< Genesis 38 >

1 Napamak nga iti dayta a tiempo ket pinanawan ni Juda dagiti kakabsatna ket nakipagnaed iti maysa nga Adullamita nga agnagan ti Hira.
Pa nthawi imeneyi, Yuda anasiyana ndi abale ake napita kukakhala ndi munthu wina wa ku Adulamu wotchedwa Hira.
2 Naam-ammona idiay ti anak ni Sua a maysa a Canaanita. Inasawana ket kinaiddana daytoy.
Kumeneko, Yuda anaona mwana wamkazi wa munthu wina wa Chikanaani wotchedwa Suwa. Anamukwatira nagona naye malo amodzi.
3 Nagsikog isuna ket nagpasngay iti lalaki. Napanaganan daytoy iti Er.
Iye anatenga pathupi, nabala mwana wamwamuna amene anamutcha Eri.
4 Nagsikog manen isuna ket nagpasngay manen iti lalaki. Pinanagananna daytoy iti Onan.
Anatenganso pathupi nabala mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Onani.
5 Naaddaan manen isuna iti anak a lalaki ket pinanagananna daytoy iti Sela. Idiay Kezib ti nangipasngayanna kenkuana.
Anaberekanso mwana wina wamwamuna ndipo anamutcha Sela. Ameneyu anabadwa Yuda ali ku Kezibi.
6 Nakasarak ni Juda iti iyasawana kenni Er nga inauna a putotna. Ti naganna ket Tamar.
Yuda anamupezera mkazi mwana wake woyamba uja Eri, ndipo dzina la mkaziyo linali Tamara.
7 Nadangkes ni Er nga inauna a putot ni Juda iti imatang ni Yahweh. Isu a pinatay isuna ni Yahweh.
Koma ntchito zoyipa za Eri, mwana wachisamba wa Yuda zinayipira Yehova. Choncho Mulungu anamulanga ndi imfa.
8 Kinuna ni Juda kenni Onan, “Kaiddaem ti asawa ti kabsatmo. Aramidem ti pagrebbengan ti maysa a bayaw ket mangpadakkelka iti anak para iti kabsatmo.”
Pamenepo Yuda anati kwa Onani, “Kwatira mkazi wamasiye wa mʼbale wako. Ulowe chokolo kuti mʼbale wako akhale ndi mwana.”
9 Ammo ni Onan a saannanto a kukua ti ubing. Tunggal kaiddaenna ti asawa ti kabsatna, ibelbellengna ti kissitna iti daga tapno saan isuna a maaddaan ti anak para iti kabsatna.
Koma Onani anadziwa kuti mwanayo sadzakhala wake. Choncho nthawi zonse pamene amagona naye mkaziyo, ankatayira umuna pansi kuti asamuberekere mwana mʼbale wake.
10 Dakes ti inaramidna iti imatang ni Yahweh. Pinatay ngarud met laeng isuna ni Yahweh.
Zimene ankachitazi zinayipira Yehova. Choncho anamulanganso ndi imfa.
11 Ket kinuna ni Juda kenni Tamar a manugangna, “Agtalinaedka a balo iti balay ti amam agingga a dumakkel ti anakko a ni Sela.” Ta napanunotna, “Nalabit a matayto met laeng daytoy a kas kadagiti kakabsatna.” Pimmanaw ni Tamar ket nagnaed iti balay ti amana.
Kenaka Yuda anati kwa mpongozi wake Tamara, “Bwererani ku nyumba ya abambo anu ndi kukhala kumeneko ngati wamasiye mpaka mwana wanga Sela atakula.” Ananena izi chifukwa ankaopa kuti Sela angafenso ngati abale ake aja. Choncho Tamara anapita kukakhala ku nyumba ya abambo ake.
12 Kalpasan ti nabayag a tiempo, natay ti putot ni Sua nga asawa ni Juda. Naliwliwa ni Juda ket napan isuna kadagiti mangpukpukis kadagiti karnerona idiay Timna, kaduana ti gayyemna nga Adullamita a ni Hiran.
Patapita nthawi yayitali, Batishua, mkazi wa Yuda anamwalira. Yuda atatha kulira maliro a mkazi wake, anapita, iyeyu pamodzi ndi bwenzi lake Hira, Mwadulamu uja, ku Timna kumene ankameta nkhosa zawo.
13 Naibaga kenni Tamar, “Ammom, mapan ti katugangam idiay Timna tapno papukisanna dagiti karnerona.”
Tamara atamva kuti apongozi ake akupita ku Timna kukameta nkhosa,
14 Inikkatna ngarud ti kawes ti kinabalona ket inabbunganna ti bagina iti naingpis a lupot ken binalkotna ti bagina. Nagtugaw isuna iti ruangan ti Enaim, nga adda iti igid ti dalan nga agturong idiay Timna. Ta nakitana a dimmakelen ni Sela ngem saan a naiyasawa ni Tamar kenkuana.
iye anavula zovala zake za umasiye, nadziphimba nkhope ndi nsalu kuti asadziwike, ndipo anakhala pansi pa chipata cha ku Enaimu popita ku Timna. Tamara anachita izi chifukwa anaona kuti ngakhale Selayo anali atakula tsopano, iye sanaperekedwe kuti amulowe chokolo.
15 Idi nakita ni Juda isuna, impagarupna a maysa isuna a balangkantis gapu ta inabbunganna ti rupana.
Yuda atamuona anangomuyesa mkazi wadama chabe, chifukwa anadziphimba nkhope.
16 Inasetganna isuna iti igid ti dalan ket kinunana, “Umayka, pangngaasim ta bay-am a kaiddaenka”- ta saanna nga ammo nga isuna ti manugangna- ket kinuna ni Tamar, “Ania ti itedmo kaniak tapno mabalinnak a kaiddaen?”
Tsono anapita kwa mkaziyo pamphepete pa msewu paja nati, “Tabwera ndigone nawe.” Apa Yuda sankadziwa kuti mkazi uja anali mpongozi wake. Ndiye mkazi uja anamufunsa Yuda nati, “Mudzandipatsa chiyani kuti ndigone nanu?”
17 Kinunana, “Mangipatuludak kenka iti urbon a kalding manipud iti arban.” Kinuna ni Tamar, ''Ikkannak kadi iti pakakitaan a mangtedkanto agingga nga ipatulodmo daytoy?”
Iye anati, “Ndidzakutumizira kamwana kambuzi ka mʼkhola mwanga.” Mkaziyo anayankha kuti, “Chabwino, ndavomera, koma mungandipatse chikole mpaka mutanditumizira mbuziyo?”
18 Kinunana, “Ania a pakakitaan ti mabalinko nga ited kenka?” Ket kinuna ni Tamar, “Ti selio, ti tali ken ti sarukod nga adda iti imam.” Intedna dagitoy kenkuana ket nakikaidda kenkuana. Ket nagsikog ni Tamar babaen kekuana.
Iye anati, “Ndikupatse chikole chanji?” Mkaziyo anayankha, “Mundipatse mphete yanuyo, chingwe chanucho pamodzi ndi ndodo imene ili mʼdzanja lanulo.” Choncho anazipereka kwa iye nagona naye ndipo anatenga pathupi.
19 Bimmangon isuna ket pimmanaw. Inikkatna ti abbongna ket inkawesna ti kawes ti kinabalona.
Kenaka Tamara anachoka, navula nsalu anadziphimba nayo ija, navalanso zovala zake za umasiye zija.
20 Impatulod ni Juda ti urbon a kalding iti Adullamita a gayyemna tapno alaenna manipud iti babai ti intedna a pakakitaan a tungpalenna ti karina iti babai, ngem saanna a nasarakan daytoy.
Tsono Yuda anatuma bwenzi lake Mwadulamu uja ndi kamwana kambuzi kaja kuti akapereke kwa mkazi wadama uja, ndi kuti akatero amubwezere chikole chake chija. Koma atafika sanamupezepo.
21 Ket dinamag ti Adulamita kadagiti tattao iti lugar, “Ayan ti balangkantis nga agserserbi iti templo nga adda iti igid ti dalan ti Enaim?” Kinunada, “Awan iti balangkantis nga agserserbi iti templo ditoy.”
Anawafunsa anthu a komweko, “Kodi mkazi wadama uja amene ankakhala pambali pa msewu wa ku Enaimu, ali kuti?” Iwo anayankha, “Sipanakhalepo mkazi wa dama aliyense pano.”
22 Nagsubli ngarud isuna kenni Juda ket kinunana, “Saanko a nasarakan isuna. Kinuna pay dagiti tattao idiay, 'Awan met iti balangkantis nga agserserbi iti templo ditoy.”'
Choncho anabwerera kwa Yuda nati, “Sindinamupeze mkazi uja. Kuwonjeza apo, anthu a kumeneko amati, ‘Sipanakhalepo mkazi wadama pano.’”
23 Kinuna ni Juda, “Bay-am nga idulinna dagiti banbanag nga intedko, maibabainta laeng. Pudno met nga impatulodko daytoy nga urbon a kalding, ngem saanmo isuna a nasarakan.”
Pamenepo Yuda anati, “Mulekeni atenge zinthuzo zikhale zake, kuopa kuti anthu angatiseke. Ine sindinalakwe, ndinamutumizira kamwana kambuzika, koma simunamupeze.”
24 Napasamak a kalpasan iti tallo a bulan, naipadamag kenni Juda, “Nagbalin a balangkantis ni Tamar a manugangmo, ket nagsikog isuna gapu iti daytoy.” Kinuna ni Juda, “Iyegyo isuna ditoy ket puoranyo isuna.”
Patapita miyezi itatu, Yuda anawuzidwa kuti, “Mpongozi wanu Tamara anachita zadama, ndipo zotsatira zake nʼzakuti ali ndi pathupi.” Yuda anati, “Kamutulutseni ndipo mukamutenthe kuti afe!”
25 Idi naiyegdan ni Tamar, nangipatulod isuna iti mensahe iti katuganganna, “Babaen iti tao nga akinkukua kadagitoy a masikogak.” Kinuna ni Tamar, “Pangngaasim ta bigbigem no siasino ti akin kukua kadagitoy, ti selio, ti tali ken ti sarukod.”
Akumutulutsa, iye anatuma mawu kwa apongozi ake. Anati, “Ndili ndi pathupi pa munthu amene ndi mwini wake wa zinthu izi. Taziyangʼanitsitsani, kodi mwini wa khoza, chingwe ndi ndodo yoyenderayi ndi yani?”
26 Nabigbig ni Juda dagitoy ket kinunana, “Ad-adda a nalinteg isuna ngem siak, gapu ta saanko isuna nga impaasawa iti anakko a ni Sela.” Ket saannan a kinaidda pay daytoy.
Yuda anazizindikira zinthuzo ndipo anati, “Uyu ndi wolungama kuposa ine, chifukwa sindinamupereke kwa mwana wanga Sela.” Ndipo Yuda sanagone nayenso.
27 Idi dimteng ti tiempo nga aganaken daytoy, singin gayam ti adda iti aanakanna.
Pamene Tamara nthawi inamukwanira yoti abeleke, mʼmimbamo munali mapasa.
28 Napasamak nga idi agan-anaken isuna, inruar ti maysa ti imana, ket nangala ti agpapaanak iti nalabbaga a sinulid, inggalotna iti ima ti ubing ket kinunana, “Daytoy ti immuna a rimmuar.”
Pamene ankabereka, mmodzi wa iwo anatulutsa dzanja lake. Choncho mzamba anatenga kawulusi kofiira nakamangirira pa mkono pa mwanayo nati, “Uyu ndiye anayamba kubadwa.”
29 Idi insublina ti imana, ti met immuna a rimuar ket ti kabsatna. Kinuna ti agpapaanak, ''Kasano a nakiinnunaka a rimmuar!”
Koma pamene anabweza mkonowo, mʼbale wake anabadwa ndipo mzamba anati, “Wachita kudziphotcholera wekha njira chonchi!” Ndipo anamutcha Perezi.
30 Ket napanaganan daytoy iti Perez. Kalpasanna, rimmuar ti kabsatna nga addaan iti nalabbaga a sinulid iti imana, ket napanagan isuna iti Zera.
Pambuyo pake mʼbale wake amene anali ndi ulusi wofiira pa mkono wake uja anabadwa ndipo anapatsidwa dzina lakuti Zera.

< Genesis 38 >