< Amos 4 >

1 Denggenyo daytoy a sao, dakayo a baka iti Basan, dakayo nga adda iti bantay ti Samaria, dakayo a mangidaddadanes kadagiti marigrigat, dakayo a mangparparigat kadagiti agkasapulan, dakayo a mangibagbaga kadagiti assawayo a lalaki, “Iyegandakami ti mainum.”
Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
2 Nagsapata ni Yahweh nga Apo babaen iti kinasantona: “Kitaenyo, dumtengto kadakayo dagiti aldaw nga alaendakayto babaen kadagiti kaw-it ken dagiti nabati kadakayo babaen kadagiti banniit.
Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
3 Rumuarkayonto babaen kadagiti rengngat iti pader ti siudad, tunggal maysa kadakayo ket rumuarto kadagitoy ket maitappuakkayonto iti Harmon —daytoy ti imbaga ni Yahweh.”
Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
4 “Mapankayo idiay Betel ket ipapasyo ti agbasol, mapankayo idiay Gilgal ket paadoenyo dagiti basbasolyo. Iyegyo dagiti datunyo iti tunggal agsapa, dagiti apagkapulloyo iti tunggal maikatlo nga aldaw.
“Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
5 Mangidatagkayo iti tinapay a kas sagut a panagyaman; iparammagyo dagiti daton a nagtaud iti nakemyo; ipablaakyo dagitoy, gapu ta daytoy ti pagragsakanyo, dakayo a tattao ti Israel—daytoy ti imbaga ni Yahweh nga Apo.
Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
6 “Inyegko kadakayo ti panagbisin iti amin a siudadyo ken kinakurang ti tinapay iti amin a lugaryo. Ngem saankayo a nagsubli kaniak —daytoy ti imbaga ni Yahweh.”
“Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
7 “Saanko pay a pinagtudo idi panawen nga adda pay iti tallo a bulan sakbay iti panagaapit. Pinagtudok iti maysa a siudad, ngem saanko a pinagtudo ti dadduma siudad. Maysa a paset iti daga ti natudoan, ngem ti paset ti daga a saan a natudoan ket nagtikag.
“Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
8 Nagakar akar ti dua wenno tallo a siudad iti sabali a siudad tapno uminum, ngem saanda a napnek. Ngem saankayo a nagsubli kaniak —daytoy ti imbaga ni Yahweh.”
Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
9 “Pinarigatkayo gapu iti panaglaylay ken buot. Inibus dagiti dudon ti amin a minuyonganyo, dagiti kaubasanyo, dagiti kayoyo nga igos ken dagiti kayoyo nga olibo. Ngem saankayo a nagsubli kaniak— daytoy ti imbaga ni Yahweh.”
“Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
10 Nangiyegak iti didigra kadakayo a kas iti inaramidko idiay Egipto. Pinatayko dagiti agtutuboyo a lalaki babaen iti kampilan, intalawko dagiti kabalioyo, impaalingasawko ti buyok iti kampoyo ket dimanun kadagiti agungyo. Ngem saankayo a nagsubli kaniak— daytoy ti imbaga ni Yahweh.”
“Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
11 “Pinarmekko dagiti siudadyo a kas idi pinarmek ti Dios ti Sodoma ken Gomora. Kayariganyo ti sumsumged a bislak a naikkat iti apoy. Ngem saankayo a nagsubli kaniak —daytoy ti imbaga ni Yahweh.”
“Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
12 Ngarud, nakabutbuteng ti aramidekto kadakayo, tattao ti Israel; ken gapu ta nakabutbuteng ti aramidekto kadakayo, agsaganakayo a sumango iti Diosyo, tattao ti Israel!
“Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
13 Kitaenyo, ti nangaramid kadagiti bantay isuna met lang ti nangparsua ti angin, ipakpakaammona ti kapanunotanna kadagiti tattao, pagbalbalinenna a sipnget ti aldaw ken agbadbadek kadagiti nangangato a disso iti daga.” Yahweh, Dios a mannakabalin amin ti naganna.
Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

< Amos 4 >