< Genesis 39 >

1 Naipan ni Jose iti Egipto. Ti Egipcio a ni Potifar, a maysa nga opisial iti Faraon ta isu ket kapitan dagiti guardia, ginatangna ni Jose manipud kadagiti Ismaelita a nangipan kenkuana sadiay.
Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
2 Adda ni Yahweh kenni Jose. Isuna ket narang-ay a tao. Adda isuna iti balay ti amona nga Egipcio.
Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
3 Nakita ti apona nga adda ni Yahweh kenkuana ken pinarang-ay ni Yahweh ti tunggal banag nga inaramidna.
Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
4 Nagbalin ngarud ni Jose a makaay-ayo iti imatang ti apona. Nagserbianna ni Potifar. Pinagbalin ni Potifar ni Jose a mangimaton iti isuamin nga adda iti balayna, ket amin a sanikuana, impaaywanna kenni Jose.
Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
5 Napasamak a manipud iti tiempo a pinagbalin ni Potifar ni Jose a mangimaton iti balayna ken iti amin a sanikuana, a binendisionan ni Yahweh ti balay ti Egipcio gapu kenni Jose. Ti bendision ni Yahweh ket adda kadagiti amin nga adda iti balay ken taltalon ni Potifar.
Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
6 Impaaywan ni Potifar dagiti amin nga adda kenkuana kenni Jose. Saannan a masapul a panunoten pay ti maipapan iti aniaman a banag malaksid ti taraon a kanenna. Ita, ni Jose ket nataer ken nabaked.
Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
7 Napasamak kalpasan daytoy, a ni Jose ket pinaggarteman ti asawa ti apona. Kinunana, “Kaiddaennak.”
Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
8 Ngem nagkedked isuna ket kinunana iti asawa ti apona, “Kitaem, saan a pakibibbiangan ti apok no ania ti aramidek iti balay, ken amin a sanikuana ket impaaywanna kaniak.
Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
9 Awan ti siasinoman a nangatngato kaniak iti daytoy a balay. Awan iti aniaman a saanna nga intalek kaniak malaksid kenka, gapu ta sika ket asawana. Apay ketdin nga aramidek daytoy a nakaro a kinadakes a pakabasulak iti Dios?”
Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
10 Inaldaw a makikisao isuna kenni Jose, ngem nagkedked isuna a makikaidda wenno makikaddua kenkuana.
Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
11 Napasamak iti maysa nga aldaw a simrek isuna iti balay tapno aramidenna ti trabahona. Awan kadagiti lallaki iti balay ti adda iti balay.
Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
12 Ginammatanna isuna babaen kadagiti kawesna ket kinunana, “Kaidddaennak.” Timmaray ni Jose a napan iti ruar, ket nabatina ti kawesna iti ima ti babai.
Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
13 Napasamak nga idi nakita ti asawa ni Potifar a nabati ni Jose ti kawesna iti ima daytoy ken timmaray iti ruar,
Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
14 immawag isuna kadagiti lallaki iti balayna ket imbagana kadakuada, “Kitaenyo, nangiserrek ditoy ni Potifar iti Hebreo a manglais kadatayo. Sinerreknak tapno kaiddaenak, ket nagikkisak.
iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
15 Napasamak nga idi nangngegna a nagikkisak, timmaray iti ruwar ket nabatina ti kawesna kaniak.”
Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
16 Inkabilna ti kawesna iti sibayna agingga a nagawid ti apona.
Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
17 Imbagana kenkuana daytoy a palawag, “Ti adipen a Hebreo nga inyegmo kadakami, sinerreknak tapno gundawayannak.
Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
18 Ket napamasak nga idi nagikkisak, timmaray iti ruar ket nabatina ti kawesna kaniak.”
Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
19 Napasamak nga idi nangngeg ni Potifar ti palawag nga imbaga ti asawana kenkuana a kunana, “Kastoy ti inaramid kaniak ti adipenmo,” nakapungtot iti kasta unay ni Potifar.
Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
20 Innala ni Potifar ni Jose ket pinaibaludna, iti lugar a nakaibaludan dagiti balud ti ari. Ket adda ngarud isunan iti pagbaludan.
Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
21 Ngem adda ni Yahweh kenni Jose ken impakitana kenkuana a napudno isuna iti tulagna. Nagtignay ni Yahweh iti agbanbantay iti pagbaludan isu a nakasarak ni Jose iti pabor iti imatang daytoy.
koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
22 Intalek ti agbanbantay iti pagbaludan dagiti amin a balud nga adda iti pagbaludan kenni Jose. Aniaman nga ar-aramidenda idiay, naitalek kenni Jose dagitoy.
Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
23 Awan ti pagdanagan ti agbanbantay iti pagbaludan maipapan iti aniaman a banag a naitalek kenni Jose, gapu ta adda ni Yahweh kenkuana. Pinarang-ay ni Yahweh ti aniaman nga inaramidna.
Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

< Genesis 39 >