< Ezekiel 3 >

1 Kinunana kaniak, “Anak ti tao, kanem ti nakitam! Kanem daytoy nalukot a pagbasaan, ket mapanka agsao iti balay ti Israel.”
Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
2 Nagngangaak ngarud, ket impakanna kaniak ti nalukot a pagbasaan.
Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
3 Kinunana kaniak, “Anak ti tao, manganka ken bussogem ta tianmo iti daytoy nalukot a pagbasaan nga intedko kenka!” Kinnanko ngarud daytoy, ket kas kasam-it iti diro ti ramanna iti ngiwatko.
Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
4 Ket kinunana kaniak, “Anak ti tao, mapanka iti balay ti Israel ket ibagam kadakuada dagiti sasaok.
Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
5 Ta saanka a naibaon kadagiti tattao a ganggannaet ti pagsasaoda wenno narigat nga awaten ti pagsasaoda, ngem naibaonka iti balay ti Israel—
Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
6 saan nga iti nabileg a nasion a ganggannaet ti pagsasaoda wenno narigat a pagsasao a saanmo a maawatan! No ibaonka kadakuada, dumngegdanto kenka!
Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
7 Ngem ti balay ti Israel ket saandanto a kayat ti dumngeg kenka, ta saanda a kayat ti dumngeg kaniak. Ta natangken ti uloda ken natangken ti panagpuspusoda.
Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
8 Dumngegka! pinagbalinka a natangsit ken natured a kas kadakuada.
Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
9 Pinagbalinka a kasla diamante a natangtangken ngem iti bato! Saanka nga agbuteng kadakuada wenno madismaya kadagiti rupada, agsipud ta isuda ket nasukir a balay.”
Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
10 Kalpasanna, kinunana kaniak, “Anak ti tao, amin dagiti sasao nga imbagak kenka—ipapusom ken ipangagmo dagitoy!
Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
11 Ket mapanka kadagiti natiliw a balud, kadagiti tattaom, ket agsaoka kadakuada. Ibagam kadakuada, 'Kastoy ti kuna ni Yahweh nga Apo,' Dumngegda man wenno saan.”
Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
12 Kalpasanna, impangatonak ti Espiritu, ket adda timek iti likudak a kasla napigsa a ginggined, a kunana, “Madaydayaw ti dayag ni Yahweh iti nasantoan a lugarna!”
Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
13 Nangegko ngarud ti banesbes dagiti payak dagiti sibibiag a parsua iti panagsinnagid dagitoy, ken ti karadakad dagiti pilid nga adda iti tunggal sikiganda, ken ti ungor ti napigsa a ginggined!
Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
14 Impangatonak ti Espiritu ket impanawnak; ket napanak nga addaan sakit ti nakem iti pungtot ti espirituk, ta sibibileg ti ima ni Yahweh a mangidurduron kaniak!
Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
15 Nakagtengak ngarud idiay Tel Abib kadagiti natiliw a balud nga agnanaed iti igid ti Karayan Kebar, ket nagtalinaedak sadiay iti pito nga aldaw, a masmasdaawak unay.
Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
16 Ket napasamak daytoy kalpasan iti pito nga aldaw a dimteng ti sao ni Yahweh kaniak ket kinunana,
Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
17 “Anak ti tao, insaadka nga agwanawan iti balay ti Israel, isu a dumngegka iti ibagak kenka, ket ipakaammom kadakuada ti ballaagko!
“Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
18 No kunaek iti nadangkes a tao, 'Awan duadua a mataykanto' ket saanmo isuna a binallaagan wenno saanmo a binallaagan ti nadangkes a tao kadagiti dakes nga aramidna, tapno agbiag isuna—matay ti nadangkes a tao gapu iti basolna, ngem singirekto ti darana manipud iti imam.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
19 Ngem no ballaagam ti nadangkes, ket saanna a tallikudan ti kinadakesna wenno dagiti dakes nga aramidna, matayto ngarud isuna gapu iti basolna, ngem sika, inispalmo ti biagmo.
Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
20 Kasta met a no ti nalinteg a tao ket tallikudanna ti kinalintegna ken agaramid kadagiti saan a nainkalintegan, ikkak ngarud isuna iti pakaitublakanna, ket matayto isuna, agsipud ta saanmo isuna a binallaagan. Matayto isuna gapu iti basolna, ket saankonto a lagipen dagiti nalinteg nga inaramidna, ngem singirekto ti darana manipud iti imam.
“Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
21 Ngem no ballaagam ti nalinteg a tao nga agsardengen nga agbasbasol tapno saan isunan nga agbasol, awan duadua nga agbiagto isuna agsipud ta naballaagan; ket sika, inispalmo ti biagmo.”
Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
22 Adda ngarud kaniak ti pannakabalin ni Yahweh sadiay, ket kinunana kaniak, “Tumakderka! Mapanka iti patad, ket kasaritaka sadiay!”
Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
23 Timmakderak ket napanak iti patad, ket sadiay, nagtalinaed ti dayag ni Yahweh, kas iti dayag a nakitak iti igid ti Karayan Kebar; isu a nagpaklebak.
Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
24 Immay kaniak ti Espiritu ket pinatakdernak; ken kinasaritanak, ket kinunana kaniak, “Agawidka ket agkulongka iti uneg ti balaymo,
Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
25 ta ita, anak ti tao, reppetendakanto babaen kadagiti tali tapno saanka a makaruar a makipulapol kadakuada.
Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
26 Idekketkonto ta dilam iti ngangawmo, tapno agbalinka nga umel; ken saanmonto ida a matubngar, agsipud ta isuda ket nasukir a balay.
Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
27 Ngem inton kasaritakanto, ungapekto ta ngiwatmo tapno maibagamto kadakuada, 'Kastoy ti kuna ni Yahweh nga Apo.' Ti tao a makangngeg ket dumngeg; ti tao a saan a dumngeg ket saan a makangngeg, ta isuda ket nasukir a balay!”
Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”

< Ezekiel 3 >