< Isaias 66 >

1 Kastoy ti kuna ni Yahweh, “Ti langit ti tronok, ken ti daga ti pagbatayan dagiti sakak. Sadino ngarud ti balay nga ipatakderyo a maipaay kaniak? Sadino ti lugar a mabalinko a paginanaan?
Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 Ti imak ti nangaramid kadagitoy amin a banbanag; kasta ti wagas a napaadda dagitoy a banbanag - daytoy ket pakaammo ni Yahweh. Daytoy ti tao nga anamungak, ti napakumbaba ken managbabawi iti espirituna, ken agpigeger iti saok.
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
3 Isuna a mangpatpatay iti baka, mangpatpatay met iti tao; isuna a mangidatdaton iti karnero ket mangtuktukkol met iti tengnged ti aso; isuna a mangidatdaton iti bukbukel a daton ket mangidatdaton met iti dara ti babuy; isuna a mangidatdaton iti insenso ket an-anamunganna met ti kinadangkes. Pinilida dagiti bukodda a wagas, ken agragsakda kadagiti makarimon nga aramidda.
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 Iti kasta met laeng a wagas a piliekto ti pannusada, iyegkonto kadakuada ti pagbutbutnganda, gapu ta idi immawagak, awan iti simmungbat; idi nagsaoak, awan iti dimngeg. Inaramidda ti dakes iti panagkitak, ken pinilida nga aramiden dagiti banbanag a saan a makaay-ayo kaniak.
Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 Denggenyo ti sao ni Yahweh, dakayo nga agpigpigerger iti saona, “Kinuna dagiti kakabsatyo a manggurgura ken mangilaklaksid kadakayo, 'Maidaydayaw koma ni Yahweh, ket makitaminto ti rag-oyo,' ngem maibabaindanto.
Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 Ti uni ti riribuk gapu iti gubat ket agtaud iti siudad, maysa nga uni manipud iti templo, ti uni manipud kenni Yahweh a mangbalbales kadagiti kabusorna.
Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
7 Sakbay nga agpasikal ti Sion, agpasngay isuna; sakbay nga umay kenkuana ti ut-ot, agipasngay isuna iti anak a lalaki.
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
8 Siasino ti nakangngeg iti kasta a banag? Siasino ti nakakita kadagiti kasta a banbanag? Maipasngay kadi iti maysa nga aldaw ti maysa a daga? Maibangon kadi ti maysa a nasion iti apagkanito? Ngem apaman nga agpasikal ti Sion, ipasngayna dagiti annakna.
Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 Iyegko aya ti maysa a maladaga iti aanakan ket saanko a palubosan a maipasngay? - salsaludsoden ni Yahweh. Wenno iyegko aya ti ubing iti kanito a maipasngay ket lappedak? - salsaludsoden ti Diosyo.”
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 Makipagrag-okayo iti Jerusalem ken agragsakkayo gapu kenkuana, dakayo amin a mangay-ayat kenkuana; makipagrag-okayo kenkuana, dakayo amin a nagladingit gapu kenkuana!
“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
11 Ta agsusokayonto ket mapnekkayo; maliwliwakayonto babaen kadagiti barukongna; ta inumenyonto dagitoy agingga a mapnekkayo ket agragsakkayo iti kinawadwad ti dayagna.
Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
12 Daytoy ti kuna ni Yahweh, “Dandanikon nga ipalak-am ti kinarang-ay iti Sion a kas iti maysa a karayan, ken dagiti kinabaknang dagiti nasion a kas iti maysa a waig nga agluplupias ti panagayusna. Agsusokayto iti sibayna, ubbaennakayonto, ken rayray-awennakayonto iti rabaw dagiti tumengna.
Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 No kasano iti panangliwliwa ti maysa nga ina iti anakna, kastanto met ti panangliwliwak kadakayo, ket maliwliwakayonto idiay Jerusalem.”
Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 Makitayonto daytoy, ket agrag-onto ti pusoyo, ket pumigsanto dagiti tulangyo a kas iti naganus a ruot nga agrusing. Maiparangarangto ti ima ni Yahweh kadagiti adipenna, ngem makaungetto isuna kadagiti kabusorna.
Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 Ta kitaenyo, umayto ni Yahweh nga addaan iti apuy, ken umayto dagiti karwahena a kas iti alawig, tapno iyegna ti bara ti ungetna ken ti panangtubngarna babaen iti darang ti apuy.
Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
16 Ta ipatungpal ni Yahweh ti pannakaukom kadagiti tattao babaen iti apuy ken babaen iti kampilanna. Adunto dagiti mapapatay ni Yahweh.
Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
17 Ilaslasinda dagiti bagida nga agpaay kenni kenni Yahweh ken daldalusanda dagiti bagbagida, tapno makaserrekda kadagiti minuyongan, sursurotenda dagiti mangmangan kadagiti lasag ti babuy ken kadagiti makarimon a banbanag a kas kadagiti utot.” Agpatinggadanto - kastoy ti pakaammo ni Yahweh.
Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 Ta ammok dagiti aramid ken kapanunotanda. Umayen ti tiempo inton ummongek dagiti amin a nasion ken pagsasao. Umaydanto ket makitada ti dayagko.
“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 Mangikabilakto iti dakkel a pagilasinan kadakuada. Ket mangibaonakto kadagiti makalasat kadakuada a mapan kadagiti nasion: idiay Tarsis, Put, ken Lud, kadagiti pumapana a mangbiat kadagiti baida, idiay Tubal, Jaban, ken kadagiti adayo nga isla a saanda pay a nangngeg ti maipanggep kaniak wenno saan pay a nakakita iti dayagko. Iwaragawagdanto ti dayagko kadagiti nasnasion.
“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
20 Isublidanto dagiti kakabsatyo manipud kadagiti amin a nasion, a kas maysa a daton kenni Yahweh. Umaydanto a nakasakay kadagiti kabalio, ken kadagiti karwahe, kadagiti karison, kadagiti mulo, ken kadagiti kamelio, ket agturongda iti nasantoan a bantayko a Jerusalem - kuna ni Yahweh. Ta mangiyegto dagiti tattao ti Israel iti bukbukel a daton a naikarga iti nadalus a pagkargaan iti balay ni Yahweh.
Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
21 Piliekto pay nga agbalin a padi ken Levita ti dadduma kadagitoy - kuna ni Yahweh.
Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 Ta no kasano nga agtalinaedto iti sangoanak ti baro a langit ken baro a daga nga aramidek - daytoy ket pakaammo ni Yahweh - kasta met nga agtalinaedto dagiti kaputotanyo, ken agtalinaedto ti naganyo.
“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
23 Manipud iti maysa a bulan agingga iti sumaruno, ken manipud iti maysa nga Aldaw a Panaginana agingga iti sumaruno, umayto amin dagiti tattao tapno agparintumeng kaniak - kuna ni Yahweh.
“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
24 Rumuardanto ket makitada dagiti bangkay dagiti tattao a nagrebelde kaniak, ta saanto a matay dagiti igges a mangan kadagitoy, ken saanto a maiddep ti apuy a manguram kadagitoy; ket agbalinto daytoy a makarimon kadagiti amin a lasag.
“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

< Isaias 66 >