< Dagiti Aramid 15 >
1 Adda lallaki a bimmaba manipud idiay Judea ken sinuroanda dagiti kakabsat a lallaki, a kunada, “Malaksid a makugit kayo a mayannurot iti kaugalian ni Moises, saankayo a maisalakan.”
Anthu ena ochokera ku Yudeya anafika ku Antiokeya ndipo amaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuchita mdulidwe potsata mwambo wa Mose, simungapulumuke.”
2 Idi saan nga immanamong da Pablo ken Bernabe, ken nakisinnupiatda kadakuada, inkeddeng dagiti kakabsat a lallaki a masapul a sumang-at da Pablo, Bernabe, ken dadduma pay idiay Jerusalem, ket mapanda kadagiti apostol ken panglakayen maipanggep iti daytoy a saludsod.
Zimenezi zinachititsa Paulo ndi Barnaba kuti atsutsane nawo kwambiri. Kotero Paulo ndi Barnaba anasankhidwa pamodzi ndi abale ena kuti apite ku Yerusalemu kukaonana ndi atumwi ndi akulu ampingo kukakambirana za nkhaniyi.
3 Ngarud, iti panangibaon kadakuada ti iglesia, nagnada idiay Fenicia ken Samaria ket impadamagda ti panamati dagiti Hentil. Nangyegda iti kasta unay a rag-o kadagiti amin a kakabsat a lallaki.
Mpingo unawaperekeza, ndipo pamene amadutsa ku Foinike ndi Samariya, iwo anafotokoza momwe a mitundu ina anatembenukira mtima. Nkhani imeneyi inakondweretsa kwambiri abale onse.
4 Idi dimtengda idiay Jerusalem, pinasangbay ida ti iglesia ken dagiti apostol ken dagiti panglakayen, ket impadamagda dagiti amin a banbanag nga inaramid ti Dios kadakuada.
Atafika ku Yerusalemu, iwo analandiridwa ndi mpingo, pamodzi ndi atumwi ndiponso akulu ampingo. Paulo ndi Barnaba anawafotokozera zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo.
5 Ngem adda dagiti lallaki a namati, a kameng ti bunggoy dagiti Pariseo, a nagtakder ken kinunada, “Kasapulan a makugitda ken surotenda ti linteg ni Moises.
Kenaka, okhulupirira ena amene kale anali a gulu la Afarisi anayimirira ndipo anati, “Anthu a mitundu ina ayenera kuchita mdulidwe ndi kusunga malamulo a Mose.”
6 Naummong ngarud dagiti apostol ken dagiti panglakayen tapno pagtutungtonganda daytoy a banag.
Atumwi ndi akulu ampingo anasonkhana kuti akambirane za nkhaniyi.
7 Kalpasan ti adu a panagsisinnuppiat, nagtakder ni Pedro ket kinunana kadakuada, “Kakabsat a lallaki, ammoyo nga iti nabayagen a tiempo, nangpili ti Dios kadakayo, a babaen iti ngiwatko ket mangngeg dagiti Hentil ti ebanghelio, ken mamatida.
Atakambirana kwambiri Petro anayimirira, ndipo anawayankhula nati: “Abale, mukudziwa kuti masiku oyambirira Mulungu anandisankha ine pakati panu kuti anthu a mitundu ina amve kuchokera pakamwa panga mawu a Uthenga Wabwino ndi kukhulupirira.
8 Ti Dios, a makaammo iti adda iti puso, ket agsaksi kadakuada, itedna kadakuada ti Nasantoan nga Espiritu, kas inaramidna kadatayo;
Mulungu amene amadziwa mtima wa munthu, Iye anaonetsa kuti anawalandira powapatsa Mzimu Woyera, monga momwe anachita kwa ife.
9 ket awan indumdumana kadatayo ken kadakuada, ket pinagbalinna a nadalus dagiti pusoda babaen iti pammati.
Iye sanasiyanitse pakati pa ife ndi iwo, pakuti anayeretsa mitima yawo mwachikhulupiriro.
10 Ita ngarud, apay a suotenyo ti Dios, ta kinabilanyo iti sangol dagiti tengged dagiti adalan nga uray pay dagiti ammatayo ken datayo ket saantayo a kabaelan a baklayen?
Tsopano, chifukwa chiyani mukuyesa Mulungu poyika goli mʼkhosi la ophunzira, limene ngakhale ife kapena makolo athu sangathe kulisenza?
11 Ngem mamati tayo a maisalakan tayo babaen iti parabur ni Apo Jesus, kas kadakuada idi.”
Osatero! Ife tikukhulupirira kuti tinapulumutsidwa mwachisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, monga iwonso anachitira.”
12 Nagtalna amin dagiti tattao kabayatan nga agdengdengngegda iti ipadpadamag da Bernabe ken Pablo maipanggep kadagiti pagilasinan ken kadagiti nakaskasdaaw nga inaramid ti Dios kadagiti Hentil, babaen kadakuada.
Gulu lonse linakhala chete pamene amamvetsera Barnaba ndi Paulo akuwawuza za zizindikiro zodabwitsa zimene Mulungu anazichita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo.
13 Kalpasan iti panagsaoda, simmungbat ni Santiago, kinunana,” Kakabsat a lallaki, dumngegkayo kaniak.
Iwo atatha kuyankhula, Yakobo anayankhula nati: “Abale, tandimverani.
14 Imbaga ni Simon no kasano a sipaparabur a tinulungan nga immuna ti Dios dagiti Hentil tapno iti kasta ket adda tattao nga agtaud kadakuada a maipaay iti naganna.
Simoni watifotokozera mmene Mulungu poyamba paja anaonetsa kukhudzidwa kwake pomwe anatenga anthu a mitundu ina kukhala ake.
15 Umanamong iti daytoy dagiti sasao dagiti profeta, kas naisurat,
Mawu a aneneri akuvomereza zimenezi, monga kwalembedwa kuti,
16 Agsubliakto kalpasan dagitoy a banbanag, ken ipatakderko manen ti tolda ni David, a narba; Tarimaanekto ken ipatakderko manen dagiti nabati a pasetna,
“‘Zitatha izi Ine ndidzabwerera ndipo ndidzamanganso nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso,
17 tapno dagiti nabati a tattao ket mabalinda a biruken ti Apo, pakairamanan dagiti amin a Hentil a naawagan babaen iti naganko.'
kuti anthu otsalawo afunefune Ambuye, ndi anthu onse a mitundu ina amene atchedwa ndi dzina langa, akutero Ambuye, amene amachita zinthu zimenezi
18 Daytoy ti ibagbaga ti Apo, a nangaramid kadagitoy a banbanag a naammoanen idi pay laeng un-unana a tiempo. (aiōn )
zinaululidwa kuyambira kalekale.’ (aiōn )
19 Isu a ti kapanunotak ket saantayo a riribuken dagiti Hentil nga nagsubli iti Dios;
“Chifukwa chake, ine ndikuweruza kuti tisamavute anthu a mitundu ina amene atembenuka mtima kutsata Mulungu.
20 ngem agsurattayo ketdi kadakuada a masapul nga umadayoda manipud iti panangtulaw dagiti didiosen, manipud iti immoralidad, ken manipud iti aniaman a nabekkel, ken manipud iti dara.
Koma tiwalembere iwo, kuwawuza kuti asadye chakudya choperekedwa kwa mafano, apewenso dama, asadyenso nyama zochita kupotola kapena kudya magazi.
21 Manipud pay kadagiti nagkauna a kaputotan, addan dagiti tattao iti tunggal siudad a mangikaskasaba ken mangibasbasa iti insurat ni Moises kadagiti sinagoga, tunggal Aldaw ti Panaginana”.
Pakuti malamulo a Mose akhala akulalikidwa mu mzinda uliwonse, kuyambira kalekale ndipo amawerengedwa mʼMasunagoge tsiku la Sabata.”
22 Ket kasla nasayaat kadagiti apostol ken kadagiti panglakayen, kaduada ti isu amin nga iglesia, a pilienda ni Judas a managan metlaeng Barsabas, ken ni Silas, a mangidadaulo iti iglesia, ken ibaonda ida idiay Antiokia a kaduada ni Pablo ken Bernabe.
Pamenepo atumwi ndi akulu ampingo, pamodzi ndi mpingo onse, anagwirizana zosankha anthu ena pakati pawo kuti awatume ku Antiokeya pamodzi ndi Paulo ndi Bamaba. Iwo anasankha Yudasi, wotchedwa Barsaba ndi Sila, anthu awiri amene anali atsogoleri pakati pa abale,
23 Insuratda daytoy, “Dagiti apostol, dagiti panglakayen ken kakabsat a lallaki, kadagiti kakabsat a Hentil iti Antiokia, Siria ken Cilicia, kablaaw.
kuti akapereke kalata yonena kuti, Kuchokera kwa atumwi ndi akulu ampingo, abale anu, Kwa anthu a mitundu ina okhulupirira a ku Antiokeya, Siriya ndi Kilikiya: Tikupereka moni.
24 Nangngegmi nga adda dagiti lallaki, a saanmi met a binilin, a naggapu kadakami ti nangburiborkakayo kadagiti panursuro a nangburibor kadagiti kararuayo.
Ife tamva kuti anthu ena ochokera pakati pathu, amene sitinawatume anakusokonezani maganizo ndi kukuvutitsani ndi zimene amakuwuzani.
25 Isu a kasla nasayaat para kadakami amin nga agkaykaysa a mangpili iti lallaki ken ibaonmi ida kadakayo, kaduada dagiti ay-ayatenmi a Bernabe ken Pablo,
Tsono ife tagwirizana kuti, tisankhe anthu ena ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi abale athu okondedwa Paulo ndi Barnaba,
26 tattao a nagpeggad dagiti bibiagda para iti nagan ni Apo tayo a Jesu-Cristo.
anthu amene anapereka moyo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
27 Imbaonmi ngarud da Judas ken Silas, a mangibaga met laeng kadakayo iti isu met laeng a banbanag.
Nʼchifukwa chake, tikutumiza Yudasi ndi Sila kuti adzachitire umboni ndi mawu a pakamwa pawo za zimene ife talemba.
28 Ta daytoy ket kasla nasayaat met iti Espiritu Santo ken kadakami, a saankamin a mangted kadakayo iti ad-adu a dadagsen no di laeng dagitoy a napapateg a banbanag:
Pakuti zinakomera Mzimu Woyera ndiponso ife kuti tisakusenzetseni katundu wina, kupatula zoyenera zokhazi:
29 nga adaywanyo dagiti banbanag a naidaton kadagiti didiosen, dara, banbanag a nabekkel, ken manipud iti immoralidad. No saluaddanyo dagiti bagbagiyo manipud kadagitoy, nasayaat ti pagbanaganyo. Agpakadakamin.”
Mupewe kudya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano, musadye magazi, kapena nyama yopha mopotola ndiponso musachite dama. Mudzachita bwino mukapewa zimenezi. Tsalani bwino.
30 Isu nga isuda, idi napalubusanda, simmalogda idiay Antiokia; kalpasan nga inummongda dagiti adu a tattao, inyawatda ti surat.
Anthu aja anatumidwa ndipo anafika ku Antiokeya, kumene anasonkhanitsa mpingo pamodzi napereka kalatayo.
31 Idi nabasada daytoy, naragsakanda gapu iti pannangpabileg.
Anthuwo anawerenga kalatayo ndipo abalewo anakondwa chifukwa cha mawu ake achirimbikitso.
32 Da Judas ken Silas, a maibilang met a profeta, pinaregtada dagiti kakabsat a lallaki babaen iti adu a sasao ken pinapigsada ida.
Yudasi ndi Sila amene analinso aneneri, ananena zambiri zowalimbikitsa ndi kuwapatsa mphamvu abalewo.
33 Kalpasan a nagtalinaedda sadiay iti sumagmamano a tiempo, napalubosanda a pumanaw a sitatalna manipud kadagiti kakabsat a lallaki tapno agsublida kadagiti nangibaon kadakuada.
Atakhala kumeneko kwa kanthawi, abale aja anatsanzikana nawo mwamtendere kuti abwerere kwa amene anawatuma.
Koma Sila anasankha kuti akhale komweko.
35 Ngem da Pablo ken ni Bernabe ket nagtalinaed idiay Antiokia a kaduada dagiti dadduma pay, a no sadino ket insuro ken inkasabada ti sao ti Apo.
Koma Paulo ndi Barnaba anatsalira ku Antiokeya kumene iwo pamodzi ndi ena ambiri anaphunzitsa ndi kulalikira Mawu a Ambuye.
36 Kalpasan iti mano nga aldaw, imbaga ni Pablo kenni Bernabe, “Agsublitan ita ken bisitaenta dagiti kakabsat a lallaki iti tunggal siudad a nangiwaragawaganta iti sao ti Apo, ken kitaenta no kasano iti kasasaadda.
Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.”
37 Kayat ni Bernabe nga ikuyog met ni Juan a maawagan Marcos.
Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo.
38 Ngem pinanunot ni Pablo a saan a nasayaat nga ikuyogda ni Marcos, a nangpanaw kadakuada idiay Pamfilia ken saan a nagtuloy a kimmuyog kadakuada iti trabaho.
Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito.
39 Kalpasan ket adda rimsua a nabara a panagsinnupiat, isu a nagsisinada, ket inkuyog ni Bernabe ni Marcos ket naglayagda nga immadayo a nagturong idiay Cyprus.
Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro.
40 Ngem pinili ni Pablo ni Silas ket pimmanawda, kalpasan nga intalek isuna dagiti kakabsat a lallaki iti parabur ti Apo.
Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka.
41 Ket napan isuna idiay Siria ken Cilicia, a nangpabpabileg kadagiti iglesia.
Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.