< Ester 2 >

1 Kalpasan dagitoy a banbanag, idi bimmaawen ti pungtot ni Ari Ahasuero, nalagipna ni Vasti ken ti inaramidna. Nalagipna met ti maipapan iti bilin nga inaramidna a maibusor kenkuana.
Pambuyo pake mtima wa Ahasiwero utatsika, Ahasiwero anakumbukira Vasiti ndi zimene anachita Vasitiyo. Anakumbukiranso lamulo lomukhudza limene anasindikiza.
2 Ket kinuna dagiti agtutubo a lallaki nga agserserbi kenkuana, “Iti biang iti ari, adda koma maaramid a panagbirok kadagiti napipintas a birhen a babbalasang.
Tsono anyamata a mfumu amene ankamutumikira anati, “Mfumu, akufunireni anamwali okongola.
3 Mangdutok koma ti ari kadagiti opisial kadagiti amin a probinsia iti pagarianna, a mangummong kadagiti amin a napipintas a birhen a babbalasang idiay harem iti palasio iti Susa. Maipaaywanda koma kenni Hegai, nga opisial ti ari, nga isu iti agay-aywan kadagiti babbai, ket bay-am isuna a mangted kadakuada kadagiti pagpapintas.
Mfumu isankhe oyangʼanira pa chigawo chilichonse cha ufumu wake kuti abwere nawo pamodzi anamwali onse okongola ku nyumba yosungira akazi ku Susa. Hegai, mdindo wofulidwa wa mfumu, amene amayangʼanira amayi, akhale wosamalira anamwaliwa ndipo aziwapatsa mafuta odzola.
4 Ti balasang a makaay-ayo iti ari ti agbalin a reyna a kasukat ni Vasti.” Daytoy a balakad ket nagustoan iti ari, ket inaramidna ngarud daytoy.
Ndipo namwali amene mfumu yakondwera naye akhale mfumukazi mʼmalo mwa Vasiti.” Mfumu inakondwera ndi uphunguwu, ndipo inachita momwemo.
5 Adda maysa a Judio iti siudad ti Susa nga agnagan iti Mardokeo a putot a lalaki ni Jair a puto a lalaki ni Simei a puto a lalaki ni Kis, a Benjamita.
Myuda wina wa fuko la Benjamini, dzina lake Mordekai, mwana wa Yairi, mwana wa Simei, mwana wa Kisi, anali mu mzinda wa Susa.
6 Naiyadayo isuna iti Jerusalem ta nairaman isuna kadagiti naitalaw a kas balud a kaduada Jehoiakim nga ari ti Juda, nga intalaw ni Nebucadnesar nga ari ti Babylonia.
Iyeyu anali mmodzi mwa anthu amene anatengedwa ukapolo ndi Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu pamodzi ndi Yekoniya mfumu ya Yuda.
7 Inay-aywananna ni Hadassa, dayta ket ni Ester, a puto a babai ti ulitegna, gapu ta awan ti ama wenno inana. Napintas ti pammagi ti balasang ken makaay-ayo ti langana. Inbilang isuna ni Mardokeo a kas bukodna a putot a babai.
Mordekai nʼkuti atalera Hadasa, amene ankatchedwanso Estere, mwana wamkazi wa amalume ake chifukwa analibe abambo kapena amayi. Mtsikanayu anali wokongola ndi wooneka bwino ndipo Mordekai ankamutenga ngati mwana wake weniweni pamene abambo ndi amayi ake anamwalira.
8 Idi a naipakaammo ti bilin ken linteg ti ari, adu a babbalasang ti naiyeg iti palasio ti Susa. Naipaaywanda kenni Hegai. Naipan met ni Ester iti palasio ti ari ken naipaaywan kenni Hegai, ti mangay-aywan kadagiti babbai.
Lamulo la mfumu atalilengeza ndi kubwera nawo pamodzi anamwali ambiri ku mzinda wa Susa kuti akasamalidwe ndi Hegai, Estere nayenso anatengedwa kupita naye ku nyumba ya mfumu kuti akasamalidwe ndi Hegai woyangʼanira nyumba yosungiramo akazi uja.
9 Naay-ayo ti balasang ni Hegai, ket nagun-odna ti paborna. Dagus nga impaayanna kadagiti pagpapintas ken iti bingayna a taraon. Nangidutok isuna kenkuana kadagiti pito nga adipen a babbai a naggapo iti palasio ti ari, ket inkabilna isuna ken dagiti adipen a babbai iti kasasayaatan a paset iti balay dagiti babbai.
Hegai anasangalatsidwa naye namwaliyo ndipo anamukomera mtima. Mosataya nthawi anamupatsa mafuta ake odzola ndi chakudya chapadera. Anamusankhiranso anamwali asanu ndi awiri a ku nyumba ya mfumu kuti azimutumikira, ndipo iye pamodzi ndi anamwali omutumikira aja anawapatsa malo abwino koposa mʼnyumba yosungira akazi.
10 Awan ti siasinoman a nangibagaan ni Ester no siasino dagiti tattao wenno kakabagianna, ta imbilin kenkuana ni Mardokeo a saanna nga ibagbaga.
Estere sanawulule mtundu wake ndi abale ake chifukwa Mordekai anamuletsa kutero.
11 Inaldaw nga agsubli subli ni Mardokeo iti paraangan ti balay dagiti babbai, tapno maamoanna no ania ti mapaspasamak kenni Ester, ken no ania iti mabalin a maaramid kenkuana.
Tsiku ndi tsiku Mordekai ankayendayenda pafupi ndi bwalo la nyumba yosungiramo akazi ija kuti adziwe za moyo wa Estere ndi kuti zinthu zikumuyendera bwanji.
12 Idi dimteng ti batang ti tunggal babai a mapan kenni Ari Ahasuero—kas panagtulnog kadagiti annuruten para kadagiti babbai, lippasen ti tunggal babai ti sangapulo ket dua a bulan a panagpapintas, innem a bulan nga agusarda iti lana ti mira, ken innem a bulan nga agusarda ti pabanglo ken pagpapintas—
Tsono nthawi inkafika kuti namwali aliyense akaonekere kwa mfumu Ahasiwero, pakutha pa miyezi khumi ndi iwiri yomwe inakhazikitsidwa kuti amayi azidzikongoletsa. Pa miyezi isanu ndi umodzi ankadzola mafuta a mure ndipo pa miyezi isanu ndi umodzi inayo ankadzola zonunkhira ndi zokongoletsa.
13 inton mapan ti balasang iti ayan ti ari, maipaay kenkuana aniaman a tarigagayanna manipud iti balay dagiti babbai, nga itugotna iti palasio.
Ndipo namwali ankapita kwa mfumu motere: Ankaloledwa kutenga chilichonse angafune mʼnyumba yosungiramo akazi kupita nacho ku nyumba ya mfumu.
14 Sumrek isuna iti rabii, ket iti kabigatanna agsubli isuna iti maikadua a balay dagiti babbai, ken iti panangaywan ni Saasgas, ti opisial iti ari, a mangay- aywan kadagiti assawa iti ari. Saan isuna nga agsubli iti ari malaksid no naliwliwa kenkuana ti ari ket paayabanna manen isuna.
Ankalowa madzulo kwa mfumu ndi kutuluka mmawa kupita ku nyumba ina yosungira akazi yomwe ankayangʼanira ndi Saasigazi, mdindo wofulidwa wa mfumu amene amayangʼanira akazi a mfumu. Namwali sankabwerera kwa mfumu pokhapokha amukomere mtima ndi kumuyitana potchula dzina lake.
15 Ita dimteng ti tiempo ni Ester (putot a babai ni Abihail, ti uliteg ni Mardokeo, a nangala kenkuana a kas bukodna a putot a babai) a mapan iti ayan ti ari, awan iti aniaman a kiniddawna no di, ti insingasing ni Hegai nga opisial ti ari a mangay-aywan kadagiti babbai. Ita nagun-od ni Ester ti pabor dagiti amin a nakakita kenkuana.
Tsono inafika nthawi kuti Estere, mwana wamkazi wa Abihaili amenenso analeredwa ndi Mordekai amalume ake, alowe kwa mfumu. Iye sanapemphe kanthu kalikonse, koma anatenga zokhazo zimene ananena Hegai mdindo wofulidwa wa mfumu woyangʼanira nyumba yosungiramo akazi. Ndipo aliyense amene anamuona Estere, anasangalatsidwa naye.
16 Naiyeg ni Ester iti pagtaengan ni Ari Ahasuero iti maikasangapulo a bulan, a bulan ti Tebeth, iti maikapito a tawen iti panagturayna.
Anapita naye kwa mfumu Ahasiwero ku nyumba ya ufumu pa mwezi wa khumi, mwezi wa Tebete, chaka cha chisanu ndi chiwiri cha ufumu wake.
17 Inayat ti ari ni Ester a nalablabes ngem kadagiti amin a babbai, ket nagun-od ni Ester ti pabor ken panagayat iti sangoanan ti ari, a nalablabes ngem kadagiti amin a birhen, isu nga inkabil ti ari ti korona ti reyna iti ulo ni Ester ket insaad ti ari ni Ester a reyna a kasukat ni Vasti.
Ndipo mfumu inamukonda Estere koposa wina aliyense wa akazi aja, kotero inamukonda ndi kumukomera mtima koposa wina aliyense wa anamwali aja. Choncho anamumveka chipewa chaufumu pa mutu pake nakhala mfumukazi mʼmalo mwa Vasiti.
18 Nangangay ti ari iti dakkel a padaya para kadagiti amin nga opisial ken kadagiti adipenna, “Padaya ni Ester,” ket impaayna ti tulong kadagiti probinsia manipud kadagiti naibayad a buis. Nangited pay isuna kadagiti sagut a nabuyugan iti kinaimbag.
Ndipo mfumu inakonza phwando lalikulu, phwando la Estere, kukonzera anthu olemekezeka ndi nduna zake zonse. Analamuliranso kuti anthu mʼzigawo zonse asapereke msonkho ndipo anapereka mphatso monga mwakukoma mtima kwa mfumu.
19 Ita, idi sangsangkamaysa a naummong manen dagiti birhen iti maikadua a tiempo, nakatugaw ni Mardokeo iti ruangan ti palasio ti ari.
Anamwali atasonkhanitsidwa pamodzi, Mordekai anakhala pansi pa chipata cha mfumu.
20 Saan pay nga imbaga ni Ester iti siasinoman iti maipanggep kadagiti kakabagianna wenno tattaona, a kas imbilin ni Mardokeo kenkuana. Intuloyna a tinungpal ti balakad ni Mardokeo, a kas inaramidna idi inaywananna isuna.
Koma Estere anali asanawululebe za mtundu wake ndi anthu a pa banja lake monga momwe analamulira Mordekai, chifukwa anapitirira kutsata malangizo a Mordekai monga ankachitira pamene ankamulera.
21 Kadagidiay nga al-aldaw, kabayatan nga agtugtugaw ni Mardokeo iti ruangan ti palasio ti ari, dua kadagiti opisyal ti ari ti nakaunget, da Bigtana ken Teres, a mangbanbantay iti ruangan iti ari, ket pinanggepda a dangran ni Ari Ahasuero.
Pa nthawi imene Mordekai ankalondera pa chipata cha mfumu, Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa amfumu, olondera pa khomo la nyumba yake, anayipidwa mtima ndipo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
22 Idi naiparangarang dayta a banag kenni Mardokeo, imbagana kenni Reyna Ester, ket nakisarita ni Ester iti ari babaen iti nagan ni Mardokeo.
Koma Mordekai atazindikira za chiwembuchi anawuza mfumukazi Estere ndipo iye anakawuza mfumu mʼmalo mwa Mordekai.
23 Nasukimat ken napaneknekan ti damag, ket nabitay nga agpada dagiti dua a lallaki. Naisurat ti pasamak Iti Libro Iti Pakasaritaan iti imatang iti ari.
Ndipo pamene anafufuza za chiwembuchi kuti zinali zoona, adindo awiriwa anaphedwa monyongedwa. Zinthu izi zinalembedwa mʼbuku la Mbiri ndi kusungidwa ndi Mfumu.

< Ester 2 >