< Isaias 11 >
1 Addanto iti rusing a rumuar manipud iti ramut ni Jesse, ken agbunganto iti maysa a sanga manipud iti ramutna.
Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.
2 Agtaengto kenkuana ti Espiritu ni Yahweh, ti espiritu ti kinasirib ken pannakaawat, ti espiritu ti paglintegan ken kinabileg, ti espiritu ti pannakaammo ken panagbuteng kenni Yahweh.
Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu, Mzimu wauphungu ndi wamphamvu, Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.
3 Ti ragsaknanto ket ti panagbuteng iti Apo; saanto isuna a mangukom babaen iti makitkitana wenno mangikeddeng babaen iti mangmangngegna.
Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa. Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso, kapena kugamula mlandu potsata zakumva;
4 Ngem ketdi, ukomennanto iti nalinteg a wagas dagiti nakurapay ken mangngedddengto iti patas para kadagiti napakumbaba iti daga. Dusaennanto ti daga babaen iti pang-or ti ngiwatna, ken babaen iti anges ti bibigna, papatayennanto dagiti nadangkes.
koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo, adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi. Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake; atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.
5 Kinalintegto ti barikes ti siketna, ken ti kinapudnonto ti barikes ti patongna.
Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.
6 Makipagnaedto ti lobo iti karnero, ken agabayto nga agidda ti leopardo ken ti urbon a kalding, ti urbon a baka, ti urbon a leon ken ti napalukmeg a baka. Idauloanto ida ti maysa a bassit nga ubing.
Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa, kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi, mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.
7 Agkaduanto nga agarab ti baka ken oso, ken agaabayto nga agidda dagiti urbonda. Manganto ti leon iti garami a kas iti baka.
Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi, ana awo adzagona pamodzi, ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.
8 Agay-ayamto ti maladaga iti abut ti uleg, ken ikabilto ti napusot nga ubing ti imana iti balay ti karasaen.
Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba, ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.
9 Saandanto a mangdangran wenno mangdadael kadagiti amin a nasantoan a bantayko; ta mapunnonto ti lubong iti pannakaammo kenni Yahweh, a kas iti panagsaknap ti danum iti baybay.
Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga pa phiri lopatulika la Yehova, pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.
10 Iti dayta nga aldaw, tumakderto ti ramut ni Jesse a kas maysa a wagayway para kadagiti tattao. Birukento isuna dagiti nasion, ket napintasto ti disso a paginanaanna.
Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero.
11 Iti dayta nga aldaw, iyunnatto manen ti Apo ti imana tapno sublienna ti natda kadagiti tattaona a nagtalinaed iti Asiria, Egipto, Patros, Cush, Elam, Shinar, Hamat, ken dagiti isla iti baybay.
Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.
12 Mangipasdekto isuna iti wagayway para kadagiti nasion ket ummongennanto dagiti napagtalaw iti Israel ken dagiti naiwara-wara a taga-Juda manipud kadagiti uppat a suli ti daga.
Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera, ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli; Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.
13 Pasardengennanto ti apal ti Efraim, ken mailaksidto dagidiay bumusbusor iti Juda. Saanto nga umapal ti Efraim iti Juda, ken saanton a bumusor ti Juda iti Efraim.
Nsanje ya Efereimu idzatha, ndipo adani a Yuda adzatha; Efereimu sadzachitira nsanje Yuda, ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.
14 Ngem ketdi, rautendanto dagiti turturod ti Filistia iti laud, ken agmaymaysadanto a mangsamsam kadagiti sanikua dagiti tattao iti daya. Rautendanto ti Edom ken Moab, ket agtulnogto kadakuada dagiti tattao ti Ammon.
Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo; ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa. Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu, ndipo Aamoni adzawagonjera.
15 Dadaelento a naan-anay ni Yahweh ti gulpo iti baybay ti Egipto. Babaen iti makasinit nga angin, ipayapaynanto ti imana iti Karayan Eufrates ket guduaennanto daytoy iti pito a karayan tapno mabalin a ballasiwen daytoy a nakansandalias.
Yehova adzaphwetsa mwendo wa nyanja ya Igupto; adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha pa mtsinje wa Yufurate. Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.
16 Addanto kalsada para kadagiti nabati kadagiti tattaona nga agsubli manipud iti Asiria, kas iti kaadda ti dalan a naipaay iti Israel idi agsubsublida manipud iti daga ti Egipto.
Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira amene anatsalira ku Asiriya, monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli pamene amachokera ku Igupto.