< Ezekiel 18 >
1 Nagsao manen ni Yahweh kaniak a kunana,
Yehova anandiyankhula nati:
2 “Ania ti kayatyo a sawen, dakayo a mangus-usar iti daytoy a proberbio maipanggep iti daga ti Israel a kunkunayo, 'Nangan dagiti nagannak kadagiti naalsem nga ubas, ket dagiti ngipen dagiti annak ti naalino?'
“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
3 Iti naganko a sibibiag a Dios—kastoy ti pakaammo ni Yahweh nga Apo—saanyonton nga aramatenen daytoy a proberbio iti Israel.
“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
4 Adtoy! Kukuak ti tunggal biag! Ken kasta met ti biag dagiti nagannak, ken ti biag dagiti annak: kukuak ida! Ti tao nga agbasbasol isu ti matay!
Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
5 Ngem no ti maysa a tao ket nalinteg ken ipatpatungpalna ti hustisia ken kinalinteg—
“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
6 no saan isuna a nangan kadagidiay a bantay a pagdaydayawan kadagiti didiosen, ken saanna nga inkita dagiti matana kadagiti didiosen ti balay ti Israel—no saanna a tinulawan ti asawa ti kaarrubana, wenno inasitgan ti maysa a babai a madama iti binulan a panagreglana—
Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
7 no saanna nga indadanes ti siasinoman ngem ketdi insublina ti insalda ti nakautang—no saanna nga innala ti natakaw, ngem ketdi itedanna kadagiti taraonna dagiti mabisin ken kawesanna dagiti lamolamo;
Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
8 no saanna a paanakan dagiti ipautangna, wenno umawat iti nalabes a ganansya—no ipatungpalna ti hustisia ken ipasdekna ti kinapudno iti nagbabaetan dagiti tattao—
Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
9 no pagtulnoganna dagiti alagadek ken tungpalenna dagiti paglintegak tapno agtignay a sipupudno—daytoy a tao ket nalinteg; agbiagto isuna! —kastoy ti pakaammo ni Yahweh nga Apo.
Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
10 Ngem no addaan isuna iti naranggas nga anak a lalaki a mammapatay ken mangar-aramid iti aniaman kadagitoy a banbanag—
“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
11 uray no ti amana ket saanna nga ar-aramiden ti aniaman kadagitoy a banbanag—ngem no ti anakna a lalaki ket mangan kadagidiay a bantay a pagdaydayawan kadagiti didiosen ken tulawanna ti asawa ti kaarrubana—
Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
12 no idadanesna dagiti nakurapay ken agkasapulan, no agsamsam isuna ken agtakaw ken saanna nga isubli ti naisalda kenkuana, no ikitana dagiti matana kadagiti didiosen wenno agaramid kadagiti makarimon;
Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
13 no paanakanna dagiti ipautangna wenno umawat kadagiti sinasaur a ganansya, rumbeng kadi nga agbiag isuna? Saan isuna nga agbiag! Inaramidna amin dagitoy a makarimon a banbanag. Awan duadua a matay isuna; ti darana ket addanto kenkuana.
Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
14 Ngem adtoy! No maaddaan isuna iti anak a makakitkita kadagiti amin a basbasol nga inaramid ti amana, ken no isuna a mismo ket managbuteng iti Dios ken saanna nga ar-aramiden dagiti kakasta a banbanag—
“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
15 no saan isuna a mangan kadagidiay a bantay a pagdaydayawan kadagiti didiosen, wenno ikita dagiti matana kadagiti didiosen ti balay ti Israel—no saanna a tulawan ti asawa ti kaarrubana;
“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
16 no saanna nga idadanes ti siasinoman, no saan nga agsamsam iti salda, wenno saanna nga alaen dagiti natakaw, ngem ketdi ikkanna kadagiti taraonna dagiti mabisin ken kawesanna dagiti lamolamo—
Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
17 no saanna nga inukom dagiti nakurapay ken saanna a paanakan ti ipautangna wenno umawat iti sinasaur a ganansya; no ipatungpalna dagiti bilinko ken agtulnog kadagiti alagadek, saanto ngarud a matay isuna gapu iti basol ti amana. Awan duadua nga agbiagto isuna!
Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
18 Agsipud ta indadanes ti amana dagiti dadduma babaen iti panangsaur ken tinakawanna ti kabsatna, ken inaramidna ti saan a nasayaat kadagiti tattaona—ngarud, matayto isuna gapu iti basolna.
Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
19 Ngem kunayo, 'Apay a saan a baklayen ti anak ti basol ti amana?' Gapu ta ipatpatungpal ti anak ti hustisia ken kinalinteg ken tungpalenna dagiti amin nga alagadek; ar-aramidenna dagitoy. Awan duadua nga agbiagto isuna!
“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
20 Ti agbasbasol ket isu ti matay. Saan a baklayen ti anak ti basol ti amana, ken saan a baklayen ti ama ti basol ti anakna. Ti kinalinteg ti tao nga agtigtignay a sililinteg ket addanto kenkuana, ken ti kinadangkes ti dakes a tao ket addanto kenkuana.
Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
21 Ngem no tallikudan ti nadangkes dagiti amin a basol nga inaramidna, ket tungpalenna dagiti amin nga alagadek ken ipatungpalna ti hustisia ken kinalinteg, awan ngarud duadua nga agbiagto isuna ket saan a matay.
“‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
22 Amin dagiti basol nga inaaramidna ket saanton a malagip a maibusor kenkuana. Agbiagto isuna babaen iti kinalinteg nga ar-aramidenna.
Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
23 Agragsakak aya unay iti pannakatay ti nadangkes ket saan nga iti panangtallikudna iti dalanna tapno agbiag isuna? —kastoy ti pakaammo ni Yahweh nga Apo—
Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
24 Ngem no ti nalinteg a tao ket tallikudanna ti kinalintegna ket agaramid iti dakes ken agaramid kadagiti makarimon a kas kadagiti makarimon nga ar-aramiden dagiti nadangkes a tattao, apay agbiagto aya isuna? Amin dagiti nalinteg nga inaramidna ket saanton a malagip inton panawannak gapu iti panagsalungasingna. Matayto ngarud isuna gapu kadagiti basol nga inar-aramidna.
“‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
25 Ngem kunayo, 'Saan a sililinteg nga agtigtignay ti Apo!' Dumngegka, balay ti Israel! Saanak aya a sililinteg nga agtigtignay? Saan aya a dakayo ti saan a sililinteg nga agtigtignay?
“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
26 Inton tallikudan ti nalinteg a tao ti kinalintegna ket agbasol, ket matay gapu kadagitoy, matayto ngarud isuna gapu iti basol nga inaramidna.
Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
27 Ngem no tallikudan ti nadangkes a tao dagiti nadangkes nga aramidna ket ipatungpalna ti hustisia ken kinalinteg, mataginayonnanto ngarud ti biagna!
Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
28 Ta nakita ken tinallikudanna dagiti panagsalungasing nga inaramidna. Agbiagto isuna; Saanto isuna a matay!
Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
29 Ngem kuna ti balay ti Israel, 'Saan a sililinteg nga agtigtignay ti Apo!' Kasano a saanak nga agtigtignay a sililinteg, O balay ti Israel? Ken kasano nga agtigtignaykayo a sililinteg?
Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
30 Ngarud, ukomekto ti tunggal maysa kadakayo segun kadagiti aramidna, O balay ti Israel! —kastoy ti pakaammo ni Yahweh nga Apo. Agbabawikayo ket tallikudanyo dagiti amin a panagsalungasingyo tapno saan nga agbalin dagitoy a basol a pakaitibkolanyo.
“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
31 Iwaksiyo dagiti amin a panagsalungasing nga inaramidyo; pabaroenyo ti puso ken espirituyo. Ta apay a rumbeng a mataykayo, O balay ti Israel?
Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
32 Ta saanak nga agragsak iti pannakatay dagiti matay—kastoy ti pakaammo ni Yahweh nga Apo—isu nga agbabawikayo ket agbiagkayo!”
Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”