< Ester 6 >

1 Iti dayta a rabii, saan a makaturog ti ari. Impaiyegna kadagiti adipenna dagiti nakaisuratan dagiti pasamak iti panagturayna, ket naibasa dagitoy iti napigsa iti ari.
Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
2 Nasarakan a nakalanad ditoy nga imbaga ni Mardokeo ti maipanggep kada Bigtana ken Teres, dua kadagiti opisial ti ari a nangbantay iti pagserrekan, a nangpadas a mangdangran kenni Ari Ahasuero.
Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
3 Sinaludsod ti ari, “Ania ti naaramid a kas pammadayaw wenno panangbigbig kenni Mardokeo para iti panangaramid iti daytoy?” Ket kinuna dagiti adipen ti ari nga agtutubo a lallaki, “Awan ti naaramid para kenkuana.”
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
4 Kinuna ti ari, “Siasino ti adda iti paraangan?” Ita, nakastreken ni Haman iti akinruar a paraangan iti balay ti ari tapno makisarita kenkuana maipanggep iti panangibitin kenni Mardokeo iti pagbitayan nga insaganana para kenkuana.
Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
5 Kinuna dagiti adipen ti ari kenkuana, “Agtaktakder ni Haman iti paraangan.” Kinuna ti ari, “Pastrekenyo isuna.”
Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
6 Idi nakastreken ni Haman, kinuna ti ari kenkuana, “Ania ti rumbeng a maaramid para iti tao a pakaragsakan ti ari a padayawan?” Ita, kinuna ni Haman iti pusona, “Siasino ngay ti pakaragsakan ti ari a padayawan nga ad-adda ngem siak?”
Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
7 Kinuna ni Haman iti ari, “Para iti tao a pakaragsakan iti ari a padayawan,
Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
8 maiyeg koma ti kagay ti ari, kawes nga insuot ti ari, ken maysa a kabalio a naglugananen ti ari ken parabawan ti ulona iti guarnasion.
Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
9 Ket maipaima dagiti kagay ken ti kabalio iti maysa kadagiti katataknengan nga opisial ti ari. Palubosam a kawesanda ti tao a pakaragsakan ti ari a padayawan, ken maiparada isuna a nakalugan iti kabalio kadagiti dalan ti siudad. Paiwaragawagmo kadakuada iti sangoananna, 'Daytoy ti maaramid iti siasinoman a pakaragsakan ti ari a padayawan!'”
Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
10 Ket kinuna ti ari kenni Haman, “Darasem, alaem dagiti kagay ken ti kabalio, a kas kinunam, ket aramidem daytoy kenni Mardokeo a Judio nga agtugtugaw iti ruangan ti ari. Saanka nga agkurang iti uray maysa kadagiti aniaman nga imbagam.”
Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
11 Innala ngarud ni Haman ti kagay ken ti kabalio. Kinawesanna ni Mardokeo ken imparadana isuna a nakalugan iti kabalio kadagiti dalan ti siudad. Inwaragawagna iti sangoanan ni Mardokeo, “Daytoy ti maaramid iti tao a pakaragsakan ti ari a padayawan!”
Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
12 Nagsubli ni Mardokeo iti ruangan ti balay ti ari. Ngem nagdardaras ni Haman a napan iti balayna, agladladingit, a naabbongan ti ulona.
Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
13 Imbaga ni Haman kenni Zeres nga asawana ken kadagiti amin a gagayyemna ti amin a napasamak kenkuana. Ket kinuna dagiti lallaki a mabigbigbig gapu iti kinasiribda ken ni Zeres nga asawana kenkuana, “No ni Mardokeo a nakarugiam a matnag ket Judio, saanmo isuna nga abaken, ngem awan duadua a matnagkanto iti sangoananna.
Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
14 Kabayatan ti pannakitungtongda kenkuana, simmangpet dagiti opisial ti ari. Nagdardarasda a nangitugot kenni Haman iti padaya nga insagana ni Ester.
Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.

< Ester 6 >