< Ezra 5 >

1 Kalpasanna, nagipadto babaen iti nagan ti Dios ti Israel da Haggeo a profeta ken Zacarias a putot a lalaki ni Iddo a profeta kadagiti Judio idiay Juda ken Jerusalem.
Nthawi imeneyo aneneri Hagai ndi Zekariya, mwana wa Ido, ankayankhula kwa Ayuda okhala mʼdziko la Yuda ndi mu Yerusalemu mʼdzina la Mulungu wa Israeli, amene anali nawo.
2 Nagsagana ni Zerubbabel a putot a lalaki ni Salatiel ken ni Jesua a putot a lalaki ni Josadac ket rinugianda a bangonen ti balay ti Dios idiay Jerusalem, a kaduada dagiti profeta a nangpabileg kadakuada.
Pambuyo pake Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki ananyamuka nakayambanso kumanga Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Ndipo aneneri a Mulungu anali nawo pamodzi, kuwathandiza.
3 Kalpasanna, immay ni Tatnai a gobernador ti Probinsia iti Ballasiw ti Karayan, ni Setar Bozenai ken dagiti kakaduada, ket kinunada kadakuada, “Siasino ti nangibilin kadakayo a bangonen daytoy a balay ken leppasen dagitoy a pader?”
Pa nthawi imeneyo Tatenai, bwanamkubwa wa chigawo cha patsidya pa Yufurate pamodzi ndi Setari-Bozenai ndi anzawo anapita kwa iwo ndi kukawafunsa kuti, “Anakulolani ndani kuti mumangenso Nyumba imeneyi ndi kutsiriza khoma lake?”
4 Kinunada pay, “Ania ti nagnagan dagiti lallaki a mangibangbangon iti daytoy a balay?”
Anawafunsanso kuti, “Kodi anthu amene akumanga nyumbayi mayina awo ndani?”
5 Ngem ti mata ti Dios ket adda kadagiti panglakayen a Judio, ket saan ida a napasardeng dagiti kabusorda. Ur-urayenda ti maipatulod a surat iti ari ken tapno maipasubli ti maysa a bilin maipapan iti daytoy.
Koma Mulungu wawo amayangʼanira atsogoleri Ayuda, motero kuti anthu aja anaganiza kuti asawaletse kumanga Nyumbayo mpaka atalembera mfumu Dariyo kalata ndi kulandira yankho lake.
6 Daytoy ti surat da Tatnai, Setar Bozenai, ken dagiti kakaduada nga opisiales para kenni Dario nga ari.
Iyi ndi kalata imene Tatenai bwanamkubwa wa dera la patsidya pa Yufurate, ndiponso Setari-Bozenai ndi anzake, akazembe amene anali mʼchigawo cha patsidya pa Yufurate, anatumiza kwa mfumu Dariyo
7 Nangipatulodda iti pakaammo, kastoy ti insuratda para kenni Ari Dario. “Kapia koma ti adda kenka.
Analemba kalatayo motere: Kwa mfumu Dariyo: Mukhale ndi mtendere wonse.
8 Maipakaammo iti ari a napan kami idiay Juda, iti balay ti naindaklan a Dios. Madama a maibangbangon daytoy babaen kadagiti dadakkel a batbato ken nakabilan iti kaykayo dagiti pader. Naan-anay ti pannakaaramid daytoy ket adu ti malmalpas dagiti imada.
Amfumu mudziwe kuti ife tinapita ku dziko la Yuda ku Nyumba ya Mulungu wamkulu. Nyumbayo ikumangidwa ndi miyala ikuluikulu ndipo akuyala matabwa pa makoma. Ntchitoyi ikugwiridwa mwachangu ndipo ikuyenda bwino kwambiri mwautsogoleri wawo.
9 Dinamagmi kadagiti panglakayenda, 'Siasino ti nangibilin kadakayo a bangonen daytoy a balay ken dagitoy a pader?'
Ndipo tinawafunsa atsogoleriwo kuti, “Anakulolezani kuti mumangenso Nyumbayi ndi kutsiriza makoma ake ndani?”
10 Dinamagmi pay dagiti nagnaganda tapno maamoam no ania ti nagan ti tunggal maysa a nangidaulo kadakuada.
Tinawafunsanso mayina a atsogoleri awo, kuti tikalemba mayina atsogoleriwo tidzakudziwitseni kuti muwadziwe.
11 Simmungbatda ket kinunada, 'Adipennakami ti Dios ti langit ken daga, ket bangbangonenmi manen daytoy a balay a siguden a naibangon, adun a tawen ti naglabas idi imbangon ken inleppas daytoy ti natan-ok nga ari ti Israel.
Yankho limene anatipatsa ndi ili: “Ife ndife atumiki a Mulungu wa kumwamba ndi wa dziko lapansi, ndipo tikumanganso Nyumba imene mfumu ina yamphamvu ya Israeli inamanga ndi kuyitsiriza zaka zambiri zapitazo.
12 Ngem idi pinagpungtot dagiti kapuonanmi ti Dios ti langit, inyawat ida ti Dios iti ima ni Nebucadnesar nga ari ti Babilonia a nangdadael iti daytoy a balay ken nangitalaw kadagiti tattao a kas balud nga impanna idiay Babilonia.
Koma chifukwa chakuti makolo athu anakwiyitsa Mulungu wakumwamba, Iye anawapereka kwa Nebukadinezara Mkalideya, mfumu ya Babuloni, amene anawononga Nyumbayi ndi kutenga anthu onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
13 Nupay kasta, iti umuna a tawen a panagturay ni Cyrus a kas ari ti Babilonia, nangipaulog ni Cyrus iti maysa a bilin tapno maibangon manen ti balay ti Dios.
“Komabe chaka choyamba cha Koresi, mfumu ya ku Babuloni, mfumu Koresiyo anapereka lamulo lakuti Nyumba ya Mulunguyi imangidwenso.
14 Insubli pay ni Ari Cyrus dagiti balitok ken pirak nga alikamen iti balay ti Dios nga innala ni Ari Nebucadnesar manipud idiay templo ti Jerusalem nga impanna iti templo idiay Babilonia. Insublina dagitoy kenni Sesbasar a pinagbalinna a gobernador.
Ndipo ziwiya zagolide ndi zasiliva za ku Nyumba ya Mulungu zimene Nebukadinezara anazitenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ndi kukaziyika mʼnyumba ya milungu ya ku Babuloni, anakazichotsa ku nyumba ya milungu ya ku Babuloniko ndi kuzipereka kwa Sesibazara, amene mfumu inamusankha kukhala bwanamkubwa.
15 Kinunana kenkuana, “Alaem dagitoy nga alikamen. Ikabilmo dagitoy iti templo idiay Jerusalem. Bay-am a maibangon manen ti balay ti Dios sadiay.
Tsono mfumuyo inamuwuza kuti, ‘Tenga ziwiyazi ukaziyike mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu. Ndipo Nyumba ya Mulunguyo ikamangidwenso pa maziko ake akale.’
16 Kalpasanna, immay daytoy a Sesbasar ket insaadna ti pundasion para iti balay ti Dios idiay Jerusalem; ket madama a maipatpatakder daytoy ngem saanpay a naileppas.'
“Choncho Sesibazarayo anabwera ndi kumanga maziko a Nyumba ya Mulunguyo mu Yerusalemu. Kuyambira tsiku limenelo mpaka lero yakhala ikumangidwa ndipo sinathebe.”
17 Ita, no nasayaat para iti ari, masukimat koma daytoy iti balay a nakaidulinan dagiti libro idiay Babilonia no adda sadiay ti bilin a nagtaud kenni Ari Cyrus a maibangon manen daytoy a balay ti Dios idiay Jerusalem. Kalpasanna, mabalin nga ipatulod ti ari ti pangngeddengna kadakami.
Nʼchifukwa chake ngati chingakukomereni amfumu, pachitike kafukufuku mʼnyumba yaufumu mosungira chuma ndi mabuku okhudza mbiri ya Babuloni kuti tione ngati mfumu Koresi inalamuladi za kumanganso Nyumba ya Mulungu mu Yerusalemu. Kenaka amfumu mutiwuze zomwe zikukondweretsani kuti mugamule pa nkhani imeneyi.

< Ezra 5 >