< Isaias 16 >

1 Mangipatulodkayo kadagiti kalakian a karnero iti mangiturturay iti daga manipud Sela idiay let-ang, iti bantay ti anak a babai ti Sion.
Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
2 Kas kadagiti billit nga agalla-alla, kas iti umok a nawara-wara, kastanto dagiti babbai iti Moab iti pagballasiwan ti karayan Arnon.
Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
3 Mangtedkayo iti bilin, ipatungpalyo ti hustisia; mangipaaykayo kadagiti linong a kasla rabii iti tengnga ti aldaw; ilemmengyo dagiti aglemlemmeng; saanyo a liputan dagiti adda ilemlemmenganna.
Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
4 Ipalubosyo a makipagnaed kadakayo dagiti kimmamang manipud iti Moab; agbalinkayo a lugar a paglemmengan para kadakuada manipud iti manangdadael.” Ta agsardengto ti panangidadanes ken agpatingganto ti pannakadadael, dagiti mangipayatpayat ket mapukawto manipud iti daga.
Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
5 Maibangonto ti maysa a trono iti kinapudno ti tulag; ket maysa a tao manipud iti tolda ni David ti sipupudno nga agtugawto sadiay. Mangukomto isuna kas panangipatungpalna iti hustisia ken panangaramidna iti kinalinteg.
Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
6 Nangngeganmi ti kinatangsit ti Moab, ti kinakuspagna, ti kinapalangguadna ken ti pungtotna. Ngem ti kinapalangguadna ket ubbaw a sasao.
Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
7 Isu nga agdung-aw ti Moab gapu iti Moab, agdung-aw ti amin a tattao. Agladingitkayo gapu kadagiti tinapay a pasas ti Kir Heres a naan-anay a nadadael.
Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
8 Natikag dagiti taltalon ti Hesbon kasta met a nagango dagiti lanut ti ubas ti Sibma. Impayatpayat dagiti mangiturturay kadagiti nasion dagiti nalangto a lanut a dimmanon idiay Jazer ken nagsaknap iti disierto. Nagsaknap dagiti saringitna iti sabali a pagilian; dimmanon dagitoy iti ballasiw ti taaw.
Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
9 Pudno, makipagsangitakto iti Jazer gapu iti kaubasan ti Sibma. Sibugankayonto kadagiti luluak, Hesbon ken Eleale. Ta pinagpatinggakon dagiti pukkaw gapu iti rag-o kadagiti taltalon iti tiempo ti panagapit kadagiti bungbunga iti panawen ti kalgaw.
Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
10 Mapukawto ti kinaragsak ken rag-o manipud iti kakaykaywan dagiti kayo nga agbunga; ken awanto ti kankanta wenno dirdir-i gapu iti rag-o kadagiti kaubasanyo. Awanto ti agpespes iti arak kadagiti pagpespesan; pinasardengkon ti dir-i gapu iti ragragsak.
Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
11 Isu nga agsensennaay toy pusok a kasla arpa gapu iti Moab ken ti kaunggak gapu iti Kir Heres.
Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
12 No agbannog ti Moab a mapan iti nangato a disso ken sumrek iti templona tapno agkararag, awanto iti pagmaayan dagiti kararagna.
Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
13 Kastoy ti sao nga imbaga ni Yahweh maipanggep iti Moab iti naglabas.
Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
14 Agsasao manen ni Yahweh, “Iti las-ud iti tallo a tawen, mapukawto ti dayag ti Moab; iti laksid dagiti adu a tattaona, manmanonto laeng dagiti mabati ken awanto ti gawayda.
Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”

< Isaias 16 >