< Isaias 19 >

1 Maysa a pakaammo maipanggep iti Egipto. Kitaenyo, agsakay ni Yahweh iti napardas nga ulep ket agturong idiay Egipto; agkintayeg iti sangoananna dagiti didiosen iti Egipto, ket marunaw dagiti puso dagiti Egipcio.
Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
2 Kiburekto dagiti Egipcio a maibusor kadagiti Egipcio. Agbibinnusorto dagiti agkakabsat ken kasta met dagiti agkakarruba; aggiginnubatto dagiti siudad kasta met dagiti pagarian.
“Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
3 Kumapuyto ti espiritu ti Egipto. Dadaelekto ti balakadda kenkuana uray pay nakiumanda kadagiti didiosen, kadagiti espiritu dagiti natay a tattao, kadagiti mangan-anito ken kadagiti mammuyon.
Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
4 Iyawatkonto dagiti Egipcio iti ima ti maysa a nakuspag nga amo, ket iturayanto ida ti maysa a nabileg nga ari—daytoy ti pakaammo ti Apo, ni Yahweh a Mannakabalin-amin.”
Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
5 Agmaganto dagiti danum iti baybay ken agmaganto ti karayan ket maawan dagiti linaonna.
Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
6 Bumangsitto dagiti karayan; bumassit ken agmaganto dagiti waig ti Egipto; magangonto dagiti runruno ken tanubong.
Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
7 Dagiti runruno iti igid ti Karayan Nilo, iti wangawangan iti Nilo, ken dagiti amin a namulaan a taltalon iti Nilo ket agmaganto, agbalinto a tapok ket maiyanginto.
ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
8 Agdung-aw ken agladingitto dagiti mangngalap, ken agladingitto dagiti amin nga agbanniit iti Karayan Nilo a kas iti panagladingit dagiti mangiwayat iti iket kadagiti danum.
Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
9 Pumusyawto dagiti trabahador iti pagabelan ken dagiti agab-abel iti puraw a lupot.
Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
10 Agladingitto dagiti agab-abel iti lupot idiay Egipto; ken agladingitto dagiti amin a matangtangdanan nga agtrabaho.
Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
11 Naan-anay a maag dagiti prinsipe ti Zoan. Nagbalin nga awan mamaayna dagiti balakad dagiti kasisiriban a mammagbaga ti Faraon. Nangal-alaam iti turedmo a mangibaga iti Faraon, “Siak ti putot a lalaki dagiti masirib a lallaki, putot a lalaki dagiti nagkakauna nga ar-ari?”
Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
12 Sadino ngarud ti ayan dagiti masirib a tattaoyo? Ibagada koma ngarud kadakayo ken ipakaammoda dagiti plano ni Yahweh a Mannakabalin-amin maipapan iti Egipto.
Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
13 Nagbalin a maag dagiti pangulo ti Zoan, naallilaw dagiti prinsipe ti Memfis; inyaw-awanda ti Egipto, isuda a pasuli a bato dagiti tribuna.
Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
14 Nangikabil ni Yahweh iti espiritu ti panangallilaw iti nagtetengaanna ket inyaw-awanda ti Egipto iti amin nga ar-aramidenna, kaiyariganna ti maysa a nabartek nga agibar-ibar iti sarwana.
Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
15 Awan ti maaramidan ti siasinoman maipaay iti Egipto, ulo man wenno ipus, sanga ti palma wenno runo.
Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
16 Iti dayta nga aldaw, agbalinto dagiti Egipcio a kasla kadagiti babbai. Agtigerger ken agbutengdanto gapu iti nakalayat nga ima ni Yahweh a Mannakabalina-amin nga intag-ayna kadakuada.
Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
17 Agbalinto a pagbutbutngan ti Egipto ti daga ti Juda. Tunggal ipalagip kadakuada ti siasinoman ti maipanggep iti Juda, agbutengdanto, gapu iti plano ni Yahweh a pangpanggepenna maibusor kadakuada.
Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
18 Iti dayta nga aldaw, addanto iti lima a siudad iti daga ti Egipto nga agsao iti pagsasao ti Canaan ken agsapatadanto a ni Yahweh a Mannakabalin-amin ti pagserbianda. Maawaganto ti maysa kadagitoy a siudad iti Siudad ti Init.
Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
19 Iti dayta nga aldaw, addanto altar a maipaay kenni Yahweh iti tengnga ti daga ti Egipto, ken maysa a dakkel nga adigi a bato iti beddeng ni Yahweh.
Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
20 Agbalinto daytoy a pagilasinan ken pammaneknek kenni Yahweh a Mannakabalin-amin iti daga ti Egipto. No umasugda kenni Yahweh gapu kadagiti mangidaddadanes, mangibaonto isuna kadakuada iti mangisalakan ken mangispal ket ispalennanto ida.
Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
21 Mabigbigto ni Yahweh idiay Egipto, ket maam-ammonto dagiti Egipcio ni Yahweh iti dayta nga aldaw. Agdayawdanto nga addaan kadagiti daton ken sagsagut, ken agkaridanto kenni Yahweh ket tungpalendanto dagitoy.
Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
22 Dusaento ni Yahweh ti Egipto, dusaen ken paimbagenna ida. Agsublidanto kenni Yahweh; denggennanto ti kararagda ket paimbagennanto ida.
Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
23 Iti dayta nga aldaw, addanto iti kalsada manipud iti Egipto agingga idiay Asiria ket makapanto dagiti taga-Asiria idiay Egipto, ken makapanto dagiti Egipcio idiay Asiria; ket makipagdaydayawto dagiti Egipcio kadagiti taga-Asiria.
Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
24 Iti dayta nga aldaw, ti Israel ket agbalinto a maikatallo iti Egipto ken Asiria, maysa a bendision iti entero a daga;
Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
25 bendisionanto ida ni Yahweh a Mannakabalin-amin ket kunaenanto, “Mabendisionan ti Egipto, a tattaok; ti Asiria nga aramid dagiti imak; ken ti Israel, a tawidko.”
Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”

< Isaias 19 >