< Ezekiel 8 >

1 Ket napasamak iti maikalima nga aldaw ti maikanem a bulan iti maika-innem a tawen, bayat nga agtugtugawak iti uneg ti balayko, ken nakatugaw iti sangoanak dagiti panglakayen ti Juda, nga immay kaniak sadiay ti pannakabalin ni Yahweh nga Apo.
Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira.
2 Ket kimmitaak, ket adtoy, adda maysa a langa a kaing-ingas ti tao, a kasla adda apuy manipud iti patongna nga agpababa! Ken manipud iti patongna nga agpangato ket adda agranraniag a kasla agbegbeggang a landok!
Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira.
3 Ket adda kasla ima nga inggaw-atna ket ginammatanna ti buokko; impangatonak ti Espiritu iti nagbaetan ti langit ken daga, ket kadagiti sirmata manipud iti Dios, impannak idiay Jerusalem nga agturong iti pagserkan ti akin-uneg a ruangan iti amianan, a pagtaktakderan ti didiosen a mangparparnuay iti nakaro nga imun.
Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu.
4 Ket adda sadiay ti dayag ti Dios ti Israel, a kalanglanga ti kas iti nakitak idi idiay patad.
Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.
5 Ket kinunana kaniak, “Anak ti tao, tumalliawka iti amianan.” Timmalliawak ngarud iti amianan, ket iti agpaamianan a ruangan nga agturong iti altar, sadiay pagserkan ket adda sadiay didiosen ti imun.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.
6 Isu a kinunana kaniak, “Anak ti tao, makitam kadi ti ar-aramidenda? Dagitoy dagiti makarimon unay nga ar-aramiden ditoy ti balay ti Israel tapno adaywak ti bukodko a santuario! Ngem tumaliawka ket makitam dagiti nakarkaro pay a makarimon nga aramid!”
Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”
7 Kalpasanna, impannak iti pagserkan a ruangan ti paraangan, ket kimmitaak, ket adda maysa nga abut iti pader.
Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo.
8 Kinunana kaniak, “Anak ti tao, palawaem ti abut daytoy a pader.” Pinalawak ngarud ti abut iti pader, ket adda nakitak a ruangan!
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.
9 Ket kinunana kaniak, “Umunegka ket kitaem dagiti agkakadakes a makarimon nga ar-aramidenda ditoy.”
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.”
10 Simrekak ngarud ket nakitak, ket adtoy! Adda agduduma a kita dagiti agkarkarayam ken makarimon a narungsot nga ay-ayup! Naikitikit iti aglawlaw ti pader ti tunggal didiosen ti balay ti Israel.
Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza.
11 Pitopulo a panglakayen iti balay ti Israel ti adda sadiay, ket agtaktakder iti tengngada ni Jaazanias a putot a lalaki ni Safan. Agtaktakderda iti sangoanan dagiti imahen, ken nakaiggem iti insensario ti tunggal tao isu a ti ayamuom ti asuk ti insenso ket nagpangato.
Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.
12 Ket kinunana kaniak, “Anak ti tao, makitam kadi ti ar-aramiden dagiti panglakayen iti balay ti Israel iti nasipnget? Ar-aramiden daytoy ti tunggal tao kadagiti nailemmeng a siled a nakaidulinan dagiti didiosenna, ta ibagbagada, 'Saannatayo a makita ni Yahweh! Binaybay-anen ni Yahweh ti daga!”'
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’
13 Ket kinunana kaniak, “Tumaliawka manen ket kitaem dagiti dadduma nga ad-adda pay a makarimon nga ar-aramidenda.”
Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’”
14 Kalpasanna, impannak iti pagserkan ti ruangan iti balay ni Yahweh nga adda iti amianan a paset, ket adtoy! Agtugtugaw sadiay dagiti babbai nga agladladingit gapu kenni Tammuz.
Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi.
15 Isu a kinunana kaniak, “Makitam kadi daytoy, anak ti tao? Tumaliawka manen ket makitam dagiti nakarkaro pay a makarimon nga aramid ngem kadagitoy.”
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”
16 Ket impannak iti akin-uneg a paraangan ti balay ni Yahweh, ket adtoy! Iti pagserkan ti templo ni Yahweh, iti nagbaetan ti portiko ken ti altar, adda agarup dua pulo ket lima a lallaki a nakatallikud iti templo ni Yahweh ken simmangoda iti daya, ket agdaydayawda kenni Semes.
Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.
17 Kinunana kaniak, “Anak ti tao, makitam kadi daytoy? Bassit kadi laeng a banag para iti balay ti Juda ti panangaramidda kadagitoy a makarimon nga ar-aramidenda ditoy? Ta pinunnoda ti daga iti kinaranggas, ket timallikudda manen tapno pagungetendak, inkabilda dagiti sangsanga kadagiti agongda.
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo!
18 Isu a dusaekto met ida; saanakto a maasi kadakuada, ket saankonto ida nga ispalen. Uray ipangngegda kaniak ti napigsa a panagsangitda, saankonto ida a denggen!”
Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”

< Ezekiel 8 >