< Jeremias 30 >

1 Kastoy ti sao ni Yahweh nga immay kenni Jeremias, kinunana,
Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 “Kastoy ti pakaammo ni Yahweh a Dios ti Israel, 'Isuratmo iti maysa a nalukot a pagsuratan ti amin a sao nga imbagak kenka.
“Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza.
3 Ta denggem, umadanin dagiti al-aldaw—kastoy ti pakaammo ni Yahweh—inton isublikto ti sigud a nasayaat a kasasaad dagiti tattaok nga Israel ken Juda. Siak a ni Yahweh, ti nangibaga iti daytoy. Ta isublikto ida iti daga nga intedko kadagiti kapuonanda, ket tagikuaendanto daytoy.'''
Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”
4 Dagitoy dagiti sasao nga impakaammo ni Yahweh maipapan iti Israel ken Juda,
Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda:
5 “Ta kastoy ti kuna ni Yahweh, “Adda nangngegmi a timek nga agpigpigerger gapu iti buteng saan ket a timek gapu iti talna.
“Yehova akuti: “Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa, ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.
6 Agsaludsoddkayo ken ammoenyo no makapagpasngay ngata ti maysa a lalaki. Apay ngarud a makitkitak ti tunggal agtutubo a lallaki nga ap-aprusanna ti pus-ongna? Kasla da la babai nga agpaspasikal, apay a pimmusyapusyaw amin dagiti rupada?
Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti: Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira? Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?
7 Asida pay! Ta daytanto nga aldaw ket agbalinto a naidumduma, nga awan ti kaaspingna. Daytoy ket tiemponto ti pannakariribuk ni Jacob, ngem maispalto isuna manipud iti daytoy.
Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri! Sipadzakhala lina lofanana nalo. Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo, koma adzapulumuka ku masautsowo.”
8 Ta iti daytanto nga aldaw—kastoy ti pakaammo ni Yahweh a Mannakabalin-amin—a tukkulekto dagiti sangol iti tenggedyo, ken pugsatekto dagiti kawaryo, isu a saandakayto a tagabuen pay dagiti gangannaet.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo, ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo ndipo ndidzadula zingwe zowamanga; Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.
9 Ngem dayawendanto ni Yahweh a Diosda ken pagserbianda ni David nga arida, a pagbalinekto nga ari a mangituray kadakuada.
Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo ndiponso Davide mfumu yawo, amene ndidzawasankhira.
10 Isu a sika, Jacob nga adipenko, saanka nga agbuteng—kastoy ti pakaammo ni Yahweh—ken saanka a maupay, Israel. Ta kitaem, umadanin ti panangisublik kenka manipud iti adayo, ken dagiti kaputotam manipud iti daga a nakaipananda a kas balud. Agsublinto ni Jacob ket addaanto isuna iti kapia; natalgedto isuna ket awanto a pulos ti pakaigapuan iti panagbuteng.
“‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo; usade nkhawa, iwe Israeli,’ akutero Yehova. ‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali, zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere, ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.
11 Ta addaak kadakayo—kastoy ti pakaammo ni Yahweh— tapno isalakankayo. Ket iyegkonto ti naan-anay a panagpatingga kadagiti amin a nasion a nangiwarawaraak kadakayo. Ngem siguradoek a saankayto a gibusan, uray no aturenkayo iti nainkalintegan ken saanko nga itulok a saankayo a madusa.'
Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’ akutero Yehova. ‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu kumene ndinakubalalitsirani, koma inu sindidzakuwonongani kotheratu. Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa. Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’”
12 Ta kastoy ti kuna ni Yahweh, “Saan a maagasan ti dunoryo; nagimpeksiyon dagiti sugatyo.
Yehova akuti, “Chilonda chanu nʼchosachizika, bala lanu ndi lonyeka.
13 Awan ti siasinoman a mangipakaasi iti kasasaadyo, awan iti pamuspusan tapno agimbag dagiti sugatyo.
Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu, palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira, palibe mankhwala ochiritsa inu.
14 Amin dagiti kaayan-ayatyo ket nalipatan dakayo. Saandakayto a pagan-ano, ta sinugatkayo iti kas iti sugat ti maysa a kabusor ken kas iti panangatur ti maysa a naranggas nga apo gapu kadagiti adu a nakaro a kinadakesyo ken saan a mabilang a basbasolyo.
Abwenzi anu onse akuyiwalani; sasamalanso za inu. Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira. Ndipo ndakulangani mwa nkhanza, chifukwa machimo anu ndi ambiri, ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.
15 Apay pay laeng a dumawatkayo iti tulong para iti dunoryo? Saan a maimbagan ti ut-ot a laklak-amenyo. Gapu kadagiti adu a nakaro a kinadakesyo ken kadagiti saan a mabilang a basbasolyo, inaramidko kadakayo dagitoy a banbanag.
Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu? Bala lanu silingapole ayi. Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.
16 Isu nga amin a mangdadael kadakayo ket madadaelto met, ken amin dagiti kabusoryo ket maipanawto a kas balud. Ta dagiti nagtakaw kadakayo ket matakawanto met, ken amin dagiti nangsamsam kenka ket masamsamto.
“Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa; adani anu onse adzapita ku ukapolo. Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso; onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.
17 Ta iyegkonto kadakayo ti pannakapaimbagyo; paimbagekto dagiti sugatyo—kastoy ti pakaammo ni Yahweh—aramidekto daytoy ta inawagan dakayo a: Napagtalaw. Awan ti siasinoman a mangisakit iti daytoy a Sion.”'
Ndidzachiza matenda anu ndi kupoletsa zilonda zanu, akutero Yehova, ‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika. Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’”
18 Kastoy ti kuna ni Yahweh, “Dumngegkayo, umadanin ti panangisublik kadagiti sigud a nasayaat a kasasaad dagiti tolda ni Jacob ken kaasiakto dagiti pagtaenganna. Ket maibangonto ti maysa a siudad kadagiti gabsuon dagiti nadadael, ken maibangonto manen ti sarikedkedda iti sigud a nakaisaadanna.
Yehova akuti, “Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo; mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake, nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.
19 Ket addanto iti kanta ti panagdaydayaw ken panagragrag-o nga agtaud kadakuada; ta paaduekto ida a saan ket a kissayan; padayawakto ida isu a saandanto a maibaba.
Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo. Ndidzawachulukitsa, ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika; ndidzawapatsa ulemerero, ndipo sadzanyozedwanso.
20 Ket agbalinto a kas iti sigud dagiti tattaoda, ken mabukelto ti taripnongda iti imatangko inton dusaek amin dagiti mangidaddadanes ita kadakuada.
Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale, ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga; ndidzalanga onse owazunza.
21 Agtaudto kadakuada ti panguloda. Agapunto isuna iti nagtetengngaanda inton ayabak isuna ket umasideg kaniak. No saanko nga aramiden daytoy, adda kadi met ngarud iti makaitured nga umasideg kaniak? —kastoy ti pakaammo ni Yahweh.
Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo. Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo. Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira. Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane popanda kuyitanidwa?” akutero Yehova.
22 Ket agbalinkayonto a tattaok, ken siakto ti Diosyo.
“Choncho inu mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”
23 Kitaenyo, ti pungtot ni Yahweh a maiyarig iti nadawel a bagio ket bimtaken. Saan nga agsardeng daytoy a nadawel a bagio. Agtayyekto daytoy iti ulo dagiti nadadangkes a tattao.
Taonani ukali wa Yehova wowomba ngati mphepo ya mkuntho. Mphepo ya namondwe ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.
24 Saanto nga agsardeng ti pungtot ni Yahweh agingga a maaramidna ken maipatungpalna dagiti panggep ti pusona. Kadagiti maudi nga al-aldaw, maawatanyonto dagitoy.”
Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka mpaka atakwaniritsa zolinga za mu mtima mwake. Mudzamvetsa zimenezi masiku akubwerawo.

< Jeremias 30 >