< Exodo 13 >

1 Nagsao ni Yahweh kenni Moises ket kinunana,
Yehova anati kwa Mose,
2 “Idatonmo kaniak dagiti amin nga inauna nga anak, tunggal inauna nga anak a lalaki kadagiti Israelita, tattao ken ayup. Kukuak dagiti inauna.”
“Ana onse aamuna oyamba kubadwa uwapatule, ndi anga. Aliyense woyamba kubadwa pakati pa Aisraeli ndi wanga, kaya ndi wa munthu kapena wa chiweto.”
3 Kinuna ni Moises kadagiti tattao, “Imulayo daytoy nga aldaw kadagiti panunotyo, ti aldaw a pimmanawkayo manipud Egipto, manipud iti balay ti pannakatagabu, ta impanawnakayo ni Yahweh manipud iti daytoy a lugar babaen iti napigsa nga imana. Awan ti tinapay nga adda lebadurana ti mabalin a kanen.
Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti.
4 Rumuarkayo manipud Egipto iti daytoy nga aldaw, iti bulan ti Abib.
Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto.
5 Inton ipannakayo ni Yahweh iti daga dagiti Cananeo, Heteo, Amorreo, Hebeo, ken dagiti Jebuseo, ti daga nga inkarina kadagiti kapuonanyo nga itedna kadakayo, daga a kasla agay-ayus ti gatas ken diro - ket masapul a ngilinenyo daytoy nga aramid a panagdayaw iti daytoy a bulan.
Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno.
6 Iti pito nga aldaw, masapul a mangankayo iti tinapay nga awan lebadurana; iti maika-pito nga aldaw, addanto iti padaya a pammadayaw kenni Yahweh.
Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova.
7 Ti tinapay nga awan lebadurana ti masapul a kanen bayat iti pito nga aldaw; masapul nga awan ti makita a tinapay nga adda lebadurana kadakayo. Masapul nga awan ti makita a lebadura kadakayo iti uray sadinoman iti uneg dagiti beddengyo.
Mudye buledi wopanda yisiti masiku asanu ndi awiri. Pasapezeke chinthu chilichonse chokhala ndi yisiti pakati panu, kapena paliponse mʼdziko lanu.
8 Iti dayta nga aldaw, ibagayonto kadagiti annakyo, ‘Daytoy ket gapu iti inaramid ni Yahweh kaniak idi pimmanawak manipud Egipto.’
Tsiku limenelo muzidzawuza ana anu kuti, ‘Ine ndimachita zimenezi chifukwa cha zimene Yehova anandichitira pamene ndimatuluka mʼdziko la Igupto.’
9 Agbalinto daytoy a palagip kadakayo dita imayo, ken palagip kadakayo dita mugingyo. Daytoy ket tapno ti linteg ni Yahweh ket adda koma dita ngiwatyo, ta impanawnakayo ni Yahweh manipud Egipto babaen iti napigsa nga imana.
Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.
10 Ngarud, masapul a tinawenyo nga aramiden daytoy a paglintegan iti naituding a tiempona.
Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.
11 Inton iyegnakayo ni Yahweh iti daga dagiti Cananeo, kas insapatana kadakayo ken kadagiti kapuonanyo, ken inton itedna ti daga kadakayo,
“Yehova akadzakulowetsani ndi kukupatsani dziko la Kanaani monga analonjezera kwa inu ndi makolo anu,
12 masapul nga ilasinyo para kenkuana ti tunggal inauna nga anak ken ti umuna nga anak dagiti ayupyo. Kukuanto ni Yahweh dagiti lallaki.
muzikapereka kwa Ambuye ana onse oyamba kubadwa. Ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa ndi za Ambuye.
13 Tunggal inauna nga asno ket masapul a masukatan iti karnero. Ngem no saanyo a kayat daytoy a sukatan, masapul ngarud a tukkolenyo ti tengngedna. Ngem iti tunggal inauna nga anak a lalaki kadagiti annakyo a lalaki - masapul a subbotenyo ida.
Koma mwana woyamba kubadwa wa bulu muzikamuwombola ndi mwana wankhosa, koma ngati simukamuwombola, muzikamuthyola khosi. Mwana wamwamuna woyamba kubadwa muzikamuwombola.
14 Inton saludsudennakayo ti anakyo a lalaki, 'Ania ti kayatna a sawen daytoy?' ket masapul nga ibagayo kenkuana, 'Babaen iti napigsa nga ima nga impanawnakami ni Yahweh iti Egipto, manipud iti balay ti pannakatagabu.
“Mʼtsogolomo mwana wanu akakafunsa kuti, ‘Zimenezi zikutanthauza chiyani?’ Mukamuwuze kuti, ‘Yehova anatitulutsa mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo ndi dzanja lamphamvu.
15 Idi sipapatangken a nagkedked ni Faraon a mangpalubos kadakami, pinatay ni Yahweh amin nga inauna nga annak idiay daga ti Egipto, dagiti inauna nga anak dagiti tattao ken dagiti ayup. Dayta ti gapuna nga idatonko kenni Yahweh amin nga inauna nga anak a lalaki dagiti ayup, ken no apay a subbotek dagiti inauna kadagiti annakko a lalaki.'
Farao atakanitsitsa kuti asatitulutse, Yehova anapha aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira ana a anthu ndi ziweto zomwe. Nʼchifukwa chake ine ndimapereka nsembe kwa Yehova, chachimuna chilichonse choyamba kubadwa ndipo mwana wamwamuna woyamba kubadwa ndimamuwombola.’
16 Agbalinto daytoy a palagip dita imayo, ken palagip dita mugingyo, ta impanawnakayo ni Yahweh iti Egipto babaen iti napigsa nga imana.''
Ndipo chidzakhala kwa inu ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi pamphumi panu kuonetsa kuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.”
17 Idi pinalubosan ni Faraon dagiti tattao, saan ida nga inturong ti Dios iti dalan a mapan iti daga dagiti Filisteo, uray no asideg dayta a daga. Ta kinuna ti Dios, “Amangan no agbaliw ti panunot dagiti tattao inton mapadasanda ti makigubat ket agsublida idiay Egipto.”
Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.”
18 Inlikaw ngarud nga inturong ti Dios dagiti tattao idiay let-ang a mapan idiay Baybay dagiti Runo. Simmang-at dagiti Israelita manipud Egipto a nakasagana a makigubat.
Choncho Mulungu anawadzeretsa anthuwo njira yozungulira ya mʼchipululu kulowera ku Nyanja Yofiira. Komabe Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto atakonzekera nkhondo.
19 Intugot ni Moises dagiti tulang ni Jose, ta siiinget a pinagsapata ni Jose dagiti Israelita ket kinunana, “Awan duadua nga ispalennakayo ti Dios, ket masapul nga itugotyo dagiti tulangko.”
Mose ananyamula mafupa a Yosefe chifukwa Yosefe anawalumbiritsa ana a Israeli. Iye anawawuza kuti, “Mulungu adzabwera ndithu kudzakuthandizani, ndipo mudzanyamule mafupa anga pochoka ku malo ano.”
20 Nagdaliasat dagiti Israelita manipud Succot ket nagkampoda idiay Etam idiay pungto ti let-ang.
Atachoka ku Sukoti anakagona ku Etamu mʼmphepete mwa chipululu.
21 Adda ni Yahweh iti sangoananda iti aldaw babaen iti kasla adigi nga ulep a mangiturong kadakuada iti dalan. Iti rabii, adda isuna babaen iti kasla adigi nga apuy a manglawag kadakuada. Iti daytoy a wagas, makapagdaliasatda iti aldaw ken iti rabii.
Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku.
22 Saan nga inikkat ni Yahweh kadagiti tattao ti kasla adigi nga ulep iti aldaw ken kasla adigi nga apuy iti rabii.
Usana, chipilala cha mtambo ndi usiku, chipilala cha moto zinali patsogolo kuwatsogolera anthu aja.

< Exodo 13 >