< Amos 7 >

1 Kastoy ti impakita ni Yahweh kaniak. Pagammoan, nangpataud isuna iti pinangen a dudon idi mangrugi nga agrusing dagiti mula, ket pagammoan, daytoy ti nabatbati a mula kalpasan a naapiten ti bingay ti ari.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
2 Kalpasan nga inibus dagiti dudon dagiti mula iti daga, kinunak, “Apo a Yahweh, pangaasim ta mamakawanka; kasano a makalasat ni Jacob? Ket nagbassit unay isuna.”
Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
3 Imbabawi ni Yahweh ti maipapan iti daytoy. “Saanto a mapasamak daytoy,” kinunana.
Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
4 Kastoy ti impakita ni Yahweh nga Apo kaniak: Pagammoan, nangayab ti Apo a ni Yahweh iti apuy tapno mangukom. Minagaan daytoy ti nalawa ken nauneg a danum nga adda iti uneg ti daga ken manguram pay koma iti daga.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
5 Ngem kinunak, “Apo a Yahweh, pangaasim ta saanmo nga aramiden dayta; kasano a makalasat ni Jacob? Ket nagbassit unay isuna.”
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
6 Imbabawi ni Yahweh ti maipanggep iti daytoy, “Uray daytoy ket saanto a mapasamak,” kinuna ni Yahweh nga Apo.
Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
7 Kastoy ti impakitana kaniak: Pagammoan, nagtakder ti Apo iti abay ti pader, nga adda iggemna a tinnag.
Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
8 Kinuna ni Yahweh kaniak, “Amos, ania ti makitkitam?” Kinunak, “Maysa a tinnag.” Ket kinuna ti Apo, “Agikabillakto iti tinnag kadagiti tattaok nga Israel. Saankonto ida nga ispalenen.
Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
9 Madadaelto dagiti nangangato a disso ni Isaac, madadaelto dagiti nasantoan a disso ti Israel, ket tumakderakto nga addaan iti kampilan maibusor iti balay ni Jeroboam.
“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
10 Kalpasana, nangipatulod ni Amasias a padi ti Betel iti maysa a mensahe kenni Jeroboam nga ari ti Israel: “Nagpanggep ni Amos maibusor kenka iti tengnga ti balay ti Israel. Saan a maibturan ti daga ti amin a saona.
Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
11 Ta kastoy ti imbaga ni Amos: 'Matayto ni Jeroboam babaen iti kampilan ken awan duadua a maitalawto a kas balud ti Israel iti lugar nga adayo iti dagana.”
Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
12 Kinuna ni Amasias kenni Amos, “Profeta, pumanawka, agsublika idiay daga ti Juda, ket manganka sadiay iti tinapay ken agipadtoka sadiay.
Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
13 Ngem saankan nga agipadto ditoy Betel gapu ta daytoy ket santuario ti ari ken balayna.”
Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
14 Ket kinuna ni Amos kenni Amasias, “Saanak a profeta wenno putot iti maysa a profeta. Agpaspastorak iti arban ken agay-aywanak kadagiti kayo a sikamoro.
Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
15 Ngem innalanak ni Yahweh iti panagpaspastorko iti arban ket kinunana kaniak, 'Mapanka agipadto kadagiti tattaok nga Israelita.'
Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
16 Ita denggem ti sao ni Yahweh. Ibagbagam, 'Saanka nga agipadto maibusor iti Israel, ken saanka nga agsao maibusor iti balay ni Isaac.'
Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
17 Ngarud, kastoy ti kuna ni Yahweh: 'Agbalinto a balangkantis iti siudad ti asawam; matayto dagiti putotmo a babbai ken lallaki babaen iti kampilan; marukod ken mabingay-bingayto ti dagam; mataykanto iti narugit a daga, ken awan duadua a maitalawto a kas balud ti Israel manipud iti dagana.”
“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”

< Amos 7 >