< Exodo 1 >

1 Dagitoy dagiti nagan dagiti annak ti Israel a kimmuyog kenni Jacob a napan idiay Egipto, kadua ti tunggal maysa ti sangkabalayanna:
Awa ndi mayina a ana a Israeli amene anapita ku Igupto pamodzi ndi Yakobo abambo awo, aliyense ndi banja lake:
2 Ruben, Simeon, Levi ken Juda,
Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda;
3 Isacar, Zabulon ken Benjamin,
Isakara, Zebuloni, Benjamini;
4 Dan, Naftali, Gad ken Aser.
Dani, Nafutali; Gadi ndi Aseri.
5 Pitopulo amin ti bilang dagiti kaputotan ni Jacob. Adda idin ni Jose idiay Egipto.
Anthu onse obadwa mwa Yakobo analipo 70. Yosefe nʼkuti ali kale ku Igupto.
6 Ket natay ni Jose, dagiti amin a kakabsatna, ken amin dayta a henerasion.
Tsono Yosefe ndi abale ake onse ndiponso mʼbado wawo wonse anamwalira.
7 Nabunga dagiti Israelita, immadu ken pimmigsada iti kasta unay; napunno ti daga kadakuada.
Koma Aisraeli anaberekana ndi kuchuluka kwambiri nakhala amphamvu kwambiri, kotero kuti anadzaza dzikolo.
8 Ket nagturay ti maysa a baro nga ari iti entero nga Egipto, a saan a mangbigbigbig iti pakasaritaan ni Jose.
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
9 Kinunana kadagiti tattaona, “Kitaenyo dagiti Israelita; ad-adu ken napigpigsada ngem datayo.
Iyo inati kwa anthu ake, “Taonani, Aisraeli achuluka ndipo ndi amphamvu kwambiri kuposa ife.
10 Umaykayo, tratoentayo ida a sisisirib. Ta no saan, ad-adda nga umaduda, ket no adda iti gubat, tumiponndanto kadagiti kabusortayo, a lumaban kadatayo, ket pumanawda iti daga.”
Tiyeni tiwachenjerere. Tikapanda kutero adzachuluka kuposa ife, ndipo ngati kutakhala nkhondo, adzadziphatika kwa adani athu nadzamenyana nafe, kenaka nʼkudzachoka mʼdziko muno.”
11 Isu a nangisaadda kadagiti kapatas a mangparigat kadakuada iti nadagsen a trabaho. Nangipatakder dagiti Israelita iti pagipenpenan a siudad para kenni Faraon: ti Pitom ken Rameses.
Kotero anayika akapitawo kuti aziwazunza ndi kuwagwiritsa ntchito yolemetsa mokakamiza. Iwo anamangira Farao mizinda ya Pitomu ndi Ramesesi kumene ankasungirako chakudya.
12 Ngem kas ad-adda a parparigaten dagiti Egipcio ida, ad-adda met nga umad-adu ken agwar-waras dagiti Israelita. Isu a nangrugi nga agbuteng dagiti Egipcio kadagiti Israelita.
Koma pamene ankawazunza kwambiri, Aisraeli ndiye ankachulukirachulukira mpaka kubalalikira mʼdziko lonse. Kotero Aigupto anayamba kuopa Aisraeliwo
13 Pinagtrabaho dagiti Egipcio dagiti Israelita iti nakaro.
ndipo anawagwiritsa ntchito mwankhanza kwambiri.
14 Pinagbalinda a nasaem ti panagbiagda babaen iti nadagsen a panagtrabaho iti alketran ken ladrilio, ken iti amin a kita ti trabaho iti talon. Amin a trabaho nga impaaramidda kadakuada ket narigat.
Aigupto anachititsa moyo wa Aisraeli kukhala owawa kwambiri powagwiritsa ntchito yakalavulagaga yowumba njerwa ndi kuponda dothi lomangira, pamodzi ndi ntchito zina zosiyanasiyana zamʼminda. Iwo anakakamiza Aisraeli mwankhanza kuti agwire ntchito yowawayi.
15 Ket nakisarita ti ari iti Egipto kadagiti partera a Hebreo; ti nagan ti maysa ket Zifra ken ti maysa ket Pua.
Mfumu ya Igupto inati kwa azamba a Chihebri omwe mayina awo anali Sifira ndi Puwa,
16 Kinunana, “No tulonganyo dagiti Hebreo a babbai iti paganakan, siputanyo no aganakda. No lalaki ti maladaga, masapul a patayenyo isuna; ngem no babai daytoy, bay-anyo nga agbiag.”
“Mukamathandiza amayi a Chihebri pa mwala wochirira, muzionetsetsa kuti akabadwa mwana wamwamuna muzipha, koma akakhala wamkazi muzimuleka akhale ndi moyo.”
17 Ngem adda panagbuteng dagiti partera iti Dios ket saanda nga inaramid ti imbilin ti ari iti Egipto kadakuada; ngem ketdi, binay-anda nga agbiag dagiti lallaki a maladaga.
Koma azambawo ankaopa Mulungu ndipo sanachite zimene mfumu ya Igupto inawawuza kuti achite. Iwo analeka ana aamuna kuti akhale ndi moyo.
18 Pinaayaban ti ari ti Egipto dagiti partera ket kinunana kadakuada, “Apay a binay-anyo nga agbiag dagiti lallaki a maladaga?”
Kenaka mfumu ya Igupto inayitanitsa azamba aja ndi kuwafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwachita zimenezi? Bwanji mwasiya ana aamuna kuti akhale ndi moyo?”
19 Simmungbat dagiti partera kenni Faraon, “Dagiti babbai a Hebreo ket saan a kasla kadagiti babbai nga Egipcio; napigsada ken nakaanakdan sakbay a sumangpet ti partera kadakuada.”
Azambawo anamuyankha Farao kuti, “Amayi a Chihebri sali ngati amayi a Chiigupto; Iwo ndi amphamvu ndipo amachira azamba asanafike.”
20 Sinalakniban ti Dios dagitoy a partera. Immadu ti dagiti tattao ken pimmigsada iti kasta unay.
Kotero Mulungu anawakomera mtima azambawo, ndipo Aisraeli anapitirirabe kuchulukana nakhala amphamvu kwambiri.
21 Gapu ta managbuteng iti Dios dagiti partera, inikkanna ida iti pamilia.
Pakuti azambawo ankaopa Mulungu, Iye anawapatsa mabanja awoawo.
22 Binilin ni Faraon dagiti amin a tattaona, “Masapul nga ibellengyo iti karayan ti tunggal lalaki a maiyanak, ngem mabalinyo a bay-an nga agbiag ti tunggal babai.”
Pamenepo Farao analamulira anthu ake onse kuti, “Mwana wamwamuna aliyense akabadwa, mukamuponye mu mtsinje wa Nailo, koma wamkazi mulekeni akhale ndi moyo.”

< Exodo 1 >