< Jeremias 15 >

1 Ket kinuna ni Yahweh kaniak, “Uray no nakatakder ni Moises wenno ni Samuel iti sangoanak, saankonto latta a paboran dagitoy a tattao. Papanawenyo ida iti sangoanak tapno umadayoda.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
2 Mapasamakto a kunaendanto kenka, ‘Sadino ngay koma ti papananmi?’ Ket masapul nga ibagam kadakuada, ‘Kastoy ti kuna ni Yahweh: Dagiti naituding a matay ket rumbeng a matay; dagiti naituding a matay iti kampilan ket matay iti kampilan. Dagiti naituding a matay iti bisin ket matay iti bisin; ken dagiti naituding a maitalaw a kas balud ket maitalaw a kas balud.’
Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
3 Ta bingayekto ida iti uppat a bunggoy—kastoy ti pakaammo ni Yahweh—ti kampilan a mangpapatay kadagiti dadduma, dagiti aso a mangpirsay kadagiti dadduma, dagiti billit kadagiti tangatang ken dagiti narungsot nga ayup iti daga a mangan ken mangdadael kadagiti dadduma.
“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
4 Pagbalinekto ida a nakabutbuteng a banag kadagiti amin a pagarian iti daga, maigapu kenni Manases a putot ni Ezekias nga ari ti Juda, gapu iti inaramidna idiay Jerusalem.
Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
5 Ta siasino komati mangngaasinto kenka, Jerusalem? Siasinonto ti agladingit para kenka? Siasinonto ti sumardeng a mangsaludsod iti kasasaadmo?
“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
6 Linaksidnak—kastoy ti pakaammo ni Yahweh— tinallikudannak. Isu a dangrankanto babaen iti imak ken dadaelenkanto. Naumaakon a mangngaasi kenka.
Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
7 Isu nga itaepkonto ida kadagiti ruangan ti daga babaen iti sarukay. Patayekto dagiti annakda. Dadaelekto dagiti tattaok agsipud ta saanda a tallikudan dagiti wagasda.
Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
8 Paaduekto ti bilang dagiti baloda nga ad-adu pay ngem iti darat iti igid ti baybay. Ibaonkonto ti manangdadael iti tengnga ti aldaw a maibusor kadagiti inna dagiti agtutubo a lallaki. Kellaatkonto nga itinnag kadakuada ti kigtot ken buteng.
Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
9 Matalimudawto ti ina a nangipasngay iti pito nga annak. Agbugsotto. Lumnekto ti initna kabayatan nga aldaw pay laeng. Maibabain ken maupayto, ta iyawatkonto dagiti nabati iti kampilan iti imatang dagiti kabusorda—daytoy ket pakaammo ni Yahweh.”
Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
10 Asi-ak pay, inak! Ta impasngaynak a maysa a lalaki a mannakisusik ken mannakisuppiat iti entero a daga. Saanak a nagpautang, wenno awan ti nagpautang kaniak ngem inlunoddak amin.
Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
11 Kinuna ni Yahweh: “Saanka kadi nga ispalen a maipaay iti kinaimbag? Siguradoekto nga agpakaasi iti tulong dagiti kabusormo iti tiempo ti kalamidad ken rigat.
Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
12 Adda kadi maysa a makatukkol iti landok? Nangnangruna iti landok a naggapu iti amianan a nalaokan iti gambang?
“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13 Itedkonto kadagiti kabusormo ti kinabaknang ken dagiti gamengmo a kas samsam nga awan bayadna. Aramidekto daytoy gapu kadagiti amin a basol nga inaramidmo kadagiti amin a beddengmo.
Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
14 Ket ipaluboskonto nga ipandaka dagiti kabusormo iti daga a saanmo nga ammo, ta addanto apuy a sumged, napasgedan gapu iti pungtotko kenka.”
Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
15 Sika a mismo iti makaammo, O Yahweh! Lagipen ken tulongannak. Ibalsannak kadagiti mangkamkamat kaniak. Saannak nga iyadayo iti kinaanusmo. Bigbigem a nagsagabaak iti pannakaibabain gapu kenka.
Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16 Nasarakan dagiti sasaom, ket kinnanko dagitoy. Dagiti sasaom ket rag-o kaniak, rag-o iti pusok, ta naiwaragawag ti naganmo kaniak, O Yahweh a Mannakabalin-amin.
Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
17 Saanak a nagtugaw iti ummong dagiti nagrambak wenno nagrag-o. Nagtugawak nga agmaymaysa gapu iti mannakabalin nga imam, ta pinunnonak iti pungtot.
Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18 Apay nga agtultuloy ti ut-otko ken saan a maagasan ti sugatko, saan nga umim-imbag? Agbalinka kadi a kasla kadagiti manangallilaw a danum kaniak, danum a matianan?
Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
19 Ngarud, kastoy ti kuna ni Yahweh, “No agbabawika, Jeremias, awatenka, ket agtakderkanto iti sangoanak ken pagserbiannak. Ta no isinam dagiti minamaag a banbanag kadagiti napateg a banbanag, agbalinkanto a kasla pannakangiwatko. Agsublinto kenka dagiti tattao, ngem sika a mismo, masapul a saanka nga agsubli kadakuada.
Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20 Pagbalinenka a kasla maysa a pader a gambang a saan a masalput dagitoy a tattao, ket gubatendakanto, ngem saandakanto a maparmek, ta addaakto a mangisalakan ken mangispal kenka—kastoy ti pakaammo ni Yahweh—
Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
21 ta ispalenkanto iti ima dagiti nadangkes ken subbotenka iti ima dagiti naranggas a tattao.”
“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

< Jeremias 15 >