< Isaias 38 >
1 Kadagidi nga aldaw, nagsakit ni Hezekias ken ngannganin matay. Isu a napan kenkuana ni Isaias a putot a lalaki ni Amos a profeta ket kinunana kenkuana, “Kuna ni Yahweh, 'Iyurnosmon ti balaymo ta mataykan, saankan nga agbiag.'”
Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
2 Kalpasanna simmango ni Hezekias iti pader ket nagkararag kenni Yahweh.
Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
3 Kinunana, “Pangngaasim O Yahweh ta lagipem no kasanoak a nagbiag a napudno iti sangoanam iti amin a pusok, ken no kasanok nga inaramid dagiti nasayaat iti imatangmo.” Ket nagsangit iti nasaem ni Hezekias.
“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
4 Kalpasanna, dimteng ti sao ni Yahweh kenni Isaias a kunana,
Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
5 “Mapanmo ibaga kenni Hezekias a pangulo dagiti tattaok, 'Kastoy ti kuna ni Yahweh a Dios ni David a kapuonam: Nangngegko ti kararagmo ken nakitak dagiti luluam. Kitaem, nayunak iti sangapulo ket lima a tawen ti biagmo.
“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
6 Ket ispalenka ken daytoy a siudad manipud iti pannakabalin ti ari ti Asiria, ket salaknibak daytoy a siudad.
Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
7 Daytoyto ti pagilasinam manipud kaniak a ni Yahweh, nga aramidekto no ania ti imbagak:
“‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
8 Kitaem, pagsubliekto iti sangapulo nga addang ti aniniwan iti agdan ni Ahaz.” Isu a nagsubli iti sangapulo nga addang iti agdan nga isu ti bimmabaanna.
Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
9 Daytoy ti naisurat a kararag ni Hezekias nga ari ti Juda, idi nagsakit isuna ket naimbagan:
Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
10 “Imbagak nga iti kabanbannuagak innakon kadagiti ruangan ti sheol; maibaonak sadiay iti nabatbati a tawtawenko. (Sheol )
Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol )
11 Imbagak a saankon a makita ni Yahweh, ni Yahweh iti daga dagiti sibibiag; saankon a mamatmatan dagiti tattao wenno dagiti agnanaed iti lubong.
Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 Naikkaten ti biagko ket naipanawen kaniak a kasla iti tolda ti maysa nga agpaspastor; Nalukotkon ti biagko a kasla iti maysa nga umaabel; putputedem ti biagko manipud iti pagab-abellan; gibgibusem ti biagko iti nagbaetan ti aldaw ken rabii.
Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 Nagdung-awak agingga iti agsapa; kasla iti maysa a leon, rangkarangkayenna dagiti tulangko; Iti nagbaetan ti aldaw ken rabii, gibgibusem ti biagko.
Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
14 Agit-itak a kasla maysa a salapingaw ken maysa a kalapati; nabannog dagiti matakon a tumangtangad. O Apo, maidaddadanesak; tulongannak.
Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
15 Ania ti mabalinko nga ibaga? Nagsaon isuna kaniak, ket inaramidnan daytoy; magnaakto a nainayad iti amin a tawenko gapu ta kasta unay ti panagladingitko.
Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
16 O Apo, ti panagsagaba nga intedmo ket naimbag para kaniak; sapay koma ta maisubli kaniak ti biagko; insublim ti biagko ken ti salun-atko.
Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
17 Agpaay iti pagimbagak a napadasak ti kasta a panagladingit. Inispalnak manipud iti abut ti pannakadadael; ta imbellengmo dagiti amin a basbasolko iti likodam.
Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
18 Ta saan a makapagyaman kenka ti sheol; saannaka a maidaydayaw ti patay; dagiti agpababa iti abut ket saan a mangnamnama iti kinamatalekmo. (Sheol )
Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol )
19 Ti sibibiag a tao, ti sibibiag a tao, isuna ti makapagyaman kenka, a kas iti ar-aramidek iti daytoy nga aldaw; ipakaammo ti maysa nga ama kadagiti annakna ti kinamatalekmo.
Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
20 Isalakannak ni Yahweh, ken rambakanminto babaen iti samiweng iti amin nga aldaw iti biagtayo idiay balay ni Yahweh.”
Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
21 Ita, kinuna ni Isaias, “Pagalaem ida iti sangkatipkel nga igos ken ikabilmo daytoy iti lettegna ket umimbagto isuna.”
Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
22 Kinuna pay ni Hezekias, “Anianto ti pagilasinan a sumang-atakto manen iti balay ni Yahweh?”
Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”