< Ester 4 >

1 Idi naammoan amin ni Mardokeo ti naaramid, rinay-abna ti pagan-anayna ket nagkawes iti nakirsang a lupot ken nagikabil kadagiti dapo. Napan isuna iti tengnga ti siudad, ket naganug-og isuna iti napigsa ken nasaem.
Mordekai atamva zonse zimene zinachitika, anangʼamba zovala zake, navala chiguduli ndi kudzola phulusa, ndipo analowa mu mzinda, akulira mokweza ndi mowawidwa mtima.
2 Nagpatingga laeng isuna iti ruangan ti palasio ti ari, gapu ta awan ti mapalubusan nga sumrek a nakakawes iti nakirsang a lupot.
Ndipo anapita ndi kuyima pa chipata cha mfumu, chifukwa panalibe wina aliyense amaloledwa kulowa pa chipata cha mfumu atavala chiguduli.
3 Kadagiti amin a probinsia a nakadanunan ti bilin ken linteg ti ari, adda iti kasta unay a panagladingit kadagiti Judio, a nabuyogan iti panagayunar, panagsangit, ken panagladingit. Adu kadakuada iti nagidda iti nakirsang a lupot ken kadagiti dapo.
Chigawo chilichonse kumene mawu a mfumu ndi lamulo lake zinafika, kunali maliro akulu pakati pa Ayuda. Iwo ankasala zakudya, kulira mofuwula ndi kumadandaula. Ambiri anavala ziguduli ndi kudzola phulusa.
4 Idi napan dagiti babbalasitang ken dagiti adipen ni Ester nga imbaga kenkuana, nagledaang ti reyna. Nangipatulod isuna iti lupot a pagkawes ni Mardokeo (tapno ussobenna ti nakirsang a lupot), ngem saanna nga inawat dagitoy.
Anamwali otumikira mfumukazi Estere ndi adindo ake ofulidwa atabwera ndi kumuwuza za Mordekai, anavutika kwambiri. Estere anamutumizira zovala kuti avale ndi kuti avule chiguduli chake koma Mordekai sanalole zimenezo.
5 Ket pinaayaban ni Ester ni Hatak, maysa kadagiti opisial ti ari, a nadutokan nga agserbi kenkuana. Binilinna isuna a mapan kenni Mardokeo tapno ammoenna ti napasamak ken no ania ti kayatna a sawen iti ar-aramidenna.
Kenaka Estere anayitana Hataki, mmodzi wa adindo a mfumu ofulidwa amene anayikidwa kuti azimutumikira kuti apite kwa Mordekai kuti akamve chimene chimamuvuta komanso chifukwa chochitira zimenezi.
6 Napan ngarud ni Hatak iti ayan ni Mardokeo iti plasa iti siudad iti sangoanan iti ruangan ti palasio ti ari.
Choncho Hataki anapita kwa Mordekai ku bwalo la mzinda patsogolo pa chipata cha mfumu.
7 Impadamag ni Mardokeo kenkuana amin a napasamak kenkuana, ken no mano ti bilang ti pirak nga ingkari ni Haman a maikilo ken maikabil iti pagiduldulinan iti kinabaknang ti ari tapno maibilin a mapapatay dagiti Judio.
Mordekai anamuwuza zonse zimene zinamuchitikira kuphatikizapo mtengo weniweni wa ndalama zimene Hamani analonjeza kupereka mosungira chuma cha mfumu za anthu amene adzawononge a Yuda.
8 Nangted pay ni Mardokeo kenni Hatak iti kopya ti bilin a naited iti Susa para iti pannakadadael dagiti Judio. Inaramidna daytoy tapno ipakita ni Hatak daytoy kenni Ester, ken tapno maitedna kenni Ester ti pagrebbengan a mapan iti ari tapno agkiddaw iti paborna, ken makipagpakpakaasi kenkuana para kadagiti tattaona.
Mordekai anamupatsanso imodzi mwa makalata a ulamuliro wonena za chiwembuchi amene anawasindikiza ku Susa kukamuonetsa ndi kumufotokozera zonse Estere. Anamuwuzanso kuti akamudandaulire kuti akapite kwa mfumu kukapempha chifundo ndi kuyidandaulira chifukwa cha anthu a mtundu wake.
9 Napan ngarud ni Hatak ken imbagana kenni Ester ti imbaga ni Mardokeo.
Hataki anabwerera ndi kumufotokozera Estere zimene Mordekai ananena.
10 Kalpasanna nakisarita ni Ester kenni Hatak ket imbagana nga agsubli isuna kenni Mardokeo.
Ndipo Estere anamutuma Hataki kuti akanene kwa Mordekai kuti,
11 Kinuna ni Ester, “Amin dagiti adipen ken dagiti tattao kadagiti probinsia ti ari ket ammoda a siasinoman a lalaki wenno babai iti mapan iti akin uneg a paraangan ti ari a saan a napaayaban, adda iti maymaysa laeng a linteg: a masapul a mapapatay isuna-malaksid iti siasinoman a pangiturungan ti ari ti balitok a setro tapno agbiag dayta a tao. Saanak a napaayaban a mapan iti ayan ti ari kadagitoy tallo-pulo nga aldaw.”
“Atumiki onse amfumu ndi anthu a zigawo za mfumu ankadziwa kuti mwamuna kapena mkazi aliyense akalowa ku bwalo lake la mʼkati mosayitanidwa ndi mfumu pali lamulo limodzi: lamuloli ndi lakuti aphedwe. Zimasintha pokhapokha ngati mfumu iloza munthuyo ndi ndodo yagolide kuti akhale ndi moyo. Koma papita masiku makumi atatu ndisanayitanidwe ndi mfumu.”
12 Isu nga impadamag ni Hatak kenni Mardokeo dagiti imbaga ni Ester.
Tsono Mordekai anawuzidwa mawu a Estere.
13 Sinungbatan ni Mardokeo daytoy a mensahe: “Saanmo a panunoten nga iti palasio ti ari, ket makalibaskanto ngem kadagiti dadduma a Judio.
Kenaka Mordekai anawawuza kuti akamuyankhe Estere motere: “Usaganize kuti iwe wekha mwa Ayuda onse udzapulumuka chifukwa chakuti uli mʼnyumba ya mfumu.
14 No agtalinaedka a naulimek kadagitoy a tiempo, aggapu iti sabali a lugar ti tulong ken panangispal kadagiti Judio, ngem sika ken ti balay ni amam ket mapukawto. Siasino ti makaammo a nalabit a naitan-okka a reyna para iti kastoy a gundaway?”
Pakuti ngati ukhalatu chete nthawi ino, chithandizo ndi chipulumutso cha Ayuda zidzachokera kwina nʼkutheka kuti iwe ndi a pa banja la makolo ako mudzafa. Ndipo adziwa ndani mwina unalowa ufumu chifukwa cha nthawi ngati imeneyi?”
15 Kalapasanna, impatulod ni Ester daytoy a mensahe kenni Mardokeo,
Pamenepo Estere anatumiza yankho ili kwa Mordekai:
16 “Mapanka, ummongem dagiti amin a Judio nga agnanaed iti Susa, ket agayunarkayo para kaniak. Saankayo a mangan wenno uminum iti tallo nga aldaw, ti rabii wenno aldaw. Dagiti babbalasitangko ken siak ket agayunar iti isu met laeng a wagas. Ket mapanakto iti ayan ti ari, uray no maibusor daytoy iti linteg. Ket no mapukawak, mapukawak.”
“Pitani, mukasonkhanitse pamodzi Ayuda onse amene ali mu Susa ndipo mundisalire chakudya. Musadye kapena kumwa kwa masiku atatu, usiku ndi usana. Ine ndi anamwali anga onditumikira tidzasala chakudya monga inu. Izi zikachitika, ine ndidzapita kwa mfumu, ngakhale kutero ndikutsutsana ndi lamulo. Ndipo ngati nʼkufa ndife ndithu.”
17 Napan ni Mardokeo ket inaramidna amin nga imbaga ni Ester nga aramidenna.
Choncho Mordekai anapita ndi kuchita monga Estere anamupemphera.

< Ester 4 >