< Genesis 49 >

1 Ket inayaban ni Jacob dagiti putotna a lallaki ket kinunana, “Aguummongkayo, tapno maibagak kadakayo ti mapasamakto kadakayo iti masakbayan.
Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
2 Aguummong ken dumngegkayo, dakayo nga annak a lallaki ni Jacob. Denggenyo ni Israel nga amayo.
“Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
3 Ruben, sika ti inauna a putotko, ti pigsak ken ti nangrugian ti kinapigsak, naisangsangayan iti kinatan-ok ken naisangsangayan iti kinabileg.
“Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
4 Saan a matengngel a kas iti napigsa ti ayusna a danum, saanto a sika ti kangrunaan, gapu ta simmagpatka iti pagiddaan ti amam. Ket rinugitam daytoy; simmagpatka iti pagtugawak.
Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
5 Agkabsat da Simeon ken Levi. Armas ti kinaranggas dagiti kampilanda.
“Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
6 O kararuak, saanka a mapan iti taripnongda; saanka a makiraman kadagiti saritaanda, gapu ta saan a maiparbeng ti kasta iti pusok. Ta gapu iti pungtotda ket nakapatayda kadagiti lallaki. Para iti pakaragsakanda ti panangpilayda kadagiti bulog a baka.
Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
7 Mailunod koma ti pungtotda, ta nakaro unay— ken ti nalaus a pungtotda, ta naulpit daytoy. Bingayekto ida iti Jacob ken iwaraskonto ida iti Israel.
Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
8 Juda, dayawendakanto dagiti kakabsatmo. Ti imam ket addanto iti tengnged dagiti kabusormo. Agrukobto iti sangoanam dagiti putot ti amam.
“Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
9 Maiyarig ni Juda iti anak ti leon. Anakko, nagsublika manipud kadagiti tinukmaam. Nagrukob isuna, nagkukot a kasla leon, a kasla babai a leon. Adda kadi makaitured a mangriing kenkuana?
Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
10 Saanto a maisina ti setro manipud kenni Juda, wenno ti sarukod ti mangiturturay manipud iti nagbaetan dagiti sakana, agingga nga umay ti Silo. Agtulnogto dagiti nasion kenkuana.
Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
11 Inggalutna ti urbon a kabalyona iti lanut ti ubas, ken ti urbon nga asnona iti napintas a lanut ti ubas, linabaanna dagiti kawesna iti arak, ken ti pagan-anayna iti dara dagiti ubas.
Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
12 Lumabbaganto dagiti matana a kas iti arak, ken dagiti ngipenna a kas kapuraw ti gatas.
Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
13 Agnaedto ni Zabulon iti igid ti baybay. Pagsangladanto isuna dagiti barko, ken dumanonto iti Sidon ti keteganna.
“Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
14 Ni Issacar ket maysa a napigsa nga asno, agid-idda iti baet ti pagapunan dagiti karnero.
“Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
15 Makitana ti nasayaat a lugar a paginanaan ken ti nadam-eg a daga. Irukobna ti abagana iti dadagsen ken agbalin nga adipen iti trabaho.
Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
16 Ukomento ni Dan dagiti tattaona a kas maysa kadagiti tribu ti Israel.
“Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
17 Maiyarigto ni Dan iti uleg nga adda iti igid ti dalan, maysa a nagita nga uleg iti pagnaan a mangkagat kadagiti mukod ti kabalio, a pakaigapuan iti pannakatnag ti nakasakay iti daytoy.
Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
18 Ur-urayek ti panangisalakanmo, Yahweh.
“Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
19 Ni Gad—darupento isuna dagiti mangraraut, ngem darupennanto ida kadagiti mukodda.
“Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
20 Nabaknangto iti taraon ni Aser, ket mangipaayto isuna kadagiti taraon a maipaay iti ari.
“Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
21 Ugsa a siwawaya iti kaiyarigan ni Neftali; maaddaanto isuna kadagiti napipintas nga annak.
“Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
22 Nabunga a sanga iti kaiyarigan ni Jose, nabunga a sanga nga asideg iti ubbog, a kimmalay-at iti pader dagiti sangana.
“Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
23 Darupento isuna dagiti pumapana ket panaendanto ken riribukenda isuna.
Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
24 Ngem agtalinaedto a nalagda ti bai ti panana ken nabilegto dagiti imana gapu kadagiti ima ti Mannakabalin a Dios ni Jacob, gapu iti nagan ti Agpaspastor, ti Bato ti Israel.
Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
25 Gapu iti Dios ti Amam, a tumulongto kenka, ken gapu iti Mannakabalin a Dios, a mangbendisionto kenka kadagiti bendision iti tangatang, kadagiti bendision ti danum nga aggapu iti uneg ti daga, kadagiti bendision dagiti barukong ken aanakan.
Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
26 Dagiti bendision ti amam ket dakdakkelto ngem dagiti nagkakauna a banbantay wenno kadagiti makaay-ayo a banbanag kadagiti agnanayon a turturod. Addanto dagitoy iti ulo ni Jose, dagiti bendision a mangkorona iti ulo ti nagbalin a prinsipe a nangidaulo kadagiti kakabsatna a lallaki.
Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
27 Ni Benjamin ket maysa a mabisin a lobo. Iti agsapa, alun-onenna ti natiliwna, ken iti rabii, bingayenna ti nasamsamda.”
“Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
28 Dagitoy dagiti sangapulo ket dua a tribu ti Israel. Kastoy ti imbaga ti amada kadakuada idi binendisionanna ida. Binendisionanna ti tunggal maysa iti maitutop a bendision.
Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
29 Kalpasanna, binilinna ida a kinunana kadakuada, “Dandanin ti ipupusayko. Itabondak iti nakaitaneman dagiti kapuonak iti rukib nga adda idiay talon ni Efron a Heteo,
Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
30 iti rukib nga adda iti talon idiay Macpela, nga asideg iti Mamre iti daga ti Canaan, ti talon a ginatang ni Abraham a mausar a pagitaneman manipud kenni Efron a Heteo.
Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
31 Intabonda sadiay ni Abraham ken ni Sara nga asawana; intabonda sadiay ni Isaac ken ni Rebeca nga asawana; ken intabonko sadiay ni Lea.
Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
32 Ti talon ken ti rukib nga adda idiay ket nagatang manipud kadagiti tattao a Heteo.
Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
33 Idi nalpasen ni Jacob dagitoy a bilbilinna kadagiti putotna a lallaki, inyunnatna dagiti sakana iti pagiddaan ket inyangesna ti maudi nga angesna, ket pimmusayen.
Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.

< Genesis 49 >