< Genesis 3 >

1 Ita, ti uleg ket nasiksikap ngem kadagiti dadduma a narungsot nga ayup iti tay-ak nga inaramid ni Yahweh a Dios. Kinunana iti babai, “Agpayso kadi a kinuna ti Dios a, 'Saankayo a mangmangan manipud iti aniaman a kayo iti minuyongan?”'
Ndipo njoka inali yochenjera kuposa nyama yakuthengo iliyonse imene Yehova Mulungu anapanga. Njokayo inati kwa mkaziyo, “Kodi Mulungu ananenadi kuti, ‘Inu musadye zipatso za mtengo uliwonse mʼmundamu?’”
2 Kinuna ti babai iti uleg, “Mabalinmi a kanen ti bunga manipud kadagiti kayo iti minuyongan,
Mkaziyo anati kwa njokayo, “Tikhoza kudya zipatso za mʼmitengo ya mʼmundawu,
3 ngem maipapan iti bunga ti kayo nga adda iti tengnga ti minuyongan, kinuna ti Dios, 'Saanyo a mabalin a kanen daytoy, wenno sagiden man laeng daytoy, ta no aramidenyo dayta, mataykayo.”'
koma Mulungu anati, ‘Musadye zipatso za mu mtengo umene uli pakati pa munda, ndipo musadzawukhudze kuti mungadzafe.’”
4 Kinuna ti uleg iti babai, “Saan, saankayo a matay.
“Ndithudi simudzafa,” inatero njokayo kwa mkaziyo.
5 Ta ammo ti Dios nga iti aldaw a kanenyo daytoy, malukatan dagiti matayo, ket agbalinkayonto a kas iti Dios, nga ammona ti naimbag ken dakes.”
“Pakuti Mulungu akudziwa kuti tsiku limene mudzadye zipatso za mu mtengowo, maso anu adzatsekuka, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wodziwa zabwino ndi zoyipa.”
6 Ket idi nakita ti babai a ti kayo ket nasayaat a kanen, ken makaay-ayo daytoy iti mata, ken ti kayo ket makapaawis a mangpasirib iti tao, nangala ti babai kadagiti bungana, ket kinnanna daytoy. Ken inikkanna met ti asawana a kaduana, ket kinnanna daytoy.
Pamene mkaziyo anaona kuti mtengowo unali wabwino kudya ndi wokongola ndi kuti unali wopatsa nzeru, anatengako zipatso zake nadya. Zina anamupatsako mwamuna wake amene anali naye pomwepo ndipo naye anadyanso.
7 Agpada a nalukatan dagiti matada, ken naamirisda a lamo-lamoda. Nangdaitda kadagiti bulbulong ti igos ket nangaramidda iti pangabbongda kadagiti bagbagida.
Kenaka maso awo anatsekuka, ndipo anazindikira kuti anali maliseche. Choncho anasoka masamba a mkuyu nadzipangira zovala.
8 Nanggegda ti arimpadek ni Yahweh a Dios iti minuyongan iti kalalammiisan ti aldaw, isu a naglemmeng ti lalaki ken ti asawana manipud iti presensia ti Dios, kadagiti kakay-kaywan iti minuyongan.
Kenaka munthu uja ndi mkazi wake anamva mtswatswa wa Yehova Mulungu akuyendayenda mʼmundamo madzulo a tsikulo, ndipo iwo anabisala pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya mʼmundamo.
9 Immawag ni Yahweh a Dios iti lalaki ket kinunana kenkuana, “Sadino ti ayanmo?”
Yehova Mulungu anayitana munthu uja kuti, “Uli kuti?”
10 Kinuna ti lalaki, “Nanggegko nga addaka iti minuyongan, ket nagbutengak, gapu ta lamo-lamoak. Isu't gapuna a naglemmengak.”
Iye anayankha, “Ndinakumvani mʼmundamo, ndipo ndimaopa chifukwa ndinali maliseche; choncho ndinabisala.”
11 Kinuna ti Dios, “Siasino ti nangibaga kenka a lamo-lamoka? Nanganka kadi manipud iti kayo nga imbilinko a saanmo a mabalin a kanen?”
Ndipo anamufunsa, “Ndani anakuwuza kuti uli maliseche? Kodi wadya zipatso za mtengo umene ndinakulamulira kuti usadye?”
12 Kinuna ti lalaki, “Ti babai nga intedmo a makaduak, inikkannak iti bunga manipud iti kayo, ket kinnanko.”
Koma munthu uja anati, “Mkazi amene munandipatsa kuti ndizikhala nayeyu anandipatsako chipatso cha mtengowo ndipo ndinadya.”
13 Kinuna ni Yahweh a Dios iti babai, “Ania daytoy nga inaramidmo?” Kinuna ti babai, “Inallilawnak ti uleg, ket nanganak.”
Tsono Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, “Wachitachi nʼchiyani?” Mkaziyo anati, “Njoka inandinamiza, ndipo ndinadya.”
14 Kinuna ni Yahweh a Dios iti uleg, “Gapu ta inaramidmo daytoy, mailunodka kadagiti amin a dingwen ken kadagiti amin a narungsot nga ayup iti tay-ak. Aguyaska babaen iti tianmo, ken tapokto ti kanem iti amin nga aldaw ti panagbiagmo.
Choncho Yehova Mulungu anati kwa njokayo, “Popeza wachita zimenezi, “Ndiwe wotembereredwa kuposa ziweto zonse ndi nyama zakuthengo zonse. Udzayenda chafufumimba ndipo udzadya fumbi masiku onse a moyo wako.
15 Mangikabilak iti pagginnuraanyo iti babai, ken iti bukelmo ken ti bukelna. Dunurennanto ti ulom, ken dunuremto ti mukodna.”
Ndipo ndidzayika chidani pakati pa iwe ndi mkaziyo, pakati pa mbewu yako ndi mbewu yake; Iye adzaphwanya mutu wako ndipo iwe udzaluma chidendene chake.”
16 Kinunana met iti babai, “Pakaruek iti kasta unay ti ut-ot iti panaganakmo; iti nakaro a rigat, ipasngaymo dagiti annakmo. Ti tarigagaymonto ket para iti asawam, ngem iturayannakanto.”
Kwa mkaziyo Iye anati, “Ndidzachulukitsa ululu wako kwambiri pamene uli ndi pakati; ndipo udzamva ululu pa nthawi yako yobereka ana. Udzakhumba mwamuna wako, ndipo adzakulamulira.”
17 Kinunana kenni Adan, “Gapu ta dimngegka iti timek ti asawam, ken nanganka manipud iti kayo, maipapan iti imbilinko kenka, a kunak, 'Saanka a mabalin a mangan manipud iti daytoy,' mailunod ti daga gapu kenka; mangankanto manipud iti nagrigatam iti amin nga aldaw ti panagbiagmo.
Ndipo kwa Adamu Mulungu anati, “Chifukwa wamvera mkazi wako ndipo wadya zipatso za mu mtengo umene ndinakulamulira kuti, ‘Usadye.’ “Nthaka yatembereredwa chifukwa cha iwe, movutikira udzadya zochokera mʼnthakamo masiku onse a moyo wako.
18 Mangpataudto daytoy kadagiti sisiit ken balang a mulmula a para kenka, ket kanemto dagiti mula iti tay-ak.
Mʼnthakamo mudzamera minga ndi nthula ndipo udzadya zomera zakuthengo.
19 Babaen iti ling-et iti rupam, mangankanto iti tinapay aginggana nga agsublika iti daga, ta iti daytoy ti naggapuam. Gapu ta tapokka, ket agsublikanto met laeng iti tapok.”
Kuti upeze chakudya udzayenera kukhetsa thukuta, mpaka utabwerera ku nthaka pakuti unachokera kumeneko; pakuti ndiwe fumbi ku fumbi komweko udzabwerera.”
20 Pinanaganan ti lalaki ti asawana nga Eva gapu ta isuna ti ina dagiti amin nga agbibiag a banbanag.
Munthu uja anatcha mkazi wake Hava, chifukwa iyeyu adzakhala mayi wa anthu onse amoyo.
21 Nangaramid ni Yahweh a Dios kadagiti pagan-anay a lalat para kenni Adan ken iti asawana ket kinawesanna ida.
Yehova Mulungu anapangira Adamu ndi mkazi wake zovala zachikopa ndipo anawaveka.
22 Kinuna ni Yahweh a Dios, “Ita, nagbalin a kasla kadatayo ti lalaki, ammona ti naimbag ken dakes. Isu nga ita, masapul a saanen isuna a mapalubusan a mangigaw-at iti imana a mangala manipud iti kayo ti biag, kanenna daytoy, ket agbiag iti agnanayon.”
Ndipo Yehova Mulungu anati, “Tsopano munthu uyu wasanduka mmodzi wa ife, wodziwa zabwino ndi zoyipa. Iyeyu asaloledwe kutambasula dzanja ndi kutengako zipatso za mu mtengo wopatsa moyo uja kuti angakhale ndi moyo mpaka muyaya.”
23 Isu a pinapanaw isuna ni Yahweh a Dios manipud iti minuyongan ti Eden, tapno sukayenna ti daga nga isu ti nakaalaanna.
Kotero Yehova Mulungu anatulutsa Adamu Mʼmunda wa Edeni kuti azilima mʼnthaka imene anachokera.
24 Pinapanaw ngarud ti Dios ti lalaki iti minuyongan, ket nangikabil isuna iti kerubim iti daya ti minuyongan ti Eden, ken umap-apoy a kampilan nga agrikrikos, tapno mabantayan ti dalan nga agturong iti kayo ti biag.
Atamuthamangitsa munthu uja, Yehova anayika Akerubi mbali ya kummawa kwa Munda wa Edeni ndi lupanga lamoto limene limayendayenda ponsepo, kuteteza njira ya ku mtengo wopatsa moyo.

< Genesis 3 >