< Isaias 41 >
1 Dumgngegkayo kaniak a siuulimek, dakayo a dagdaga iti adayo; pabaroen koma dagiti nasion ti pigsada; umasidegda koma ket agsaoda; agiinnasidegtayo tapno aglilinnawagtayo.
“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
2 Siasino ti nangsugsog iti maysa a taga-daya? Siasino ti nangayab kenkuana tapno agserbi kenkuana? Impaimana dagiti nasion kenkuana ken nangted kenkuana iti pannakabael a mangparmek kadagiti ar-ari; ar-aramidenna ida a kasla tapuk babaen iti kampilanna, a kasla naitayab a punget iti baina.
“Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3 Kamkamatenna ida ken lumablabas a saan a maan-ano, iti napartak a pagnaan a saan pay a nasagid dagiti sakana.
Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4 Siasino ti nangaramid ken nangtungpal kadagitoy nga ar-aramid? Siasino ti nangayab kadagiti kaputotan manipud idi punganay? Siak a ni Yahweh ti umuna ken ti maudi, siak daydiay.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5 Nakita dagiti purpuro ket nagbutengda; nagpigerger dagiti pagpatinggaan ti daga; umasidegda ken umayda.
Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
6 Tultulongan ti tunggal maysa ti kaarubana, ken ibagada iti tunggal maysa, 'Bumilegka.'
aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7 Isu a parparegtaen ti karpintero ti mammanday, ken parparegtaen ti agmarmartilyo ti agtaltaltal ti pasnaan, a kunana iti aglinlinang, ‘Nagsayaat ti pannakalinangna.’ Inlansada daytoy tapno saanto daytoy a matnag.
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8 Ngem sika Israel nga adipenko, Jacob a pinilik, nga anak ni Abraham a gayyemko,
“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9 sika nga isubsublik manipud kadagiti murdong ti daga, sika nga inawagak manipud kadagiti adayo a luglugar, ken ti nangibagaak, 'Sika ti adipenko;' Pinilika ken saanka a linaksid.
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Saanka nga agbuteng ta addaak kenka. Saanka a madanagan ta siak ti Diosmo. Papigsaenka, tulonganka ken ipangatoka babaen iti kannawan nga ima ti naikari a balligik.
Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11 Kitaenyo, amin a gumurgura kadakayo ket maipababa ken maibabainto; dagiti sumupsuppiat kadakayo ket kasdanto la awan ken mapukawdanto.
“Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Sapulemto ket saanmo a masapulan dagiti nakisuppiat kenka; dagiti nakigubgubat kenka ket agbalinto a kasla awan, awan kapaypay-anda.
Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
13 Ta siak, ni Yahweh a Diosmo ti mangkibin iti makannawan nga imam, ibagak kenka, 'Saanka nga agbuteng; tulonganka.'
Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
14 Saanka nga agbuteng, Jacob, sika nga igges, ken dakayo a lallaki ti Israel; tulongankayonto” - daytoy ti pakaammo ni Yahweh, a Mannubbotmo ken Nasantoan a Dios ti Israel.
Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 “Kitaen, pagbalinenka a kasla natadem a pagtaltag; baro ken dua ti tademna; taltalgemto dagiti banbantay ken rumekem ida; aramidemto a kasla taep dagiti turturod.
“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 Itaepmonto ida, ket itayabto ida ti angin; warawaraento ida ti angin. Agrag-okanto kenni Yahweh, agraokanto iti Nasantoan a Dios ti Israel.
Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17 Agbirok iti danum ti maparparigat ken agkasapulan ngem awan a pulos, ken agmaga dagiti dila gapu iti pannakawaw; Siak a ni Yahweh ket sumungbatto kadagiti kararagda; Siak a Dios ti Israel ket saankonto ida a baybay-an.
“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Pagayusekto dagiti waig kadagiti turturod, ken dagiti ubbog iti tengnga dagiti tanap; Pagbalinekto a dan-aw ti danum ti disierto ken ti natikag a daga nga ubbog ti danum.
Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 Iti let-ang, agtubonto ti sedro, ti akasia, ti arayan ken ti kayo ti olibo; pagtuboekto iti disierto ti saleng, ti aruo ken ti parwa.
Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 Aramidekto daytoy tapno makita, mabigbig, ken maawatan dagiti tattao nga inaramid daytoy ti ima ni Yahweh, a pinarsua daytoy ti Nasantoan a Dios ti Israel.
kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21 Ibagayo ti darumyo,” kuna ni Yahweh; 'iparangyo ti kasayaatan a pammaneknekyo nga agpaay kadagiti didiosenyo,” kuna ti Ari ni Jacob.
“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 Yegda koma kadakami dagiti bukodda a pammaneknek; paumayenyo ida iti sangoanan ken ipakaammoda kadakami no ania ti mapasamak, tapno maammoanmi a nalaing dagitoy a banbanag. Ibagada koma kadakami dagiti immuna nga impadtoda a pakaammo tapno utobenmi dagitoy ken ammoenmi ti pannakapatungpal dagitoy.
Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23 Ibagayo dagiti banbanag maipapan iti masakbayan tapno maammoanmi no dioskayo; agaramidkayo iti naimbag wenno dakes tapno agbuteng ken masdaawkami.
tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 Kitaenyo, awan serserbi dagiti didiosenyo ken dagiti aramidyo; ti mangpili kadakayo ket makarimon.
Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25 Nangpataudak iti maysa a tao manipud iti ammianan ket umay isuna; manipud iti isisingising ti init, inayabak isuna nga umaw-awag iti naganko, ket ibaddeknanto a kasla pitak dagiti mangiturturay, kas iti dumadamili a mangibaddebaddek iti pila.
“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 Siasino ti nangiwaragawag iti daytoy manipud idi punganay, tapno maammoantayo? Ken sakbay a nangrugi ti tiempo tapno maibagatayo, “Husto isuna?” Ngem kinapudnona, awan ti nangipablaak iti daytoy, wen, awan ti nakangngeg nga adda ti aniaman nga imbagayo.
Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
27 Immuna a kinunak iti Sion, “Kitaenyo, adtoydan;” Nangibaonak iti maysa a mangipadamag iti Jerusalem.
Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 Idi kimmitaak, awan a pulos, awan ti uray maysa kadakuada a makaited iti nasayaat a pammagbaga, ti makasungbat iti saludsodko.
Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Kitaenyo, awan serserbida amin ken dagiti ar-aramidda ket awan serserbina; dagiti sinukogda nga imahe ket angin ken kinaubbaw.
Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.