< Genesis 4 >

1 Kinaidda ti lalaki ti asawana a ni Eva. Nagsikog isuna ket impasngayna ni Cain. Kinuna ti babai, “Nangipasngayak iti lalaki babaen iti tulong ni Yahweh.”
Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
2 Kalpasanna, impasngayna ti kabsat ni Cain a ni Abel. Ita, ni Abel ket nagbalin nga agpaspastor, idinto a ni Cain ket nagtrabaho iti daga.
Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
3 Napasamak nga iti panaglabas ti tiempo, nangidatag ni Cain kadagiti bunga ti daga kas daton kenni Yahweh.
Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
4 Ni Abel met ket nangidatag manipud kadagiti umuna nga annak ti arbanna ken kadagiti taba. Inawat ni Yahweh ni Abel ken ti datonna,
Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
5 ngem saanna nga inawat ni Cain ken ti datonna. Isu a nakaunget unay ni Cain, ket nagruppanget isuna.
Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
6 Kinuna ni Yahweh kenni Cain, “Apay ngay met a makaunget ken nakaruppangetka?
Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
7 No ar-aramidem ti umno, saanka kadi nga awaten? Ngem no saanmo nga ar-aramiden ti umno, agur-uray ti basol iti ruangan ket tartarigagayannaka a tenglen, ngem masapul nga iturayam daytoy.”
Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
8 Nakisarita ni Cain iti kabsatna a ni Abel, ket kabayatan nga addada iti kataltalunan, dinuklos ni Cain ti kabsatna a ni Abel ket pinatayna isuna.
Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
9 Kalpasanna, kinuna ni Yahweh kenni Cain, “Sadino ti ayan ti kabsatmo a ni Abel?” Kinunana, “Saanko nga ammo. Siak aya ti para-aywan iti kabsatko?”
Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
10 Kinuna ni Yahweh, “Ania ti inaramidmo? Umaw-awag kaniak ti dara ti kabsatmo manipud iti daga.
Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
11 Ita, nailunodka iti daga, inungapna dagiti ngiwatna a mangawat iti dara ti kabsatmo manipud iti imam.
Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
12 Manipud ita, no sukayem ti daga, saanna nga ipaay ti pigsana kenka. Aglemmelemmeng ken agalla-allakanto iti daga.”
Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
13 Kinuna ni Cain kenni Yahweh,” Ti dusak ket dakdakkel ngem iti kabaelak.
Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
14 Pudno, iti daytoy nga aldaw ket pinatalawnakon manipud iti daytoy a daga ket mailemmengakto manipud iti rupam. Aglemmelemmeng ken agalla-allaakto iti daga, ket siasinoman a makasarak kaniak ket patayennak.”
Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
15 Kinuna ni Yahweh kenkuana, “No addaman ti mangpapatay kenni Cain, mabalesto isuna iti maminpito a daras.” Kalpasanna, minarkaan ni Yahweh ni Cain, tapno saanto isuna a dangran ti siasinoman a tao a makasarak kenkuana.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
16 Isu a pimmanaw ni Cain manipud iti presensia ni Yahweh ket nagnaed iti daga iti Nod, iti daya iti Eden.
Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
17 Kinaidda ni Cain ti asawana ket nagsikog. Impasngayna ni Enoc. Nangibangon isuna iti siudad ket pinanagananna daytoy nga insurotna iti nagan ti putotna a ni Enoc.
Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
18 Naaddaan ni Enoc iti putot ket isu ni Irad. Naaddaan ni Irad iti putot ket isu ni Mehujael. Naaddan ni Mehujael iti putot ket isu ni Metusael. Naaddaan ni Metusael iti putot ket isu ni Lamec.
Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
19 Dua iti inasawa ni Lamec: Ada ti nagan ti maysa ken Zilla met ti nagan ti maysa.
Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
20 Impasngay ni Ada ni Jabal. Isuna ti ama dagiti agnanaed kadagiti tolda nga addaan kadagiti taraken nga ayup.
Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
21 Jubal ti nagan ti kabsatna a lalaki. Isuna ti ama dagiti agtuktukar iti arpa ken plauta.
Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
22 Ni Zilla met, impasngayna ni Tubal Cain, nga agpanpanday kadagiti alikamen a tanso ken landok. Ti kabsat a babai ni Tubal Cain ket ni Naama.
Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
23 Kinuna ni Lamec kadagiti assawana, “Ada ken Zilla, dummegkayo iti timekko; dakayo nga assawa ni Lamec, dumngegkayo iti ibagak. Ta nakapatayak iti lalaki gapu iti panangsugatna kaniak, maysa nga agtutubo a lalaki gapu ta dinunornak.
Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
24 No ni Cain ket naibales iti naminpito a daras, pudno a maibales ni Lamec iti pitopulo ket pito a daras.”
Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
25 Kinaidda manen ni Adan ti asawana ket naganak iti maysa pay a lalaki. Pinanaganan ni Eva dayta iti Set ket kinunana, “Inikkannak ti Dios iti maysa pay nga anak a lalaki a kasukat ni Abel, ta pinatay isuna ni Cain.”
Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
26 Naaddaan ni Set iti putot ket pinanagananna iti Enos. Kalpasanna, ket inrugi dagiti tattao nga immawag iti nagan ni Yahweh.
Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

< Genesis 4 >