< Isaias 1 >

1 Ti Sirmata ni Isaias a putot ni Amos, a nakitana maipapan iti Juda ken Jerusalem, kadagidi al-aldaw da Uzzias, Jotam, Acaz ken Ezekias a nagbalin nga ar-ari ti Juda.
Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
2 Dumngegkayo a langlangit, ken denggem, daga; ta nagsao ni Yahweh: “Nangaywan ken nangpadakkelak kadagiti ubbing, ngem nagsukirda kaniak.
Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi! Pakuti Yehova wanena kuti, “Ndinabala ana ndi kuwalera, koma anawo andiwukira Ine.
3 Ammo ti baka ti akin-kukua kenkuana, ken ammo ti asno iti pagpakanan ti amona, ngem saan nga ammo ti Israel, awan pannakaawat ti Israel.”
Ngʼombe imadziwa mwini wake, bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake, koma Israeli sadziwa, anthu anga samvetsa konse.”
4 Asika pay a nasion, managbasol, tattao a nailumlom iti kinadangkes, anak dagiti managdakdakes, annak nga agtigtignay a sidadakes! Tinallikudanda ni Yahweh, linaisda ti Nasantoan a Dios ti Israel, pinagbalinda a gangannaet dagiti bagbagida manipud kenkuana.
Haa, mtundu wochimwa, anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoyipa, ana odzipereka ku zoyipa! Iwo asiya Yehova; anyoza Woyerayo wa Israeli ndipo afulatira Iyeyo.
5 Apay ketdin a ti pakabautanyo ti birbirukenyo? Apay ta itultuloyyo ti panagsukiryo? Ti sibubukel nga ulo ket masakit, ti sibubukel a puso ket nakapuy.
Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe? Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira? Mutu wanu wonse uli ndi mabala, mtima wanu wonse wafowokeratu.
6 Manipud iti dapan agingga iti ulo, awan ti paset a saan a nadangran: pasig a sugsugat, litlitem, ken silulukat a sugsugat; saanda pay a nagserra, nadalusan, nabedbedan, wenno saan pay a naagasan iti lana.
Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu palibe pabwino, paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu, mabala ake ngosatsuka, ngosamanga ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
7 Nadadael ti pagilianyo; napuoran dagiti siudadyo, dagiti taltalonyo-iti presensiayo-daddadaelen dagitoy dagiti ganggannaet-nadadael ken napanawan, pinarmek dagiti ganggannaet.
Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; minda yanu ikukololedwa ndi alendo inu muli pomwepo, dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
8 Napanawan ti anak ti Sion a kasla kalapaw iti maysa a kaubasan, kasla paglinungan iti nakaimulaan dagiti pipino, kasla nalakub a siudad.
Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha ngati nsanja mʼmunda wampesa, ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka, ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
9 No saan a nagibati ni Yahweh a Mannakabalin-amin iti bassit kadatayo, nagbalintayo koman a kasla iti Sodoma, mabalin a nagbalintayo koman a kasla iti Gomora;
Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira opulumuka, tikanawonongeka ngati Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
10 Denggenyo ti sao ni Yahweh, dakayo a mangiturturay iti Sodoma; dumngegkayo iti linteg ti Diostayo, dakayo a tattao iti Gomora:
Imvani mawu a Yehova, inu olamulira Sodomu; mverani lamulo la Mulungu wathu, inu anthu a ku Gomora!
11 “Ania ngay koma ti serbi kaniak dagiti adu a sagsagutyo?” kinuna ni Yahweh. “Naumaakon kadagiti daton a mapuoran a kalakian a karnero, ken iti taba dagiti napalukmeg nga ay-ayup; ken saanko a pagragsakan ti dara dagiti bulog a baka, karnero, wenno kalding.
Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka?” “Zandikola nsembe zanu zopsereza za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa; sindikusangalatsidwanso ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
12 No kasta nga umaykayo dumatag iti sangoanak, siasino ti nangkiddaw kadakayo iti daytoy, a baddekanyo dagiti paraangak?
Ndani anakulamulirani kuti mubwere nazo pamaso panga? Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
13 Saankayon a mangiyeg kadagiti awan serserbina a sagsagut; makarimon kaniak ti insenso; ti panangrambakyo iti baro a bulan ken panagtitiponyo iti Aldaw ti Panaginana-saanko a maanusan no kasta nga agtitiponkayo gapu kadagiti dakes nga ar-aramidenyo.
Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
14 Kagurak ti panangrambakyo iti baro a bulan ken dagiti naikeddeng a fiestayo; dadagsen dagitoy kaniak; nabannogakon a mangib-ibtur kadagitoy.
Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera; ndatopa kuzinyamula.
15 Isu a tunggal ingatoyo dagiti imayo nga agkararag, ilingedko dagiti matak kadakayo; uray no mangipaaykayo iti adu a karkararag, saanakto a dumngeg; napno iti dara dagiti imayo.
Mukamatambasula manja anu popemphera, Ine sindidzakuyangʼanani; ngakhale muchulukitse mapemphero anu, sindidzakumverani. Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
16 Agbuggokayo, dalusanyo dagiti bagbagiyo; ikkatenyo dagiti dakes nga aramidyo manipud iti imatangko; isardengyo ti kinadakesyo;
sambani, dziyeretseni. Chotsani pamaso panu ntchito zanu zoyipa! Lekani kuchita zoyipa,
17 sursuroenyo ti agaramid iti naimbag; ipakatyo ti hustisia, tulunganyo dagiti maidaddadanes, ikalinteganyo dagiti ulila iti ama, salaknibanyo dagiti balo.”
phunzirani kuchita zabwino! Funafunani chilungamo, thandizani oponderezedwa. Tetezani ana amasiye, muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
18 “Umaykayo ita, ta aglilinnawagtayo,” kuna ni Yahweh; “uray no dagiti basolyo ket kasla naraniag a nalabaga, pumurawdanto a kasla niebe; uray no nalabagada a kasla karmesi, kasladanto kapuraw iti dutdot.
Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.
19 No natulok ken natulnogkayo, kanenyonto ti naimbag nga apit iti daga.
Ngati muli okonzeka kundimvera mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
20 ngem no agkedked ken agsukirkayo, alun-onennakayonto ti kampilan,” ta ti ngiwat ni Yahweh ti nangisao iti daytoy.
koma mukakana ndi kuwukira mudzaphedwa ndi lupanga.” Pakuti Yehova wayankhula.
21 Nagkas-angen ta nagbalinen a balangkantis ti napudno a siudad! Napnoan isuna iti hustisia- napnoan isuna iti kinalinteg, ngem ita napnoan isunan kadagiti mammapatay.
Taonani momwe mzinda wokhulupirika wasandukira wadama! Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama; mu mzindamo munali chilungamo, koma tsopano muli anthu opha anzawo!
22 Ti pirakmo ket nagbalin a narugit, ti arakmo ket nalaokan iti danum.
Siliva wako wasanduka wachabechabe, vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
23 Dagiti prinsipem ket nasukir ken kakadua dagiti mannanakaw; pagaayat ti amin ti pasuksok ken gunguna. Saanda nga ikalkalintegan dagiti ulila iti ama, ken dagiti darum dagiti balo ket saan a makagteng kadakuada.
Atsogoleri ako ndi owukira, anthu ogwirizana ndi mbala; onse amakonda ziphuphu ndipo amathamangira mphatso. Iwo sateteza ana amasiye; ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
24 Isu a daytoy ti pakaammo ti Apo, ni Yahweh a Mannakabalin-amin, a Mannakabalin a Dios ti Israel: Asida pay! Agibalesakto kadagiti kabusorko, ket balsek dagiti kabusorko;
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu, Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti, “Haa, odana nane ndidzawatha, ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
25 iturongkonto ti imak a maibusor kadakayo, dalusak dagiti rugityo, ken ikkatek amin ti kinarugityo.
Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe; ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa, monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
26 Isublikto dagiti ukomyo a kas idi un-unana, ken dagiti mammagbagayo a kas idi punganay; kalpasan dayta, maawagankanto a siudad ti kinalinteg, maysa a napudno nga ili.”
Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana, aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja. Kenaka iweyo udzatchedwa mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.”
27 Masubbotto ti Sion babaen iti hustisia, ken dagiti tattaona nga agbabawi babaen iti kinalinteg.
Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama, anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
28 Madadaelto a sangsangkamaysa dagiti nasukir ken managbasol, ken mapapatayto dagiti tumallikud kenni Yahweh.
Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi, ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
29 “Ta mabainkayonto gapu kadagiti nasagradoan a lugo a kaykayo a tinarigagayanyo, ket mabainankayto gapu kadagiti minuyongan a piniliyo.
“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani; mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene munayipatula.
30 Ta kaiyariganyonto ti kayo alugo a magango dagiti bulongna, ken kasla minuyongan nga awan iti danumna.
Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
31 Ti napigsa a tao ket kaslanto nagango a kayo ken ti aramidna ket kas iti risak; mapuoranda nga agpada, ket awanto ti mang-iddep kadakuada.”
Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma, ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali; motero zonse zidzayakira limodzi, popanda woti azimitse motowo.”

< Isaias 1 >