< Ezekiel 19 >

1 “Isu a sika! Ikantam daytoy a panagunnoy a maibusor kadagiti mangidadaulo iti Israel
“Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli.
2 ket kunaem, 'Siasino ti inam? Maysa a kabaian a leon a nagnaed kadagiti kalakian nga urbon ti maysa a leon; iti nagtetengngaan dagiti bumaro a leon, tinaraonanna dagiti urbonna.
Uzinena kuti, “‘Amayi ako anali ndani? Anali ngati mkango waukazi! Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna; unkalera ana ake pakati pa misona.
3 Ket pinadakkelna ti maysa kadagiti urbonna agingga a nagbalin a bumaro a leon a nakasursuro a mangrangkay kadagiti biktimana. Naglamut isuna kadagiti tattao.
Unalera mmodzi mwa ana ake, ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama, ndipo unayamba kudya anthu.
4 Ket nangngeg dagiti nasion ti maipanggep kenkuana. Natiliw isuna iti palab-ogda, ket impanda iti daga ti Egipto babaen kadagiti kallawit.
Anthu amitundu anamva za mkangowo, ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo. Iwo anawukoka ndi ngowe kupita nawo ku dziko la Igupto.
5 Ket nakitana nga uray no nagur-uray isuna iti panagsublina, napukawen ti namnamana, isu a nangala isuna iti maysa pay kadagiti urbonna ket pinadakkelna agingga a nagbalin a bumaro a leon.
“‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera, amayiwo anatenganso mwana wina namusandutsa mkango wamphamvu.
6 Nakipagdakiwas daytoy a bumaro a leon kadagiti padana a leon. Bumaro isuna a leon ket nasursurona ti mangrangkay kadagiti biktimana; naglamut isuna kadagiti tattao.
Unkayendayenda pakati pa mikango inzake, pakuti tsopano unali mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama ndipo unayamba kudya anthu.
7 Ket rinamesna dagiti balo dagiti napapatayna ken dinadaelna dagiti siudadda. Ket nabaybay-an ti daga ken amin a linaonna gapu iti uni ti panagngerngerna!
Unagwetsa malinga awo, ndikuwononga mizinda yawo. Onse a mʼdzikomo anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
8 Ngem immay dagiti nasion a maibusor kenkuana manipud kadagiti kabangibang a probinsia; inwayatda dagiti iketda kenkuana. Natiliw isuna iti palab-ogda.
Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira, inabwera kudzalimbana nawo. Anawutchera ukonde wawo, ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
9 Inkabilda isuna iti tangkal babaen iti kallawit ket impanda iti ari ti Babilonia. Impanda isuna kadagiti sarikedked dagiti bantay tapno saanen a mangngeg ti timekna kadagiti bantay ti Israel.
Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga. Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso ku mapiri a Israeli.
10 Maiyarig ti inam iti ubas a naimula iti daram iti abay ti danum. Nabunga isuna ken adu ti sangana gapu iti kinawadwad ti danum.
“‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa wodzalidwa mʼmbali mwa madzi. Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
11 Addaan isuna kadagiti natitibker a sanga nga agpaay a setro ti pangulo, ken maidaydayaw ti kinatayagna kadagiti sanga dagiti kaykayo nga adda iti aglawlawna.
Nthambi zake zinali zolimba, zoyenera kupangira ndodo yaufumu. Unatalika nusomphoka pakati pa zomera zina. Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake, ndi nthambi zake zambiri.
12 Ngem naparut ti ubas gapu iti pungtot ket naibelleng iti daga, ket pinagango ti angin manipud daya ti bungana. Nasip-ak dagiti natibker a sangana ket nalaylay; inuram ti apuy dagitoy.
Koma unazulidwa mwaukali ndipo unagwetsedwa pansi. Unawuma ndi mphepo ya kummawa, zipatso zake zinayoyoka; nthambi zake zolimba zinafota ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
13 Isu nga ita naimula isuna iti let-ang, iti daga a natikag ken namaga.
Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu, dziko lowuma ndi lopanda madzi.
14 Ta adda apuy a rimmuar manipud kadagiti dadakkel a sangana ket pinuoran daytoy dagiti bungana. Awanen ti natibker a sangana, awanen ti setro nga agturay.' Daytoy ket un-unnoy a maikantanto a kas panagunnoy.”
Moto unatulukanso mu mtengomo ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake. Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo yoyenera kupangira ndodo yaufumu. Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’”

< Ezekiel 19 >