< II Samuel 7 >

1 Apaman a nagnaed ti ari iti balayna, ken pinaginana isuna ni Yahweh manipud kadagiti amin a nakapalawlaw a kabusorna,
Mfumu itakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, Yehova atayipatsa mpumulo kwa adani ake onse woyizungulira,
2 kinuna ti ari kenni Natan a profeta, “Kitaem, agnanaedak iti balay a sedro, ngem agtaltalinaed ti Lakasa ti Tulag ti Dios iti tengnga ti tolda.”
mfumuyo inawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Mulungu lili mu tenti.”
3 Ket kinuna ni Natan iti ari, “Mapanka, aramidem ti adda dita pusom, ta adda ni Yahweh kenka.”
Natani anayankha mfumu kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu chifukwa Yehova ali nanu.”
4 Ngem iti dayta met la a rabii immay ti sao ni Yahweh kenni Natan ket kinunana,
Usiku umenewo mawu a Yehova anafika kwa Natani ndipo anati,
5 “Mapanka ket ibagam kenni David nga adipenko, 'Kastoy ti kuna ni Yahweh: Ibangonannak kadi iti balay a pagnaedak?
“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti: kodi ndiwe amene udzandimangira Ine nyumba yokhalamo?
6 Ta saanak pay a nagnaed iti balay sipud idi aldaw nga inruarko dagiti tattao ti Israel manipud Egipto inggana kadagitoy nga aldaw; ngem ketdi, agakar-akarak iti tolda, ti tabernakulo.
Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda uku ndi uku ndipo mokhala mwanga munali mu tenti.
7 Kadagiti amin a lugar a nagakar-akarak a kaduak dagiti amin a tattao ti Israel, adda kadi imbagak iti siasinoman kadagiti mangidadaulo kadagiti Israelita a dinutokak a mangaywan kadagiti tattaok nga Israel, nga ibagbagak, “Apay a saandak nga impatakderan iti balay a sedro?”'”
Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense atsogoleri awo, amene ndinamulamula kuweta anthu anga Aisraeli kuti, nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’”
8 Ita ngarud, ibagam kenni David nga adipenko, “Kastoy ti kuna ni Yahweh a mannakabalin amin: 'Innalaka manipud iti pagpaspasturan, manipud iti panagpaspastormo iti karnero, tapno iturayam dagiti tattaok nga Israel.
“Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
9 Kinaduaanka sadinoman iti napanam ken pinapatayko iti sangoanam dagiti amin a kabusormo. Ken aramidek a natan-ok ti naganmo, kasla nagan dagiti natan-ok a tattao nga adda iti rabaw ti daga.
Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi.
10 Mangisaadak iti lugar a para kadagiti tattaok nga Israel ket pagtalinaedek ida sadiay, tapno makapagnaedda kadagiti bukodda a lugar ket saandanton a mariribukan. Awanton dagiti nadangkes a tattao a mangparigat kadakuada, a kas inaramidda idi,
Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja,
11 ti ar-aramidenda manipud kadagidi nga aldaw a binilinko dagiti uk-ukom nga agturay kadagiti tattaok nga Israel. Ket paginanaenka manipud kadagiti amin a kabusormo. Maysa pay, Siak, ni Yahweh, ibagak kenka nga iyaramidanka iti balay.
monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzakupatsaninso mpumulo kwa adani anu onse. “‘Yehova akulengeza kwa iwe kuti Iye mwini adzakhazikitsa banja lako:
12 Inton malpasto dagiti aldawmo ket maitiponka kadagiti ammam, pataudekto ti sumukat kenka manipud kadagiti kaputotam, maysa nga agtaud iti mismo a bagim, ket ipasdekonto ti pagarianna.
Masiku ako akadzatha ndipo ukadzakapuma ndi makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, imene idzachokera mʼthupi mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake.
13 Mangbangunto isuna iti balay gapu iti naganko, ken pagtaginayunekto ti trono iti pagarianna.
Iye ndiye amene adzamangire nyumba Dzina langa, ndipo Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya.
14 Agbalinnakto nga amana, ket agbalinto met isuna nga anakko. No makabasol isuna, adalakto isuna babaen iti sarukod dagiti tattao ken babaen iti panangsaplit kadagiti annak ti tattao.
Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Akadzachita choyipa, Ineyo ndidzamulanga ndi ndodo ndi zikwapu za anthu.
15 Ngem agtalinaed kenkuana ti kinapudno ti tulagko, a kas imbabawik kenni Saul, nga inikkatko sakbay a nagarika.
Koma sindidzasiya kumukonda, monga ndinachitira ndi Sauli, amene ndinamuchotsa iwe usanakhale mfumu.
16 Mapasingkedanto nga agtalinaed iti agnanayon ti balay ken pagariam. Agtalinaedto nga agnanayon ti tronom.'”
Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhala zamuyaya pamaso panga. Mpando wako waufumu udzakhazikika kwamuyaya!’”
17 Kinasarita ni Natan ni David ket imbagana kenkuana amin dagitoy a sasao, ken imbagana kenkuana ti sibubukel a sirmata.
Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.
18 Ket immuneg ni ari David ket natugaw iti sangoanan ni Yahweh; kinunana, “Siasino-ak koma, O Yahweh a Dios, ken ania koma ti pamiliak ta inyegnak iti kastoy a kasasaad?
Choncho Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati: “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ine ndine yani, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa?”
19 Bassit daytoy a banag iti imatangmo, Apo a Yahweh. Imbagam pay ti maipanggep iti pamilia ti adipenmo a dumtengto ti naindaklan a tiempo, ken impakitam kaniak dagiti sumarsaruno a kaputotak, Apo a Yahweh!
Ndipo kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Kodi umu ndi mmene mumachitira ndi munthu, Inu Ambuye Wamphamvuzonse?
20 Siak daytoy ni David, ania pay ti maibagak kenka? Pinadayawam ti adipenmo, Apo a Yahweh.
Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu? Pakuti Inu Ambuye Wamphamvuzonse mukumudziwa mtumiki wanu.
21 Para kadagiti sasaom, ken tapno matungpal ti bukodmo a panggep, inaramidmo dagiti naindaklan a banbanag ken imparangmo daytoy iti adipenmo.
Chifukwa cha mawu anu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwachiwulula kwa mtumiki wanu.
22 Ngarud naindaklanka, Apo a Yahweh. Ta awan ti kas kenka, ken awanen ti Dios malaksid kenka, kas kadagiti nangnangngegmi.
Inu ndinu wamkulu, Yehova Wamphamvuzonse! Palibe wina wofanana nanu, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha, monga tamvera ndi makutu athu.
23 Ken ania a nasion ti kasla kadagiti tattaom nga Israelita, ti maysa a nasion iti rabaw ti daga a napanam ken inispalmo, Dios, a para kenka? Inaramidmo daytoy tapno agbalinda a tattaom, a mangitag-ay iti naganmo, ken agaramid kadagiti naindaklan ken nakaskasdaaw nga ar-aramid para iti dagam. Pinapanawmo dagiti nasion ken dagiti didiosenda manipud iti sangoanan dagiti tattaom, nga inispalmo manipud idiay Egipto.
Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina ndi milungu yawo pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto?
24 Inaramidmo ti Israel a bukodmo a tattao iti agnanayon, ken sika, Yahweh ti nagbalin a Diosda.
Inu mwawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.
25 Isu nga ita, Yahweh a Dios, dagiti koma ingkarim a maipapan iti adipenmo ken iti pamiliana ket mapasamak iti agnanayon. Aramidem koma a kas iti imbagam.
“Ndipo tsopano Yehova Mulungu, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake. Chitani monga mwalonjezera,
26 Mataginayon koma a naindaklan ti naganmo, tapno ibaganto dagiti tattao, 'Ni Yahweh a mannakabalin amin ti Dios ti Israel,' kabayatan a maibangbangon iti sangoanam ti balayko, David, toy adipenmo.
kotero dzina lanu lidzakhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.
27 Ta sika, Yahweh a mannakabalin amin, a Dios ti Israel, ti nangipablaak iti adipenmo nga iyaramidamto isuna iti balay. Dayta ti makagapu a siak, ti adipenmo, ket napakired nga agkararag kenka.
“Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, mwaululira mtumiki wanu ponena kuti, ‘Ine ndidzakumangira iwe nyumba!’ Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere.
28 Ita, Apo a Yahweh, Dioska, ken mapagtalkan dagiti sasaom, ken inkarim daytoy nasayaat a kari iti adipenmo.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, ndinu Mulungu! Mawu anu ndi odalirika, ndipo mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu.
29 Ita ngarud, maay-ayonaka koma daytoy a mangbendision iti balay ti adipenmo, tapno agtultuloy daytoy iti agnanayon iti sangoanam. Ta sika, Apo a Yahweh ti nangibaga kadagitoy a banbanag, ken babaen iti panangbendisionmo agnanayunto a maparparaburan ti balay ti adipenmo.”
Ndipo tsopano chikukomereni kudalitsa banja la mtumiki wanu, kuti likhale mpaka muyaya pamaso panu. Pakuti Inu, Yehova Wamphamvuzonse, mwayankhula, ndipo ndi mʼdalitso wanu banja la mtumiki wanu lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

< II Samuel 7 >