< Ezekiel 25 >

1 Kalpasanna, immay kaniak ti sao ni Yahweh a kunana,
Yehova anandiyankhula kuti:
2 ”Anak ti tao, isangom ti rupam kadagiti tattao ti Ammon ket agipadtoka maibusor kadakuada.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula.
3 Ibagam kadagiti tattao ti Ammon, ‘Denggenyo ti sao ti Apo a ni Yahweh. Kastoy ti kuna ti Apo a ni Yahweh: Kinunayo, “Aha!” maibusor iti santuariok idi natulawan daytoy, ken maibusor iti daga ti Israel idi nagbalin a langalang daytoy, ken maibusor iti balay ti Juda idi naipanawda a kas balud.
Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo.
4 Ngarud, dumngegkayo! Iyawatkayon kadagiti tattao iti daya a kas sanikuada; mangiyaramiddanto iti kampoda a maibusor kadakayo ken iyaramidda dagiti toldada iti ayanyo. Kanendanto dagiti bunga ti mulayo, ken inumendanto dagiti gatasyo!
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu.
5 Ket pagbalinekto ti Rabba a maysa a pagpaaraban kadagiti kamelio ken pagpaaraban kadagiti arban ti talon dagiti tattao nga Ammon, isu a maammoanyonto a Siak ni Yahweh!
Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
6 Ta kastoy ti kuna ti Apo a ni Yahweh: Intipatyo dagiti imayo ken intabbugayo dagiti sakayo, ken nagragrag-okayo kadagiti amin a pananglalaisyo iti daga ti Israel.
Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli.
7 Isu a dumngegkayo! Isipatkonto kadakayo ti imak ken itedkayto a kas samsam kadagiti nasion. Isinakayto kadagiti tattao ken pukawenkayto kadagiti pagilian! Dadaelenkayto, ket maammoanyonto a Siak ni Yahweh!’
Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’”
8 Kastoy ti kuna ti Apo a ni Yahweh, ‘Gapu ta ibagbaga ti Moab ken Seir, “Kitaenyo! Ti balay ti Juda ket kasla kadagiti dadduma a nasion!”
“Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’
9 Isu a dumngegkayo! Lukatakto dagiti beddeng iti Moab, manipud kadagiti siudadna nga ayan ti beddeng—ti kinangayed ti Bet Jesimot, Baal Meon ken Kariatim—
Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu.
10 kadagiti tattao iti daya a siguden a bumusbusor kadagiti tattao ti Ammon. Iyawatkonto ida a kasla maysa a sanikua tapno dagiti tattao ti Ammon ket saanton a malagip pay kadagiti nasion.
Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina.
11 Isu a kedngakto dagiti taga-Moab, ket maammoandanto a Siak ni Yahweh!’
Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
12 Kastoy ti kuna ti Apo a ni Yahweh, ‘Binales dagiti taga-Edom ti balay ti Juda ket nagbiddutda iti panangaramidda iti kasta.
“Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi.
13 Isu a kastoy ti kuna ti Apo a ni Yahweh: Isipatkonto ti imak iti Edom ken dadaelek ti amin a tao ken ayup sadiay. Pagbalinekto ida a nadadael, nabaybay-an a lugar, manipud Teman agingga iti Dedan. Mapasagdanto babaen iti kampilan!
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani.
14 Iti kastoy a wagas, makaibalesakto iti Edom babaen iti ima dagiti tattaok nga Israelita, ket ipalak-amdanto iti Edom ti nalaus nga unget ken pungtotko! Isu a maammoandanto ti panagibalesko! —kastoy ti pakaammo ti Apo a ni Yahweh!’
Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’”
15 Kastoy ti kuna ti Apo a ni Yahweh, ‘Nagibales dagiti Filisteo gapu iti nalaos a gurada ken inulit-ulitda a pinadpadas a dadaelen ti Juda.
“Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira.
16 Isu a kastoy ti kuna ti Apo a ni Yahweh: Dumngegkayo! Iyunnatkonto ti imak kadagiti Filisteo, ken isinakto dagiti Kereteo ken dadaelek dagiti nabatbati nga adda kadagiti igid ti baybay!
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.
17 Ta balsekto ida iti nakaro babaen iti nakaro a panangdusak kadakuada, isu a maammoandanto a Siak ni Yahweh, inton balsek ida!”’
Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”

< Ezekiel 25 >