< Isaias 7 >
1 Kadagidi aldaw ni Ahaz a putot ni Jotam a putot ni Uzzias, nga ari ti Juda, simmang-at da Rezin nga ari ti Aram ken ni Peka a putot ni Remalias nga ari ti Israel idiay Jerusalem a manggubat iti daytoy, ngem saanda a maparmek daytoy.
Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.
2 Naipakaammo iti balay ni David a nakikadua ti Aram iti Efraim. Kasta unay ti butengna, ken uray dagiti tattaona ket uray la agpigerger gapu iti buteng, kasla da la kaykayo iti kabakiran a ginunggon ti angin.
Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.
3 Ket kinuna ni Yahweh kenni Isaias, “Rummuarka a kaduam ti putotmo lalaki a ni Sear Jasub ket inkayo sabten ni Ahaz iti murdong ti kanal iti akinngato a pagurnongan ti danum, iti dalan a mapan iti tay-ak ti Aglablaba iti lupot.
Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu.
4 Ibagam kenkuana, 'Agannadka, saanka nga agdanag, dika agbuteng kadagitoy dua a kayo nga umas-asok, iti nalaus a pungtot ni Rezin, ni Aram, ken ni Peka a putot ni Remalias.
Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya.
5 Nagpanggep iti kinadakes a maibusor kenka da Aram, Efraim, ken Rezin a putot ni Remalias; kinunada,
Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti,
6 “Rautentayo ti Juda ken butbutngentayo daytoy, serkentayo daytyoy ket isaadtayo sadiay ti putot ni Tabeel kas aritayo.”
‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’
7 Kinuna ni Apo a Yahweh, “Saan a mapasamak daytoy; saan a maaramid daytoy,
Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi: “‘Zimenezo sizidzatheka, sizidzachitika konse,
8 gapu ta ti ulo ti Aram ket ti Damasco, ken ti ulo ti Damasco ket ni Rezin. Iti las-ud iti 65 a tawen, maparmekto ti Efraim ket saandanton a maibilang a maysa a nasion.
pakuti Siriya amadalira Damasiko, ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi. Zisanathe zaka 65 Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.
9 Ti ulo ti Efraim ket ti Samaria, ken ti ulo ti Samaria ket ti putot ni Remalias. No saan nga agtalinaed a natibker ti pammatiyo, sigurado a saankayonto nga agtalinaed a natalged.”'”
Dziko la Efereimu limadalira Samariya ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi. Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu, ndithu simudzalimba konse.’”
10 Nagsao manen ti Apo kenni Ahaz,
Yehova anayankhulanso ndi Ahazi,
11 “Dumawatka iti pagilasinan kenni Yahweh a Diosmo; dawatem kenkuana daytoy iti kaunggan wenno iti kangatoan.” (Sheol )
“Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.” (Sheol )
12 Ngem kinuna ni Ahaz, “Saanak a dumawat ken saanko a padasen ni Yahweh.”
Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”
13 Isu a simmungbat ni Isaias, “Dumngegka, O balay ni David. Saan kadi nga umanay kenka ti panangpadasmo iti kinaanus ti tattao? Masapul kadi pay a padasem ti kinaanus ti Diosko?
Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga?
14 Ngarud, mismo a ti Apo ti mangted kenka iti pagilasinan: kitaem, agsikogto ti maysa a babai, agpasngayto iti maysa a lalaki, ket mapanagananto iti Immanuel.
Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli.
15 Manganto isuna iti gatas ken diro inton ammonan nga agkedked nga agaramid iti dakes ken pilienna ti kinaimbag.
Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino.
16 Ta sakbay a maammoan ti ubing ti agkedked nga agaramid iti dakes ken pilienna ti kinaimbag, agbalinto a langalang ti daga dagiti dua nga ari a pagbutbutngam.
Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja.
17 Iyegto ni Yahweh kenka ken kadagiti tattaom ken iti balay ti amam dagiti aldaw nga awan kapadana sipud pay idi simmina ti Efraim iti Juda—iyegnanto a maibusor kenka ti Ari ti Asiria.
Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”
18 Iti dayta a tempo, paswitanto ni Yahweh ti maysa a ngilaw manipud kadagiti adayo a karayan ti Egipto, ken maysa nga alimbubuyog manipud iti daga ti Asiria.
Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya.
19 Umaydanto amin agnaed kadagiti amin a tanap, kadagiti rangkis a batbato, kadagiti siit-siitan a mulmula, ken kadagiti amin a pagpaaraban.
Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto.
20 Iti dayta a tiempo, kuskusanto ti Apo babaen iti labahas nga inabanganna iti ballasiw ti Karayan Eufrates—ti Ari ti Asiria— kuskosannanto ti ulom, dagiti buok kadagiti luppom; kuskosennanto pay ti barbasmo.
Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe.
21 Iti dayta nga aldaw, mangibatinto ti maysa a tao iti maysa a sibibiag nga urbon a baka ken dua a karnero,
Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri.
22 ket gapu iti aglaplapusanan a gatas nga itedda, manganto isuna iti gatas, gapu ta manganto iti gatas ken diro dagiti amin a nabati iti daga.
Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi.
23 Iti dayta a tiempo, tunggal disso nga adda iti sangaribo a kaubasan nga aggatad iti sangaribo a pirak a sekel, ket awanto ti mabati no di laeng sisiitan a mula ken kalkalunay.
Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga.
24 Mapanto dagiti tattao sadiay nga aganup babaen kadagiti panada, gapu ta agbalinto a sisiitan ken kakalkalunayan dayta a daga.
Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga.
25 Umadayodanto kadagiti turturod a nasukay iti gabyon, gapu iti panagbuteng kadagiti siit ken kalkalunay; ngem agbalinto daytoy a pagaraban dagiti baka ken karnero.
Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.