< Genesis 2 >

1 Ket nalpas dagiti langit ken ti daga, ken dagiti amin nga agbibiag a banbanag a nangpunno kadagitoy.
Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.
2 Iti maika-pito nga aldaw, nalpas ti Dios ti trabahona, isu a naginana isuna iti maika-pito nga aldaw manipud iti amin a trabahona.
Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse.
3 Binendisionan ti Dios ti maika-pito nga aldaw ken imbilangna daytoy a nasantoan nga aldaw, gapu ta iti daytoy, naginana isuna manipud iti amin a trabahona iti panangparsuana.
Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.
4 Dagitoy dagiti pasamak maipapan kadagiti langit ken iti daga, idi naparsua dagitoy, iti aldaw nga inaramid ni Yaweh a Dios ti daga ken dagiti langit.
Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi: Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba,
5 Awan pay ti babassit a kayo ti tay-ak iti daga, ken awan pay ti nagrusing a mulmula iti daga, gapu ta saan pay a pinagtudo ni Yahweh a Dios, ken awan ti tao a mangsukay iti daga.
zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka,
6 Ngem adda angep a nagpangato manipud iti daga ket dinanumanna ti entero a rabaw ti daga.
koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse.
7 Inaramid ni Yahweh a Dios ti tao manipud iti tapuk ti daga, inyangesna iti agongna ti anges ti biag, ket nagbalin a sibibiag a parsua ti tao.
Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.
8 Nangikabil ni Yahweh a Dios iti minuyongan iti dayaen a paset, iti Eden, ket inkabilna sadiay ti lalaki a sinukogna.
Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja.
9 Manipud iti daga, pinadakkel ni Yahweh a Dios ti tunggal kayo a makaay-ayo iti panagkita ken nasayaat a kanen. Nairaman ditoy ti kayo ti biag nga adda idiay tengnga ti minuyongan, ken ti kayo iti pannakaammo iti nasayaat ken dakes.
Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.
10 Adda karayan a rimmuar manipud iti Eden a mangdanum iti minuyongan. Manipud sadiay, nabingay daytoy ket nagbalin nga uppat a karayan.
Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi.
11 Ti nagan ti umuna ket Pison. Daytoy ti agay-ayus iti entero a daga ti Havila, a ditoy ket adda ti balitok.
Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide.
12 Napintas ti balitok iti dayta a daga. Adda met ti bidelio ken ti onix a bato sadiay.
(Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi).
13 Ti nagan ti maikadua a karayan ket Gihon. Agay-ayus daytoy iti entero a daga ti Cus.
Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi.
14 Ti nagan ti maika-tallo a karayan ket Tigris, nga agay-ayus iti daya ti Assur. Ti maika-uppat a karayan ket ti Eufrates.
Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.
15 Innala ni Yahweh a Dios ti tao ket impanna isuna idiay minuyongan ti Eden tapno sukayen ken taripatoenna daytoy.
Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira.
16 Binilin ni Yahweh a Dios ti tao a kunana, “Nawayaka a mangan manipud iti tunggal kayo iti minuyongan.
Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu;
17 Ngem saanka a mangmangan manipud iti kayo ti pannakaammo iti nasayaat ken dakes, ta iti kanito a manganka manipud iti daytoy, awan duadua a matayka.”
koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”
18 Ket kinuna ni Yahweh a Dios, “Saan a nasayaat nga agmaymaysa ti lalaki. Mangaramidak iti kaduana a maitutop kenkuana.”
Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”
19 Manipud iti daga, inaramid ni Yaweh a Dios ti tunggal ayup iti daga ken tunggal tumatayab iti tangatang. Ket inyegna dagitoy iti ayan ti lalaki tapno kitaenna no ania ti iyawagna kadagitoy. Aniaman nga iyawag ti lalaki iti tunggal parsua, dayta ti naganna.
Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake.
20 Pinanaganan ti lalaki dagiti amin a dingwen, dagiti billit iti tangatang, ken ti tunggal narungsot nga ayup nga adda iti tay-ak. Ngem iti lalaki, awan ti nasarakan a kaduana a maitutop kenkuana.
Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse. Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza.
21 Pinaturog ni Yahweh a Dios iti nasimbeng ti lalaki. Nangala ni Yahweh a Dios iti maysa kadagiti paragpagna ket inserrana ti lasag a nangalaanna iti daytoy.
Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu.
22 Babaen iti paragpag nga innala ni Yahweh a Dios manipud iti lalaki, inaramidna ti babai ket inyegna daytoy iti lalaki.
Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.
23 Kinuna ti lalaki, “Ita, daytoy ket tulang dagiti tulangko, ken lasag ti lasagko.” Maawagan isuna a 'babai,' gapu ta naala isuna manipud iti lalaki.
Munthu uja anati, “Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga; adzatchedwa ‘mkazi,’ popeza wachokera mwa mwamuna.”
24 Iti kasta, panawanto iti lalaki ti ama ken inana, makipagmaymaysa isuna iti asawana, ket agbalinda a maymaysa a lasag.
Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.
25 Agpada a lamo-lamo ti lalaki ken ti asawana a babai, ngem saanda a mabain.
Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.

< Genesis 2 >