< Genesis 32 >

1 Intuloy met ni Jacob ti panagdaliasatna, ket sinabat isuna dagiti anghel ti Dios.
Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
2 Idi nakita ida ni Jacob, kinunana, “Daytoy ket kampo ti Dios”, isu nga inawaganna dayta a lugar iti Mahanaim.
Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
3 Nangibaon ni Jacob kadagiti mensahero nga umun-una ngem isuna a mapan iti kabsatna a ni Esau, iti daga ti Seir, iti rehion ti Edom.
Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
4 Binilinna ida, a kunana, “Kastoy ti ibagayo iti apok a ni Esau: Kastoy ti kuna ti adipenmo a ni Jacob: 'Nakipagnanaedak kenni Laban, ket nagtalinaedak a nakipagnanaed aginggana ita.
Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
5 Addaanak kadagiti baka, asno, ken arban, lallaki nga adipen, ken babbai nga adipen. Nangibaonak tapno maibaga daytoy iti apok, tapno makasarakak koma iti pabor iti imatangmo.”'
Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
6 Nagsubli dagiti mensahero kenni Jacob ket kinunada, “Napankami iti kabsatmo a ni Esau. Umaynaka sabten, ket adda kaduana nga uppat a gasut a lallaki.
Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
7 Ket nagbuteng ken nariribukan ni Jacob ti kasta unay. Isu a biningayna dagiti tattao a kaduana iti dua a kampo, ken kasta met dagiti arban ti karnero ken kalding, baka, ken dagiti kamelyo.
Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
8 Kinunana, “No umay ni Esau iti maysa kadagiti kampo ket darupenna daytoy, aglibasto ti maysa a kampo.”
Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
9 Kinuna ni Jacob, “Dios ti amak a ni Abraham, ken Dios ti amak a ni Isaac, Yahweh, a nagkuna kaniak, 'Agsublika iti pagiliam ken kadagiti kakabagiam, ket parang-ayenkanto,'
Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
10 Saanak a maikari iti amin nga aramidmo a nangipakita iti kinapudnom iti katulagan ken iti amin a kinamatalek nga inaramidmo para iti adipenmo. Ta sarukod laeng ti awitko idi bimmallasiwak iti daytoy a Jordan, ket ita nagbalinakon a dua a kampo.
Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
11 Pangnga-asim ta ispalennak manipud iti ima ti kabsatko, manipud iti ima ni Esau, ta mabutengak kenkuana, nga umay isuna ket darupennak ken dagiti inna a kadua dagiti ubbing.
Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
12 Ngem kinunam, 'Pudno a parang-ayenkanto. Pagbalinekto dagiti kaputotam a kasla darat iti baybay, a saan a mabilang iti kinaaduda.”'
Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
13 Nagtalinaed ni Jacob sadiay iti dayta a rabii. Nangala isuna iti sumagmamano kadagiti adda kenkuana a kas sagut a maipaay kenni Esau, a kabsatna:
Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
14 dua gasut a kabaian a kalding ken duapulo a kalakian a kalding, dua gasut a kabaian a karnero ken duapulo a kalakian a karnero,
Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
15 tallopulo nga agpagpagatas a kamelio ken dagiti urbonda, uppat a pulo a kabaian a baka ken sangapulo a kalakian a baka, duapulo a kabaian nga asno ken sangapulo a kalakian nga asno.
ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
16 Impaaywanna dagitoy kadagiti adipenna, maysa nga arban iti tunggal adipen. Kinunana kadagiti adipenna, “Umunakayo kaniak ket ikkanyo iti pagbaetan ti tunggal arban.”
Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
17 Binilinna ti umuna nga adipen, a kunana, “Inton masabatnaka ni Esau a kabsatko ken agsaludsod kenka, a kunana, 'Siasino ti nakaibilangam? Sadino ti papanam? Ken siasino ti makinkukua kadagitoy nga ayup iti sangoanam?'
Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
18 Ket ibagamto a, 'Dagitoy ket kukua ti adipenmo a ni Jacob. Dagitoy ket sagut a naipatulod para iti apok a ni Esau. Ket makitamto, sumarsaruno isuna kadakami,'”
Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
19 Binilin ni Jacob ti maikadua a bunggoy, ti maikatlo, ken dagiti amin a tattao a mangsarsaruno kadagiti arban. Kinunana, “Ibagayo ti isu met laeng a banag kenni Esau inton makitayo isuna.
Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
20 Ibagayo met a, “Sumarsaruno kadakami ti adipenmo a ni Jacob.'” Ta pinanunotna nga, “Ay-ayoek isuna babaen kadagiti sagut nga ummun-una kaniak. Inton makitak isuna, barbareng no awatennakto.”
Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
21 Isu nga immuna a napan dagiti sagut ngem isuna. Nagtalinaed isuna iti dayta a rabii iti kampo.
Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
22 Bimmangon ni Jacob iti dayta a rabii, ket inkuyogna dagiti dua nga assawana, dagiti dua a babai nga adipenna, ken dagiti sangapulo ket maysa a putotna a lallaki. Imbaonna ida iti ballasiw ti waig ti Jabbok.
Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
23 Iti kastoy a wagas, imbaonna ida iti ballasiw ti waig kasta met dagiti amin a sanikuana.
Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
24 Nabati nga agmaymaysa ni Jacob, ket maysa a lalaki ti nakigabbo kenkuana inggana iti panagsingising ti init.
Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
25 Idi nakita ti lalaki a saanna a maabak isuna, dinapigna ti patong ni Jacob. Naglagisi ti patong ni Jacob kabayatan a makigabgabbo isuna kenkuana.
Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
26 Kinuna ti lalaki, “Palubosannakon, ta sumingsingisingen ti init.” Kinuna ni Jacob, “Saanka a palubosan malaksid no bendisionannak.”
Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
27 Kinuna ti lalaki kenkuana, “Ania iti naganmo? Simmungbat ni Jacob, “Jacob.”
Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
28 Kinuna ti lalaki, “Ti naganmo ket saanen a Jacob, no di ket Israel. Ta nakibinnalubalka iti Dios ken kadagiti tattao ket nangabakka.”
Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
29 Sinaludsod ni Jacob kenkuana, “Pangngaasim ta ibagam kaniak ti naganmo.” Kinunana, “Apay a salsaludsudem ti naganko?” Ket binendisionanna isuna sadiay.
Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
30 Pinanaganan ni Jacob ti lugar a Peniel ta kinunana, “Nakitak ti Dios iti rupan-rupa, ket naisalakan ti biagko.”
Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
31 Lumgaken ti init idi pumanaw ni Jacob idiay Peniel. Agpilaypilay isuna gapu iti patongna.
Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
32 Dayta ti makagapu no apay nga agingga iti daytoy nga aldaw ket saan a kankanen dagiti tattao ti Israel ti pennet iti patong nga adda iti nagsuopan iti patong, gapu ta dinangran ti lalaki dagidiay a pennet bayat iti panaglagisi ti patong ni Jacob.
Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.

< Genesis 32 >