< Daniel 2 >

1 Iti maikadua a tawen ti panagturay ni Nebucadnesar, nagtagtagainep isuna. Nariribukan isuna, ket saanen a makaturog.
Chaka chachiwiri cha ulamuliro wake, Nebukadinezara analota maloto; anavutika mu mtima mwake ndipo analephera kugona.
2 Ket pinaayaban ti ari dagiti salamangkero ken dagiti mangibagbaga a kabaelanda ti makisarita kadagiti natay. Pinaayabanna pay dagiti managanito ken dagiti nasirib a lallaki. Kayatna nga ibagada kenkuana ti maipapan kadagiti tagtagainepna. Isu a simrekda ket nagtakderda iti sangoanan ti ari.
Tsono mfumu inayitana amatsenga, owombeza, amawula ndi oyangʼana nyenyezi kuti amufotokozere zomwe analota. Pamene iwo analowa ndi kuyima pamaso pa mfumu,
3 Kinuna ti ari kadakuada, “Nagtagtagainepak, ket magagaranak a mangammo iti kayat a sawen ti tagtagainep.”
mfumuyo inawawuza kuti, “Ndalota loto lomwe likundisautsa ndipo ndikufuna kudziwa tanthauzo lake.”
4 Ket nakisarita dagiti nasirib a lallaki iti ari babaen iti pagsasao nga Arameo, “O Ari, agbiagka iti agnanayon! Ibagam ti tagtagainep kadakami nga adipenmo, ket ibagami ti kaipapananna.”
Pamenepa alawuli anati kwa mfumu mʼChiaramu, “Mukhale ndi moyo wautali mfumu! Tiwuzeni ife atumiki anu zimene mwalota, ndipo tidzakuwuzani tanthauzo lake.”
5 Insungbat ti ari kadagiti nasirib a lallaki, “Naikeddengen daytoy a banag. No saanyo a maibaga ti tagtagainep kaniak ken ti kaipapanan daytoy, marangrangkayto dagiti bagiyo ken agbalin a gabsuon dagiti rugit dagiti balayyo.
Mfumu inayankha alawuliwo kuti, “Zimene ndatsimikiza kuchita ndi izi: Ngati inu simundifotokozera zimene ndalota ndi tanthauzo lake, mudzadulidwa nthulinthuli ndipo nyumba zanu ndidzazisandutsa bwinja.
6 Ngem no maibagayo kaniak ti tagtagainep ken ti kaipapanan daytoy, makaawatkayo kadagiti sagut manipud kaniak, maysa a gunggona ken dakkel a pammadayaw. Isu nga ibagayo kaniak ti tagtagainep ken ti kaipapanan daytoy.”
Koma ngati mundiwuza zimene ndalota ndi tanthauzo lake, ndidzakupatsani mphatso ndi mphotho ndi ulemu waukulu. Choncho mundiwuze zimene ndalota ndi tanthauzo lake.”
7 Insungbatda manen ket kinunada, “Ibaga koma ti ari kadakami nga adipenna, ti tagtagainep ket ibagami kenka ti kaipapanan daytoy.”
Iwo anayankhanso kachiwiri kuti, “Mfumu iwuze atumiki ake chimene yalota, ndipo ife tidzatanthauzira.”
8 Simmungbat ti ari, “Ammok a kayatyo ti at-atiddog pay a tiempo gapu ta makitayo ti natibker a pangngeddengko maipapan iti daytoy.
Ndipo mfumu inayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti mukungozengereza kufuna kutaya nthawi chabe chifukwa mukuzindikira kuti izi ndi zimene ndatsimikiza kuchita.
9 Ngem no saanyo a maibaga kaniak ti tagtagainep, maysa laeng ti sentensia para kadakayo. Inkeddengyo ti mangisagana iti palso ken manangallilaw a sasao a nagnunumoanyo nga ibaga kaniak agingga nga agbaliw ti panunotko. Isu nga Ibagayo kaniak ti tagtagainep, ket maammoak a kabaelanyo nga ibaga ti kaipapanan daytoy para kaniak.”
Ngati simundiwuza zimene ndalota, chilango chake ndi chimodzi. Inu mwagwirizana kuti mundiwuze ine bodza ndi chinyengo ndi kuyembekeza kuti ine ndisintha. Tsono mundiwuze zimene ndalota, ndipo ine ndidzadziwa kuti mukhoza kunditanthauzira.”
10 Insungbat dagiti nasirib a lallaki iti ari, “Awan ti uray maysa a tao iti daga a makabael a mangibaga iti kalikagum ti ari. Awan ti nabileg ken mannakabalin nga ari ti agkalikagum iti kasta manipud iti siasinoman a salamangkero, wenno manipud iti siasinoman a mangibagbaga a kabaelanda ti makisarita kadagiti natay wenno manipud iti maysa a nasirib a tao.
Alawuli anayankha mfumu kuti, “Palibe munthu pa dziko lapansi amene akhoza kuchita chimene mfumu ikufunsa! Palibe mfumu, kaya yayikulu kapena yamphamvu bwanji imene inafunsapo amatsenga, owombeza kapena alawuli aliwonse zimenezi.
11 Narigat ti kalkalikaguman ti ari, ket awan ti siasinoman a makaibaga iti daytoy iti ari malaksid kadagiti didios, ket saanda a makipagnanaed kadagiti tattao.”
Zimene mfumu yafunsa ndi zapatali. Palibe wina amene angathe kuwulula izi kwa mfumu kupatula milungu, ndipo sikhala pakati pa anthu.”
12 Daytoy ti nangpaunget ken nangpapungtot unay iti ari, ket imbilinna a mapapatay dagiti amin nga adda iti Babilonia a nalatak gapu iti kinasiribda.
Zimenezi zinapsetsa mtima mfumu ndipo inakwiya kwambiri kotero inalamula kuti anzeru onse a ku Babuloni aphedwe.
13 Isu a naiwaragawag ti bilin. Mapapatay dagiti amin a nalatak gapu iti kinasiribda; binirokda ni Daniel ken dagiti gagayyemna tapno mapapatayda met.
Choncho lamulo linaperekedwa kuti anthu anzeru aphedwe, ndipo anatuma anthu kukafunafuna Danieli ndi anzake kuti iwonso aphedwe.
14 Ket simmungbat ni Daniel nga addaan iti kinaannad ken kinatimbeng kenni Arioc a pangulo dagiti guardia ti ari, nga immay a mangpapatay kadagiti amin a nalatak idiay Babilonia gapu iti kinasiribda.
Danieli anayankhula mwanzeru ndi mwaulemu kwa Ariyoki, mkulu wa asilikali olondera mfumu amene anatumidwa kukapha anthu anzeru a ku Babuloni.
15 Sinaludsod ni Daniel iti panguloen dagiti guardia ti ari, “Apay a naganat unay ti bilin ti ari?” Imbaga ngarud ni Arioc kenni Daniel ti napasamak.
Danieli anafunsa Ariyoki kapitawo wa mfumu kuti, “Chifukwa chiyani mfumu yapereka lamulo lankhanza lotere?” Kenaka Ariyoki anafotokoza nkhaniyi kwa Danieli.
16 Kalpasanna, simrek ni Daniel ket kiniddawna a mangikeddeng ti ari iti tiempo tapno maibagana ti kaipapanan ti tagtagainep iti ari.
Danieli anapita mofulumira kwa mfumu ndipo anamupempha kuti amupatse nthawi kuti amuwuze zimene walota ndi tanthauzo lake.
17 Kalpasanna, nagawid ni Daniel ket inlawlawagna kada Hananias, Misael, ken Azarias ti napasamak.
Kenaka Danieli anabwerera ku nyumba kwake ndi kukafotokozera anzake aja zimenezi: Hananiya, Misaeli ndi Azariya.
18 Ginuyugoyna ida nga agpakaasida iti Dios ti langit maipapan iti daytoy a misterio tapno saanda a mapapatay a kaduada dagiti dadduma a lallaki ti Babilonia a nalatak gapu iti kinasiribda.
Danieli anadandaulira anzake kuti apemphe kwa Mulungu wakumwamba kuti awachitire chifundo ndi kumuwululira chinsinsi, kuti iye ndi anzakewo asanyongedwe pamodzi ndi anzeru ena onse a ku Babuloni.
19 Iti dayta a rabii, naiparang kenni Daniel ti palimed babaen iti maysa a sirmata. Ket dinaydayaw ni Daniel ti Dios ti langit
Usiku Yehova anamuwululira Danieli chinsinsi chija mʼmasomphenya. Pamenepo Danieli anatamanda Mulungu wakumwamba,
20 ket kinunana, “Madaydayaw ti nagan ti Dios iti agnanayon nga awan patinggana; ta kukuana ti kinasirib ken pannakabalin.
ndipo anati: “Litamandike dzina la Mulungu ku nthawi za nthawi; nzeru ndi mphamvu zonse ndi zake.
21 Balbaliwanna dagiti tiempo ken dagiti panawen; Ik-ikkatenna dagiti ari ket isasaadna dagiti ari kadagiti tronoda. Ik-ikkanna iti kinasirib dagiti nasirib ken ik-ikkanna iti pannakaammo dagiti addaan pannakaawat.
Amasintha nthawi ndi nyengo; amakweza mafumu ndipo amawatsitsanso. Amapatsa nzeru kwa anzeru ndi chidziwitso kwa ozindikira zinthu.
22 Iparparangna dagiti nauneg ken nailemmeng a banbanag gapu ta ammona no ania ti adda iti kasipngetan, ken agnanaed kenkuana ti lawag.
Amavumbulutsa zinthu zozama ndi zobisika; amadziwa zimene zili mu mdima, ndipo kuwunika kumakhala ndi Iye.
23 O Dios dagiti kapuonak, agyaman ken agdaydayawak kenka gapu iti kinasirib ken pannakabalin nga intedmo kaniak. Ita, impakaammom kaniak ti inkararagmi kenka; impakaammom kadakami ti banag a pakaseknan ti ari.”
Ndikuyamika ndi kutamanda Inu Mulungu wa makolo anga: mwandipatsa nzeru ndi mphamvu, mwandiwululira zomwe tinakupemphani, mwatiwululira maloto a mfumu.”
24 Gapu amin kadagitoy, napan ni Daniel kenni Ariok, ti dinutokan ti ari a mangpapatay kadagiti amin a nasirib iti Babilonia. Napan ket kinunana kenkuana, “Saanmo a papatayen dagiti nasirib a lallaki iti Babilonia. Kadduaannak a mapan iti sangoanan ti ari ket ibagak ti kaipapanan ti tagtagainep iti ari.”
Motero Danieli anapita kwa Ariyoki, amene mfumu inamusankha kuti akaphe anthu anzeru a ku Babuloni, ndipo anati kwa iye, “Musaphe anthu anzeru a ku Babuloni. Ndiperekezeni kwa mfumu, ndipo ndidzayimasulira maloto ake.”
25 Ket dagus nga impan ni Arioc ni Daniel iti sangoanan ti ari ket kinunana, “Nakasapulak iti maysa a lalaki manipud kadagiti napagtalaw a kas balud ti Juda a makaibaga iti kaipapanan ti tagtagainep ti ari.”
Ariyoki anapita naye Danieli kwa mfumu nthawi yomweyo ndipo anati, “Ndapeza munthu pakati pa akapolo ochokera ku Yuda amene akhoza kuwuza mfumu zimene maloto ake akutanthauza.”
26 Kinuna ti ari kenni Daniel (a naawagan iti Beltesazar), “Kabaelam kadi nga ibaga kaniak ti natagtagainepko ken ti kaipapanan daytoy?”
Mfumu inafunsa Danieli (wotchedwanso Belitesezara) kuti, “Kodi ukhoza kundiwuza zomwe ine ndinaona mʼmaloto anga ndi tanthauzo lake?”
27 Simmungbat ni Daniel iti ari ket kinunana, “Ti misterio a kinalikaguman ti ari ket a saan a maibaga dagiti addaan iti kinasirib, wenno dagiti mangibagbaga a kabaelanda ti makisarita kadagiti natay, wenno dagiti salamangkero, ken saan a maibaga dagiti astrologo.
Danieli anayankha kuti, “Palibe munthu wanzeru, wowombeza, wamatsenga kapena wamawula amene akhoza kufotokozera mfumu chinsinsi chimene mwafuna kudziwa,
28 Nupay kasta, adda Dios nga agnanaed kadagiti langit, a mangiparparangarang kadagiti palimed, ket impakaammona kenka, O Ari Nebucadnezar, dagiti mapasamakto kadagiti sumaruno nga al-aldaw. Ti tagtagainepmo ken dagiti sirmata iti panunotmo bayat nga agid-iddaka iti pagiddaam ket dagitoy:
koma kuli Mulungu kumwamba amene amawulula zinsinsi. Iye waonetsera mfumu Nebukadinezara zimene zidzachitika mʼmasiku akutsogolo. Maloto ndi masomphenya anu amene munawaona mukugona pa bedi lanu ndi awa:
29 No maipapan kenka, O ari, dagiti panpanunotem iti pagiddaam ket maipapan kadagiti banbanag a mapasamakto iti masakbayan, ket impakaammo kenka ti mangiparparang kadagiti palimed ti mapasamakto.
“Mukugona pa bedi, inu Mfumu, maganizo anakufikirani a zinthu zakutsogolo, ndipo Yehova wowulula zinsinsi anakuonetserani zimene zidzachitika.
30 No maipapan kaniak, saan a naiparang kaniak daytoy a palimed gapu ta nasirsiribak ngem iti siasinoman a sibibiag a tao. Naiparang kaniak daytoy a palimed tapno sika, O ari, maawatam koma ti kaipapananna, ken tapno maammoam koma dagiti kapanunotan iti kaunggam.
Koma chinsinsi ichi chavumbulutsidwa kwa ine, si chifukwa chakuti ndili ndi nzeru zochuluka kuposa anthu ena onse, koma kuti mfumu mudziwe tanthauzo la maloto anu ndi kuti muzindikire maganizo amene anali mu mtima mwanu.
31 O ari, timmangadka ket nakakitaka iti maysa a dakkel nga estatua. Nakatakder iti sangoanam daytoy nga estatua a nabileg ken naraniag unay. Nakabutbuteng ti kinaraniagna.
“Inu mfumu, munaona chinthu chowumba chachikulu chimene chinayima pamaso panu. Chowumbachi chinali chonyezimira mʼmaonekedwe.
32 Ti ulo ti estatua ket naaramid iti puro a balitok. Ti barukong ken dagiti takkiagna ket naaramid iti pirak. Ti tian ken dagiti luppona ket naaramid iti bronse, ken dagiti gurongna ket naaramid iti landok.
Mutu wa chowumbacho unali wagolide wabwino kwambiri. Chifuwa ndi manja ake zinali zasiliva. Mimba ndi ntchafu zake zinali zamkuwa.
33 Dagiti sakana ket naaramid iti naglaok a landok ken damili.
Miyendo yake inali yachitsulo, mapazi ake anali achitsulo chosakaniza ndi dongo.
34 Timmangadka ket maysa a bato ti nargaay, uray no kasta, saan a babaen kadagiti ima ti tao, ket naitupak daytoy kadagiti saka ti estatua a naaramid iti naglaok a landok ken damili, ket nawarawara dagitoy.
Inu mukuona, mwala unagamuka, koma osati ndi manja a munthu. Unagwera fanolo pa mapazi ake achitsulo chosakaniza ndi dongo aja ndi kuwaphwanya.
35 Kalpasanna, naggigiddan a naburak ti landok, damili, bronse, pirak ken balitok ket nagbalin a kasla taep ti pagirikan iti kalgaw. Naiyangin dagitoy ket awanen ti nabati a pakakitaan kadagitoy. Ngem ti bato a naitupak iti estatua ket nagbalin a dakkel a bantay ket pinunnona ti entero a daga.
Tsono chitsulo, dongo, mkuwa, siliva ndi golide zonse zinaphwanyika pamodzi ndikukhala tizidutswa towuluka ndi mphepo ngati mungu wa mowombera tirigu nthawi ya chilimwe. Zonse zinawuluka ndi mphepo osasiyako chilichonse. Koma mwala umene unagwera pa chowumba chija unasanduka phiri lalikulu ndi kudzaza dziko lonse lapansi.
36 Daytoy ti tagtagainepmo. Ita, ibagami iti ari ti kaipapanan ti tagtagainepna.
“Maloto aja ndi amenewa; tidzafotokoza tanthauzo lake kwa mfumu.
37 Sika, O ari, ket ari dagiti ar-ari a nangitedan ti Dios ti langit iti pagarian, ti pannakabalin, bileg ken dayaw.
Inu mfumu, ndinu mfumu ya mafumu. Mulungu wakumwamba wakupatsani ufumu, ulamuliro ndi mphamvu ndi ulemerero;
38 Inyawatna iti imam ti disso a pagnanaedan dagiti tattao. Inyawatna iti imam dagiti ayup iti kataltalonan ken dagiti billit iti tangatang, ken pinaiturayanna amin ida kenka. Sika ti balitok nga ulo ti estatua.
Iye anayika mʼmanja mwanu anthu ndi nyama zakuthengo ndi mbalame zamlengalenga. Kulikonse kumene zikhala, iye anakuyikani wolamulira wa zonse. Inu ndinu mutu wagolidewo.
39 Kalpasan ti panagturaymo, tumaudto ti maysa pay a pagarian a saan a nabilbileg ngem sika, ngem agturayto iti entero a daga ti maikatlo a pagarian ti bronse.
“Pambuyo pa inu, ufumu wina udzadzuka, wochepa mphamvu poyerekeza ndi wanuwu. Padzabweranso ufumu wachitatu, wamkuwa, udzalamulira dziko lonse lapansi.
40 Addanto maikapat a pagarian a kas katibker ti landok, gapu ta buraken ti landok dagiti dadduma a banbanag ken warawaraen daytoy dagiti amin a banag. Warawaraen ken rumekento daytoy dagiti amin a banbanag.
Pomaliza, padzakhala ufumu wachinayi, wolimba ngati chitsulo popeza chitsulo chimaphwanya ndi kutikita chilichonse. Ndipo monga chitsulo chimaphwanya zinthu ndikuteketeratu, choncho udzawononga ndi kuphwanya maufumu ena onse.
41 Kas iti nakitam, naglaok a damili ken landok dagiti saka ken ramay daytoy, isu a magudduanto daytoy a pagarian; addanto iti daytoy ti dadduma a tibker ti landok kas iti nakitam a nailaok ti landok iti damili.
Ndipo monga munaonera kuti mapazi ndi zala zake zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho uwu udzakhala ufumu wogawikana; komabe udzakhala ndi mphamvu zina zachitsulo zotikita.
42 Gapu ta naaramid dagiti saka ken ramay iti naglaok a landok ken damili, kastanto met ti pagarian, napigsanto ti dadduma a paset ket narasinto ti dadduma a paset.
Monga zala zinali za chitsulo chosakaniza ndi dongo, choncho ufumu uwu udzakhala pangʼono wolimba ndi pangʼono wofowoka.
43 Kas iti nakitam, nailaok ti landok iti damili, isu nga aglalaokto dagiti tattao; saandanto a nadekket iti tunggal maysa, kas iti saan a pannakailaok ti landok iti damili.
Ndipo monga munaona chitsulo chosakanizidwa ndi dongo, choncho anthu adzakhala wosakanizana ndipo sadzagwirizana, monga muja chitsulo sichingasakanizike ndi dongo.
44 Kadagiti al-aldaw dagitoy nga ar-ari, mangipasdekto ti Dios ti langit iti maysa a pagarian a saanto a pulos a madadael wenno maparmek dagiti sabali a tattao. Burakento daytoy dagiti dadduma a pagarian ken gibusannanto amin dagitoy, ket agtalinaedto daytoy iti agnanayon.
“Pa nthawi ya mafumu amenewo, Mulungu wakumwamba adzakhazikitsa ufumu umene sudzawonongedwa, kapenanso kuperekedwa kwa anthu ena. Udzawononga maufumu onse aja ndi kuwatheratu, koma iwo wokha udzakhalapobe mpaka muyaya.
45 Kas iti nakitam, maysa a bato ti nareggaay manipud iti bantay, ngem saan a babaen kadagiti ima ti tao. Binurakburak daytoy ti landok, bronse, damili, pirak ken balitok. Impakaammo kenka ti naindaklan a Dios, O ari, no ania ti mapasamakto kalpasan daytoy. Pudno ti tagtagainep ken mapagtalkan ti kaipapanan daytoy.”
Limeneli ndilo tanthauzo la masomphenya a mwala umene unagamuka pa phiri, koma osati ndi manja a anthu; mwala umene unaphwanya chitsulo, mkuwa, dongo, siliva ndi golide mʼtizidutswa. “Mulungu wamkulu wakuonetsani mfumu chimene chidzachitika kutsogolo. Malotowo ndi woona ndipo tanthauzo lake ndi lodalirika.”
46 Nagpakleb ni Ari Nebucadnesar iti sangoanan ni Daniel ket pinadayawanna isuna; imbilinna nga agidatonda ken mangpuorda iti insenso tapno padayawan isuna.
Pamenepo mfumu Nebukadinezara inadzigwetsa chafufumimba pamaso pa Danieli ndi kumupatsa ulemu. Ndipo inalamula kuti anthu onse amuthirire Danieli nsembe ndi kumufukizira lubani.
47 Kinuna ti ari kenni Daniel, “Pudno a ti Diosmo ket Dios dagiti dios, ti Apo dagiti ari, ken ti mangiparparang kadagiti palimed, ta nabaelam nga imparang daytoy a misterio.”
Mfumu inati kwa Danieli, “Zoonadi, Mulungu wako ndi Mulungu wa milungu ndi Ambuye wa mafumu ndi wowulula zinsinsi, pakuti iwe wathadi kuwulula chinsinsi ichi.”
48 Ket pinadayawan ti ari ni Daniel iti kasta unay, ken inikkanna isuna iti adu a sagut. Pinagbalinna isuna a mangituray iti entero a probinsia ti Babilonia. Nagbalin ni Daniel a kangatoan a gobernador kadagiti kasisiriban a lallaki ti Babilonia.
Ndipo mfumu inamukweza Danieli ndi kumupatsa mphatso zambiri. Anamuyika kuti akhale wolamulira chigawo chonse cha Babuloni ndi kutinso akhale woyangʼanira anthu ake onse anzeru.
49 Nagkiddaw ni Daniel iti ari, ket dinutokan ti ari da Sedrac, Mesac, ken Abednego nga agbalin nga administrador iti entero a probinsia ti Babilonia. Ngem nagtalinaed ni Daniel iti palasio ti ari.
Komanso, monga mwa pempho la Danieli, mfumu inayika Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti akhale oyangʼanira chigawo cha Babuloni, pamene Danieliyo ankakhazikika mʼbwalo la mfumu.

< Daniel 2 >