< Jeremias 1 >
1 Dagitoy dagiti sao ni Jeremias a putot ni Hilkias; maysa isuna kadagiti papadi idiay Anatot iti daga ti Benjamin.
Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
2 Immay ti sao ni Yahweh kenkuana kadagiti aldaw ti ari ti Juda a ni Josias a putot ni Amon, iti maikasangapulo ket tallo a tawen a panagturayna.
Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
3 Immay met daytoy kadagiti aldaw a ni Jehoyakim a putot ni Josias ti ari idiay Juda, agingga iti maikalima a bulan iti maika-sangapulo ket maysa a tawen a panagturay kas ari ni Zedekias a putot ni Josias idiay Juda, idi naitalaw a kas balud dagiti tattao ti Jerusalem.
Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
4 Immay ti sao ni Yahweh kaniak a kunana,
Yehova anayankhula nane kuti,
5 “Sakbay a binukelka iti aanakan, pinilikan; sakbay a naipasngayka, inlasinka; pinagbalinka a profeta kadagiti nasion.”
“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
6 “O Apo a Yahweh!” Kinunak, “Saanko nga ammo ti agsao, ta ubingak unay.”
Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
7 Ngem kinuna ni Yahweh kaniak, “Saanmo a kunaen, 'Ubingak unay'. Masapul a mapanka iti sadinoman a pangibaonak kenka, ken masapul nga ibagam ti aniaman nga ibilinko kenka!
Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
8 Saanka a mabuteng kadakuada, ta addaak kenka a mangispal kenka—kastoy ti pakaammo ni Yahweh.”
Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
9 Ket inyunnat ni Yahweh ti imana, sinagidna ti ngiwatko ket kinunana kaniak, “Ita, inkabilko ti saok iti ngiwatmo.
Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
10 Dutokanka ita nga aldaw kadagiti nasion ken kadagiti pagarian, a mangparut ken mangrebba, a mangdadael ken mangparmek, a mangbangon ken mangimula.”
Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
11 Immay ti sao ni Yahweh kaniak a kunana, “Ania ti makitam Jeremias? Kinunak, “Makitak ti maysa a sanga ti almendras.”
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
12 Kinuna ni Yahweh kaniak, “Husto ti nakitam, ta sipsiputak ti saok tapno maipatungpal daytoy.”
Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
13 Immay kaniak ti sao ni Yahweh iti maikadua a daras, a kunana, “Ania ti makitam?” Kinunak, “Makitak ti maysa a kaldero nga agburburek ti linaonna, nakatingeg manipud iti amianan.”
Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
14 Kinuna ni Yahweh kaniak, “Addanto tumaud a didigra manipud amianan a sagrapen dagiti amin nga agnanaed iti daytoy a daga.
Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
15 Ta ay-ayabak dagiti amin a tribu kadagiti akin-amianan a pagarian, impakaammo ni Yahweh. Umaydanto, ket isaadto ti tunggal maysa ti tronona iti pagserkan kadagiti ruangan ti Jerusalem, kadagiti amin a pader a nakapalawlaw iti daytoy, ken kadagiti amin a siudad ti Juda.
Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 Kedngakto ida gapu iti amin a kinadakesda iti panangtallikudda kaniak, iti panangpuorda iti insenso a maipaay kadagiti didiosen, ken iti panangdayawda iti inaramid dagiti bukodda nga ima.
Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
17 Agsaganaka! Tumakderka ket ibagam kadakuada ti aniaman nga ibilinko kenka. Saanka nga agbuteng iti sangoananda, ta no saan, ad-adda pay a pagbutngenka iti sangoananda!
“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
18 Denggem! Ita nga aldaw, pinagbalinka a nasarikedkedan a siudad, adigi a landok, ken bakud a bronse a maibusor iti entero a daga—maibusor kadagiti ari ti Juda, kadagiti opisiales daytoy, kadagiti padi daytoy, ken kadagiti tattao iti daga.
Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
19 Bumusordanto kenka, ngem saandakanto a maparmek, ta addaakto kenka a mangispal kenka—kastoy ti pakaammo ni Yahweh.”
Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.