< Isaias 39 >

1 Iti dayta a tiempo, nangipatulod ni Merodak Baladan nga anak ni Baladan, nga ari ti Babilonia, iti sursurat ken sagut kenni Hezekias; ta nadamagna a nagsakit ni Hezekias ket immimbagen.
Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
2 Naay-ayo ni Hezekias kadagitoy a banbanag; impakitana kadagiti mensahero iti bodegana a nakaidulinan dagiti napapateg a banbanag-ti pirak, ti balitok, dagiti bangbanglo ken dagiti napapateg a lana, ti pagiduldulinan kadagiti armasna, ken amin a masarakan iti dayta a bodegana. Awan ti aniaman iti balayna, wenno iti amin a pagarianna ti saan nga impakita ni Hezekias kadakuada.
Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
3 Kalpasan daytoy, napan ni profeta Isaias kenni Ari Hezekias ket sinaludsodna kenkuana, “Ania ti imbaga kenka dagitoy a lallaki? Sadino ti nagappuanda?” Kinuna ni Hezekias, “Immayda kaniak manipud iti adayo a pagilian ti Babilonia.”
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
4 Sinaludsod ni Isaias, “Ania ti nakitada iti uneg ti balaymo?” Insungbat ni Hezekias, “Nakitada amin nga adda iti uneg ti balayko. Awan ti aniaman kadagiti napapateg a banbanag iti balayko a saanko nga impakita kadakuada.”
Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
5 Ket kinuna ni Isaias kenni Hezekias, “Denggem ti sao ni Yahweh a Manakabalin-amin:
Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
6 “Kitaem, dumtengto dagiti aldaw nga amin a banag iti palasiom, dagiti banbanag nga indulin dagiti kapuonam agingga iti daytoy nga aldaw, ket maipanto idiay Babilonia. Awanto ti mabati, kuna ni Yahweh.
Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
7 Ket dagiti annak a lalaki a naiyanak manipud kenka, nga isu ti nagbalinam nga ama-ipanawdanto ida, ket agbalindanto nga eunuko iti palasio ti ari iti Babilonia.”
Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
8 Kalpasanna, kinuna ni Hezekias kenni Isaias, “Ti sao ni Yahweh nga imbagam ket naimbag.” Ta pinanunotna, “Addaanto ti kappia ken kinatalged kadagiti aldawko.”
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”

< Isaias 39 >