< Oseas 4 >

1 Denggenyo ti sao ni Yahweh, dakayo a tattao ti Israel. Addaan ti pammabasol ni Yahweh kadagiti agnanaed iti daga, gapu ta awanen ti napudno kadakayo, ken awanen ti napudno iti tulag, awanen ti pannakaammoyo iti Dios iti daga.
Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
2 Adda ti panangilunod, panagulbod, pammapatay, panagtakaw, ken pannakikamalala. Sinalungasing dagiti tattao dagiti amin a linteg, ket agsasaruno ti pannakaiparukpok ti dara.
Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
3 Isu nga agmagmaga ti daga, ket kumapkapuy dagiti amin nga agnanaed iti daytoy: dagiti narungsot nga ayup iti tay-ak ken dagiti billit iti tangatang; uray pay dagiti ikan iti baybay ket napukawdan.
Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
4 Ngem saanmo a palubosan ti siasinoman a mangyeg iti darum; saanmo a palubosan a pabasolen ti maysa a tao ti siasinoman. Gapu ta dakayo a papadi ti pabpabasolek.
“Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
5 Maitibkolkayonto a papadi iti aldaw; Maitibkolkto met dagiti profeta a kaduayo iti rabii, ket dadaelekto ti inayo.
Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
6 Madaddadael dagiti tattaok gapu iti kinakurang iti pannakaammo. Gapu ta linaksidyo a papadi ti pannakaammo, laksidendakayonto met a kas papadi kaniak. Gapu ta linipatyo ti lintegko, uray no siak ti Diosyo, lipatekto met dagiti annakyo.
Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
7 No kasano ti panagadu dagiti papadi, ad-adda met ti panagbasolda kaniak. Pagbalinekto a pakaibabainan dagiti dayawda.
Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
8 Agtaraonda iti basol dagiti tattaok; naagumda kadagiti kinadangkesda.
Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
9 Kastanto met laeng kadagiti tattao a kas kadagiti papadi: dusaekto ida amin gapu kadagiti aramidda; pagsagabaekto ida gapu kadagiti aramidda.
Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
10 Mangandanto ngem saanda a mapnek; agbalangkantisdanto ngem saanda nga umado, gapu ta tinalikkudan ken pinanawandak, siak a ni Yahweh.
“Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
11 Ti kinaderrep, arak ken ti baro nga arak ti nangpukaw ti pannakaawatda.
ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12 Makium-uman dagiti tattaok kadagiti didiosenda a kayo, ket agipadpadto kadakuada dagiti sarukodda. Ta inyaw-awan ida ti espiritu ti kinaderrep, ket pinanawandak a Diosda.
za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13 Agidatdatonda kadagiti tapaw dagiti bantay ken agpupuorda iti insenso iti tapaw dagiti turod, iti sirok dagiti kayo a lugo, alamo, ken terebinto gapu ta nasayaat ti linongda. Isu a nagbalangkantis dagiti annakyo a babbai, ken nakikamalala dagiti manugangyo a babbai.
Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
14 Saankonto a dusaen dagiti annakyo a babbai inton pilienda ti pannakikamalala, wenno dagiti manugangyo a babbai inton makikamalalada. Gapu ta ipaay met dagiti lallaki dagiti bagida kadagiti balangkantis, ken agidatagda met kadagiti daton tapno makaaramidda kadagiti dakes nga aramid a kadua dagiti kulto a balangkantis. Isu a madadaelto dagitoy a tattao a saan a makaaw-awat.
“Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
15 Uray no nakikammalalaka, O Israel, saan koma nga agbasol ti Juda. Saankayo a mapan idiay Gilgal, dakayo a tattao; saankayo a sumang-at idiay Bethaven. Ket saankayo nga agikari, “Iti nagan ni Yahweh nga adda iti agnanayon.”
“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16 Gapu ta nagtignay a sisusukir ti Israel, kas iti maysa a nasukir a bumalasang a baka. Kasano ngarud ida a maiturong ni Yahweh iti pagaraban a kas kadagiti urbon a karnero iti tay-ak?
Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17 Nakipagmaymaysa ti Efraim kadagiti didiosen; baybay-am isuna.
Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
18 Uray no naibusen dagiti naingel a mainumda, itultuloyda latta ti makikamkamalala; ay-ayaten met dagiti pangulona dagiti pakaibabainanda.
Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19 Balkutento isuna ti angin kadagiti payyakna; ket mababaindanto gapu kadagiti datdatonda.
Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.

< Oseas 4 >