, ken pagunienyo ti tangguyob iti nasantoan a bantayko! Agpigerger koma iti buteng dagiti amin nga agnanaed iti daga, ta umadanin ti aldaw ni Yahweh; pudno nga asidegen daytoy.
Lizani lipenga mu Ziyoni. Chenjezani pa phiri langa loyera. Onse okhala mʼdziko anjenjemere, pakuti tsiku la Yehova likubwera, layandikira;
2 Daytoy ket aldaw iti kinasipnget ken kinalidem, aldaw a naulep ken nalulem. Kas iti parbangon nga agsaknap kadagiti bantay, sumungsungaden ti dakkel ken nabileg nga armada. Awan pay ti armada a kas iti daytoy, ken awanton ti kastoy, uray kalpasan iti adu a henerasion.
tsiku la mdima ndi chisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani. Ngati mʼbandakucha umene wakuta mapiri, gulu lalikulu ndi la ankhondo amphamvu likubwera, gulu limene nʼkale lomwe silinaonekepo ngakhale kutsogolo kuno silidzaonekanso.
3 Ikiskisap ti apuy ti amin a banag iti sangoananna, ken adda gil-ayab iti likudan. Ti daga ket kas iti minoyungan ti Eden iti sangoananna, ngem iti likudanna ket adda iti nadadael a let-ang. Pudno, awanto ti makalibas iti daytoy.
Patsogolo pawo moto ukupsereza, kumbuyo kwawo malawi amoto akutentha zinthu. Patsogolo pawo dziko lili ngati munda wa Edeni, kumbuyo kwawo kuli ngati chipululu, kulibe kanthu kotsalapo.
4 Kasla kabalio ti langa ti armada, ken kasla kumakabalio ti panagtarayda.
Maonekedwe awo ali ngati akavalo; akuthamanga ngati akavalo ankhondo.
5 Kumaradakad ti panaglagtoda a kasla kadagiti karuahe iti tuktok dagiti bantay, kasla iti uni ti gumilgil-ayab nga apuy a mangikiskisap iti garami, kasla iti nabileg nga armada a nakasagana a makigubat.
Akulumpha pamwamba pa mapiri ndi phokoso ngati la magaleta, ngati moto wothetheka wonyeketsa ziputu, ngati gulu lalikulu la ankhondo lokonzekera nkhondo.
6 Iti isusungadda, agbuteng dagiti tattao ken pummusyaw dagiti rupada.
Akangowaona, anthu a mitundu ina amazunzika mu mtima; nkhope iliyonse imagwa.
7 Ti panagtarayda ket kasla iti nabileg a mannakigubat; kumalay-atda kadagiti pader a kasla kadagiti soldado; agmarmartsada, aggigiddan ti addangda, ken naurnos dagiti linyada.
Amathamanga ngati ankhondo; amakwera makoma ngati asilikali. Onse amayenda pa mizere, osaphonya njira yawo.
8 Awan ti agdidinnuron; agmarmartsa ti tunggal maysa iti dalanna; lumasatda kadagiti sarikedked ket saan a madadael ti linyada.
Iwo sakankhanakankhana, aliyense amayenda molunjika. Amadutsa malo otchingidwa popanda kumwazikana.
9 Sipapardasda a mangraut iti siudad, tumarayda kadagiti pader, kumalay-atda kadagiti babbalay, ket sumrekda kadagiti tawa a kasla kadagiti agtatakaw.
Amakhamukira mu mzinda, amathamanga mʼmbali mwa khoma. Amakwera nyumba ndi kulowamo; amalowera pa zenera ngati mbala.
10 Agkintayeg ti daga iti sangoananda, agpigerger dagiti langit, simmepnget ti init ken bulan, ken saanen nga agraniag dagiti bituen.
Patsogolo pawo dziko limagwedezeka, thambo limanjenjemera, dzuwa ndi mwezi zimachita mdima, ndipo nyenyezi zimaleka kuwala.
11 Binilin ni Yahweh ti armadana, ta nagadu unay dagiti mannakigubatna ken nabilegda, dagiti agtungtungpal kadagiti bilbilinna. Ta kasta unay a nakabutbuteng ti aldaw ni Yahweh. Siasino ngay koma ti makalasat iti daytoy?
Yehova amabangula patsogolo pawo, gulu lake lankhondo ndi losawerengeka, ndipo amphamvu ndi amene amamvera kulamula kwake. Tsiku la Yehova ndi lalikulu; ndi loopsa. Ndani adzapirira pa tsikulo?
12 Kuna ni Yahweh, “Ngem uray pay ita, agsublikayo kaniak iti amin a pusoyo. Agayunar, agsangit, ken agladingitkayo.”
“Ngakhale tsopano, bwererani kwa Ine ndi mtima wanu wonse posala zakudya ndi kukhetsa misozi,” akutero Yehova.
13 Ipakitayo ti sipupuso a panagbabawiyo ken saan laeng nga iti panangray-abyo kadagiti kawesyo, ket agsublikayo kenni Yahweh a Diosyo. Ta naasi ken managparabur isuna, saan a nalaka nga agunget ngem ketdi napnoan iti ayat, ken saannatayo koma a kayat a dusaen.
Ngʼambani mtima wanu osati zovala zanu. Bwererani kwa Yehova Mulungu wanu, pakuti Iye ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka, ndipo amaleka kubweretsa mavuto.
14 Siasino ngay koma ti makaammo? No ngay agbaliw ti pangngeddengna ket maasian isuna, ken mangted isuna kadagiti bendision, daton a bukbukel ken daton a mainum nga agpaay kenni Yahweh a Diosyo?
Akudziwa ndani? Mwina adzasintha maganizo nʼkutimvera chisoni, nʼkutisiyira madalitso, a chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa kwa Yehova Mulungu wanu.
15 Pagunienyo ti trumpeta idiay Sion, ken agayunarkayo, ket mangangaykayo iti nasantoan a gimong.
Lizani lipenga mu Ziyoni, lengezani tsiku losala zakudya, itanitsani msonkhano wopatulika.
16 Ummongenyo dagiti tattao, mang-angaykayo iti nasantoan a gimong. Ummongenyo dagiti panglakayen, ummongenyo dagiti ubbing, ken dagiti maladaga. Paruarenyo dagiti nobio kadagiti siledda ken paruarenyo dagiti nobia kadagiti siled a pagur-urayanda iti seremonia ti kasar.
Sonkhanitsani anthu pamodzi, muwawuze kuti adziyeretse; sonkhanitsani akuluakulu, sonkhanitsani ana, sonkhanitsani ndi oyamwa omwe. Mkwati atuluke mʼchipinda chake, mkwatibwi atuluke mokhala mwake.
17 Agsangit koma dagiti papadi nga agserserbi kenni Yahweh iti nagbaetan ti pagserkan ken ti altar. Kunaenda koma, “O Yahweh, kaasiam dagiti tattaom ket saanmo nga ipalubos a maibabain dagiti tattaom a maiyarig a tawidmo, ket iturayan ida dagiti nasion. Apay nga ibaga dagiti nasion, ayanna ngayen ti Diosda?''
Ansembe amene amatumikira pamaso pa Yehova, alire pakati pa guwa lansembe ndi khonde la Nyumba ya Yehova. Azinena kuti, “Inu Yehova, achitireni chifundo anthu anu. Musalole kuti cholowa chanu chikhale chinthu chonyozeka, kuti anthu a mitundu ina awalamulire. Kodi nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina amanena kuti, ‘Ali kuti Mulungu wawo?’”
18 Kalpasanna, impakita ni Yahweh ti panangipategna iti dagana ket kinaasianna dagiti tattaona.
Pamenepo Yehova adzachitira nsanje dziko lake ndi kuchitira chisoni anthu ake.
19 Insungbat ni Yahweh kadagiti tattaona: “Adtoy, ikkankayo kadagiti bukel, baro nga arak, ken lana. Mapnekkayonto kadagitoy, ken saankonton nga itulok a maibabainkayo kadagiti nasion.
Yehova adzawayankha kuti, “Ine ndikukutumizirani tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta ndipo mudzakhuta ndithu; sindidzakuperekaninso kuti mukhale chitonzo kwa anthu a mitundu ina.
20 Ipanawkonto kadakayo dagiti mangdarup a naggapu iti amianan, ket iturongko ida iti namaga ken langalang a daga. Agturong dagiti akin-sango nga armadada iti baybay iti daya, ken ti akinlikud nga armada iti baybay iti laud. Umalingasawdanto ken sumngawto dagiti bangsitda. Agaramidakto kadagiti nakakaskasdaaw a banbanag.
“Ine ndidzachotsa ankhondo akumpoto kuti apite kutali ndi inu, kuwapirikitsira ku dziko lowuma ndi lachipululu, gulu lawo lakutsogolo ndidzalipirikitsira ku nyanja ya kummawa ndi gulu lawo lakumbuyo, ku nyanja ya kumadzulo. Ndipo mitembo yawo idzawola, fungo lake lidzamveka.” Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
21 Saanka nga agbuteng, daga, agragsak ken agrag-oka, ta nagaramid ni Yahweh kadagiti nakakaskasdaaw a banbanag.
Iwe dziko usachite mantha; sangalala ndipo kondwera. Zoonadi Yehova wachita zinthu zazikulu.
22 Saankayo nga agbuteng, dakayo nga atap nga ay-ayup iti tay-ak, ta agtubonto dagiti ruruot iti pagaraban kadagiti let-ang, agbunganto dagiti kaykayo, ket umadunto ti apit kadagiti igos ken ubas.
Inu nyama zakuthengo, musachite mantha, pakuti msipu wa ku chipululu ukuphukira. Mitengo ikubala zipatso zake; mitengo ya mkuyu ndi mpesa ikubereka kwambiri.
23 Agragsakayo, tattao ti Sion, ken agrag-okayo kenni Yahweh a Diosyo. Ta pagtuduennanto iti umno a tiempo ket agbayakabak ti tudo para kadakayo, ti tudo iti tiempo ti panagrurusing ken tiempo ti panagregreg iti bulong a kas idi damo.
Inu anthu a ku Ziyoni sangalalani, kondwerani mwa Yehova Mulungu wanu, pakuti wakupatsani mvula yoyambirira mwachilungamo chake. Iye wakutumizirani mivumbi yochuluka, mvula yoyambirira ndi mvula ya nthawi ya mphukira, monga poyamba paja.
24 Mapnonto iti trigo dagiti pagirikan, ken aglippiasto dagiti pagkargaan iti baro nga arak ken lana.
Pa malo opunthira padzaza tirigu; mʼmitsuko mudzasefukira vinyo watsopano ndi mafuta.
25 “Isublikto kadakayo dagiti mula nga inay-aywananyo iti adu a tawen a kinnan dagiti nagsasaruno a pangen dagiti dudon, ti nabileg nga armadak nga imbaonko kadakayo.
“Ine ndidzakubwezerani zonse zimene zinawonongedwa ndi dzombe, dzombe lalikulu ndi dzombe lalingʼono, dzombe lopanda mapiko ndi dzombe lowuluka; gulu langa lalikulu la nkhondo limene ndinalitumiza pakati panu.
26 Mangankayonto iti adu ket mabsogkayo, ken dayawenyo ti nagan ni Yahweh a Diosyo a nagaramid kadagiti nakaskasdaaw kadakayo. Saankonton nga ibabain dagiti tattaok.
Mudzakhala ndi chakudya chambiri, mpaka mudzakhuta, ndipo mudzatamanda dzina la Yehova Mulungu wanu, amene wakuchitirani zodabwitsa; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
27 Maammoanyonto nga addaak iti Israel, ket Siak ni Yahweh a Diosyo, ken awanen ti sabali. Saankonton nga ibabain dagiti tattaok.
Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndili mu Israeli, kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndi kuti palibenso wina; ndipo anthu anga sadzachitanso manyazi.
28 Iti mabiit, ibukbukkonto ti Espirituk kadagiti amin a lasag, ket agipadtonto dagiti annakyo a lallaki ken babbai. Agtagtagainepto dagiti panglakayenyo, makakitanto iti sirmata dagiti agtutuboyo a lallaki.
“Ndipo patapita nthawi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi ana anu aakazi adzanenera, nkhalamba zanu zidzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya.
29 Kadagidiay nga aldaw, ibukbukkonto met ti Espirituk kadagiti adipen a lallaki ken babbai.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo.
30 Mangipakitaakto kadagiti nakakaskasdaaw iti langit ken iti daga, dara, apuy ken dagiti adigi nga asuk.
Ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi pa dziko lapansi, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
31 Sumipngetto ti init ken lumabbaganto ti bulan a kasla iti dara, sakbay a dumteng ti nakabutbuteng unay nga aldaw ni Yahweh.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Ambuye.
32 Iti dayta a tiempo, maisalakanto dagiti amin nga umawag iti nagan ni Yahweh. Ta addanto dagiti makalasat idiay Bantay Sion ken idiay Jerusalem, a kas imbaga ni Yahweh, ket makalasatto dagiti pinili ni Yahweh.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka; pakuti chipulumutso chidzakhala pa Phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, monga Yehova wanenera, pakati pa otsala amene Yehova wawayitana.

< Joel 2 >