< 2 Ar-ari 4 >

1 Ita, napan a nagsangsangit kenni Eliseo ti asawa ti maysa kadagiti annak dagiti profeta, ibagbagana, “Natayen ti asawak nga adipenmo, ket ammom a managbuteng ti adipenmo kenni Yahweh. Ita, immay ti agpapautang tapno alaenna ti dua nga annakko nga agbalin a tagabuna.”
Mkazi wa mmodzi mwa ana a aneneri anafuwula kwa Elisa kuti, “Mtumiki wanu, mwamuna wanga wamwalira ndipo inu mukudziwa kuti ankaopa Yehova. Koma tsopano munthu amene mwamuna wanga anakongolako zinthu zake, akubwera kudzatenga ana anga awiri aamuna kuti akhale akapolo ake.”
2 Isu a kinuna ni Eliseo iti babai, “Ania ti maipaayko kenka? Ibagam kaniak ti adda iti balaymo?” Kinuna ti babai, “Awan a pulos iti adda iti balay ti adipenmo, malaksid iti sangaputik a lana.”
Elisa anayankha mayiyo kuti, “Kodi ufuna ndikuchitire chiyani? Tandiwuza uli ndi chiyani mʼnyumba mwako?” Mayiyo anayankha kuti, “Mdzakazi wanu alibe kanthu kalikonse koma timafuta pangʼono chabe.”
3 Ket kinuna ni Eliseo, “Rummuarka tapno mapanka bumulod kadagiti kaarrubam kadagiti burnay nga awan nagianna. No mabalbalin bumulodka iti adu.
Elisa anati, “Pita kabwereke mitsuko yonse yopanda kanthu kwa anzako. Usakabwereke mitsuko yochepa.
4 Kalpasanna masapul a sumrekka ken dagiti annakmo ket irekepyo ti ridaw, ket bukbukanyo ti lana amin dagitoy a burnay; ilasinyo dagiti burnay a napunno.”
Kenaka ukalowe mʼnyumba mwako ndi kudzitsekera iwe ndi ana ako. Mukakatero mukakhuthulire mafuta mʼmitsuko yonseyo, ndipo mtsuko uliwonse ukadzaza muzikawuyika pambali.”
5 Isu a pinanawanna ni Eliseo ket inrekepna ti ridaw iti likudanna ken dagiti annakna. Impanda kenkuana dagiti burnay, ket pinunnona dagitoy iti lana.
Mayi uja anachoka kwa Elisa nakadzitsekera ndi ana ake. Anthu anabweretsa mitsuko kwa iye ndipo ankathiramo mafuta.
6 Idi napnon dagiti pagkargaan, kinunana iti anakna, “Mangiyegka kaniak ti sabali a burnay.” Ngem kinunana kenkuana, “Awanen ti burnay.” Ket nagsardeng a nagayus ti lana.
Mitsuko yonse itadzaza, mayiyo anawuza mwana wake kuti, “Bweretsa mtsuko wina.” Koma iye anayankha kuti, “Mitsuko yonse yatha.” Pamenepo mafuta analeka kutuluka.
7 Kalpasanna, nagsubi ti babai ket imbagana iti tao ti Dios. Kinunana, “Mapanka, ilakom ti lana; bayadam ti utangmo, ket pagbiaganyo kadagiti annakmo ti nabati.”
Mayiyo anapita nakamuwuza munthu wa Mulungu amene anamuyankha kuti, “Pita, kagulitse mafutawo ndipo ukabweze ngongole ija. Ndalama zotsalazo zikakhale zako ndi ana ako.”
8 Maysa nga aldaw, nagna ni Eliseo idiay Sunem a pagnanaedan ti babai a baknang; inawis ti babai isuna a makipangan kenkuana. Isu a tunggal lumabas ni Eliseo, dumagas isuna sadiay tapno mangan.
Tsiku lina Elisa anapita ku Sunemu. Kumeneko kunkakhala mayi wina wachuma amene anawumiriza Elisa kuti adye chakudya. Choncho nthawi iliyonse imene Elisa amadutsa kumeneko, ankayima ndi kudya.
9 Kinuna ti babai iti asawana, “Kitaem, ita maamirisko a nasantoan daytoy a tao ti Dios a kanayon a lumablabas.
Mayiyo anawuza mwamuna wake kuti, “Taonani, ine ndikudziwa kuti munthu amene amadutsa pano nthawi zambiriyu ndi munthu woyera wa Mulungu.
10 Mangaramidta iti bassit a siled iti ngato a para kenni Eliseo, ket mangikabilta iti pagiddaan, lamisaan, tugaw, ken silaw. Ket inton sarungkarannata, agyanto isuna sadiay.”
Tiyeni timumangire kachipinda kakangʼono pa denga la nyumbayi ndi kumuyikiramo bedi ndi tebulo, mpando ndi nyale. Akabwera kuno azikhala mʼmenemo.”
11 Isu nga idi dimteng manen ti aldaw a dimmagas ni Eliseo sadiay, nagyan isuna iti siled ket naginana sadiay.
Tsiku lina pamene Elisa anafika ku Sunemu, iye anakalowa mʼchipinda chake chija nagona mʼmenemo.
12 Kinunana ni Elias kenni Gehazi nga adipenna, “Ayabam daytoy a Sunamita.” Idi naayabanna ti babai, nagtakder ni Gehazi iti sangngoananna.
Iye anati kwa mtumiki wake Gehazi, “Muyitane Msunemuyu.” Ndipo anapita kukamuyitana mayiyo, ndipo anabwera nayima pamaso pa Elisa.
13 Kinuna ni Eliseo kenkuana, “Ibagam iti babai, 'Naaramidmo amin dagitoy a pakaseknan a mangaywan kadakami. Ania ti maipaaymi a para kenka? Kayatmo kadi a katungtongenmi para kenka iti ari wenno iti komadante ti armada?” Simmungbat ti babai, “Agnanaedak kadagiti tattaok.”
Elisa anati kwa Gehazi, “Muwuze mayiyo kuti, ‘Wavutika potichitira zonsezi. Nanga tsopano ifeyo tikuchitire chiyani? Kodi ukufuna kuti tikadziwitse mfumu kapena mtsogoleri wa ankhondo zimene watichitirazi?’” Mayiyo anayankha kuti, “Ine ndimakhala mwamtendere pakati pa abale anga.”
14 Isu a kinuna ni Eliseo, “Ania ngarud ti aramidenta para kenkuana?” Simmungbat ni Gehazi, “Iti kinapudnona, awan iti anakna, ket lakayen ti asawana.”
Elisa anafunsanso Gehazi kuti, “Kodi tingamuchitire chiyani?” Gehazi anati, “Ndithu, mayiyu alibe mwana ndipo mwamuna wake ndi wokalamba.”
15 Isu a simmungbat ni Eliseo, “Ayabam ti babai.” Idi naayabanna isuna, nagtakder ti babai iti ridaw.
Pamenepo Elisa anati, “Muyitane.” Choncho Gehazi anamuyitana, ndipo iye anabwera nayima pa khomo.
16 Kinuna ni Eliseo, “Iti kastoy a tiempo, iti umay a tawen, ub-ubbaemton ti anak a lalaki.” Kinuna ti babai, “Saan, apok ken tao ti Dios, saanka nga agulbod iti adipenmo.”
Elisa anati kwa mayiyo, “Nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, udzakhala utanyamula mwana wamwamuna mʼmanja mwako.” Mayiyo anatsutsa zimenezi nanena kuti, “Ayi mbuye wanga. Inu munthu wa Mulungu, musanamize mdzakazi wanu!”
17 Ngem nagsikog ti babai ket nangipasngay isuna iti anak a lalaki iti dayta met laeng a tiempo iti sumaruno a tawen, kas iti kinuna ni Eliseo kenkuana.
Koma mayi uja anakhala woyembekezera, ndipo chaka chotsatiracho, nthawi ngati yomweyo anabereka mwana wamwamuna monga momwe Elisa anamuwuzira.
18 Idi dimmakkelen ti ubing, maysa nga aldaw, napan isuna iti ayan iti amana, a kaduana dagiti agburburas.
Mwana uja anakula, ndipo tsiku lina anapita kwa abambo ake amene anali ndi anthu odula tirigu.
19 Kinunana iti amana, “Ti ulok, ti ulok.” Kinuna ti amana iti adipenna, “Bagkatem isuna nga ipan iti inana.”
Mwanayo anafuwula kwa abambo ake kuti, “Mayo! Mutu wanga ine! Mayo! Mutu wanga ine!” Abambo akewo anawuza wantchito wake kuti, “Munyamule ndi kukamupereka kwa amayi ake.”
20 Idi binagkat ti adipen ti ubing ket impanna iti inana, sinaklot ti babai ti ubing agingga a natay iti agmatuon.
Wantchito uja atamunyamula ndi kumupereka kwa amayi ake. Mwanayo anakhala pa miyendo ya amayi akeyo mpaka masana, ndipo pambuyo pake anamwalira.
21 Isu a timmakder ti babai ket impaiddana ti ubing iti pagiddaan ti tao ti Dios, inrekepna ti ridaw, ket rimmuar.
Mayiyo ananyamula mwanayo nakamugoneka pa bedi la munthu wa Mulungu uja. Kenaka anatseka chitseko iye nʼkuchokapo.
22 Inayabanna ti asawana, ket kinunana, “Pangaasim, ibaonmo kaniak ti maysa kadagiti adipen ken maysa kadagiti asno tapno makapanak a dagus iti tao ti Dios ket kalpasanna makasubliak.”
Iye anayitanitsa mwamuna wake namuwuza kuti, “Tumizireni wantchito mmodzi ndi bulu mmodzi kuti ndipite mofulumira kwa munthu wa Mulungu nʼkubwererako.”
23 Kinuna ti asawa ti babai, “Apay a kayatmo ti mapan kenkuana ita nga aldaw? Saan met a baro ti bulan wenno Aldaw a Panaginana, “Simmungbat isuna, “Saan a bale.”
Mwamuna wakeyo anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani ukupita kwa iyeyo lero? Lero si tsiku la Chikondwerero cha Mwezi Watsopano kapena tsiku la Sabata.” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
24 Kalpasanna sinilyaanna ti asno ket kinunana iti adipenna, “Partakam a patarayen; saanmo a pagin-innayaden malaksid no ibagak.”
Mayiyo anamangirira chishalo pa bulu ndipo anawuza wantchito wake kuti, “Yendetsa bulu mofulumira. Usachepetse liwiro pokhapokha nditakuwuza.”
25 Isu a napan isuna ket nakadanon iti ayan iti tao ti Dios idiay Bantay Carmel. Isu nga idi nakita ti tao ti Dios ti babai iti saan unay nga adayo, kinunana kenni Gehazi nga adipenna, “Kitaem, sumungsungad ti babai a Sunamita.
Choncho ananyamuka nakafika kwa munthu wa Mulungu uja ku Phiri la Karimeli. Munthu wa Mulungu ataona mayiyo patali, anawuza mtumiki wake Gehazi kuti, “Taona! Msunemu uyo!
26 Pangngaasim, tumarayka a mangsabat kenkuana ket ibagam kenkuana, 'Nasayaat kadi ti kasasaadmo kasta met ti asawam ken ti anakmo?'” Simmungbat ti babai, “Nasayaat ti amin.”
Thamanga msanga ukakumane naye ndipo ukamufunse kuti, ‘Kodi muli bwino? Kodi mwamuna wanu ali bwino? Kodi mwana wanu ali bwino?’” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
27 Idi nakadanon ti babai iti ayan iti tao ti Dios nga adda idiay bantay, iniggamanna ti sakana. Immasideg ni Gehazi iti babai tapno iyadayona ngem kinuna ti tao ti Dios, “Panawam isuna, ta mariribukan unay, ken inlimed ni Yahweh daytoy a parikut, ken awan ti imbagana kaniak.”
Atafika kwa munthu wa Mulunguyo pa phiripo, mayiyo anagwira mapazi a Elisa. Gehazi anabwera kuti amukankhe, koma munthu wa Mulungu anati, “Musiye! Iyeyu ali pa mavuto aakulu, koma Yehova wandibisira zimenezi ndipo sanandiwuze chifukwa chake.”
28 Kalpasanna, kinuna ti babai, “Nagkiddawak kadi kenka iti anak, apok? Saanko kadi nga imbaga, 'Saannak nga ulbodan'?”
Tsono mayiyo anati, “Mbuye wanga, kodi ine ndinakupemphani mwana? Kodi sindinakuwuzeni kuti musandinamize?”
29 Ket kinuna ni Eliseo kenni Gehazi, “Agrubuatka ket alaem ti sarukodko. Mapanka iti pagtaenganna. No adda masabatmo a lalaki, saanmo a kablaawan isuna, ken no adda mangkablaaw kenka, saanmo a sungbatan. Iparabawmo ti sarukodko iti rupa ti ubing.”
Elisa anawuza Gehazi kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga ndodo yanga mʼdzanja lako ndipo thamanga. Ngati ukumana ndi munthu wina aliyense, usamupatse moni, ndipo ngati wina akupatsa moni, usayankhe. Ukagoneke ndodo yanga pa nkhope ya mwanayo.”
30 Ngem kinuna ti ina ti ubing, “Iti nagan ni Yahweh nga adda iti agnanayon, ken kas sibibiagka, saanka a panpanawan.” Isu a timmakder ni Eliseo ket simmurot iti babai.
Koma mayi wake wa mwana uja anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Choncho Elisa ananyamuka natsatira mayiyo.
31 Nagdardaras ken inunaan ni Gehazi isuda ket imparabawna ti sarukod iti rupa ti ubing, ngem saan a nagsao wenno nakangeg ti ubing. Kalpasanna nagsubli ni Gehazi a mangsabat kenni Eliseo ket imbagana kenkuana, “Saan a mariing ti ubing.”
Gehazi anatsogola nakagoneka ndodoyo pa nkhope ya mwanayo, koma sipanamveke mawu kapena kugwedezeka kuonetsa kuti ali moyo. Choncho Gehazi anabwerera kukakumana ndi Elisa ndipo anamuwuza kuti, “Mwanayo sanatsitsimuke.”
32 Idi nakasanngpet ni Eliseo iti balay, natayen ti ubing ket adda pay laeng iti pagiddaan.
Ndipo Elisa atafika ku nyumbako, taonani, mwanayo anali wakufa atamugoneka pa bedi lake.
33 Isu a simrek ni Eliseo ket inrekepna ti ridaw nga ayan iti ubing ket nagkakarag kenni Yahweh.
Elisa analowa mʼnyumbamo natseka chitseko. Anali awiri okha mʼchipindamo ndipo iye anapemphera kwa Yehova.
34 Napanna pinakleban ti ubing; indekketna ti ngiwatna iti ngiwat ti ubing, ti matana iti mata ti ubing ken ti imana iti ima ti ubing. Impaklebna ti bagina iti ubing a lalaki, ket bimmara ti bagi ti ubing.
Kenaka anakwera pa bedi ndi kumugonera mwanayo, pakamwa pake panakhudzana ndi pakamwa pa mwanayo, maso ake anakhudzana ndi maso a mwanayo, ndipo manja ake anakhudzana ndi manja a mwanayo. Pamene ankadzitambalitsa yekha pa mwanayo, thupi la mwanayo linayamba kufunda.
35 Kalpasanna timmakder ni Eliseo ket nagpagnapagna iti siled ket nagsubli manen ket impaklebna ti bagina iti ubing a lalaki. Nagbaeng ti ubing iti pito a daras sana inmulagat dagiti matana!
Elisa anatembenuka nayenda uku ndi uku kamodzi mʼchipindamo ndipo kenaka anakweranso pa bedi nagoneranso mwanayo. Mwanayo anayetsemula kasanu ndi kawiri ndipo anatsekula maso ake.
36 Isu nga inayaban ni Eliseo ni Gehazi ket kinunana, “Ayabam ti Sunamita!” Isu nga inayabanna ti babai, ket idi nakastrek isuna iti siled, Kinuna ni Eliseo, “Alaemon ti anakmo.”
Elisa anayitana Gehazi ndipo anati, “Muyitane Msunemuyo.” Ndipo anaterodi. Mayiyo atabwera, Elisa anati, “Tenga mwana wako.”
37 Ket nagpakleb ti babai iti daga iti sakaananna ken nagkurno isuna iti daga, kalpasanna, innalana ti anakna sa pimmanaw.
Mayiyo analowa, nagwada pa mapazi a Elisa, naweramitsa mutu wake pansi. Kenaka ananyamula mwana wake natuluka.
38 Kalpasanna napan manen ni Eliseo iti Gilgal. Adda iti panagbisin iti daga, ket agtugtugaw dagiti annak dagiti profeta iti sangoananna. Kinunana iti adipenna, “Isaangmo ti dakkel a dungdong iti apuy ket manglutoka iti sidaen a para kadagiti annak dagiti profeta.”
Elisa anabwerera ku Giligala ndipo ku dera limenelo kunali njala. Elisa akukumana ndi ana a aneneri, anati kwa mtumiki wake, “Ika mʼphika waukulu pa moto ndipo uwaphikire chakudya anthu awa.”
39 Napan iti taltalon ti maysa kadakuada tapno agala kadagiti natnateng. Nakasarak isuna iti balang a lanut ket nangala iti balang a bunga nga umanay a maisab-ok ti kagayna. Ginalipda dagitoy ket inlaokda iti sidaen, ngem saanda nga ammo no ania a kita dagitoy.
Mmodzi mwa ana aneneriwo anapita kuthengo kukafuna ndiwo ndipo anakapeza mpesa wakuthengo. Iye anathyolako zipatso zake nadzaza nsalu yake. Atabwerera, anazidula zipatsozo naziyika mu mʼphika, ngakhale kuti panalibe amene ankazidziwa.
40 Isu nga indasarda ti sidaen a kanen dagiti lallaki. Saan a nagbayag, apaman a mangmanganda, nagpukkawda ket kinunada, “Tao ti Dios, adda iti makapatay iti dungdong!” Ket saandan a kayat a kanen daytoy.
Anawapakulira anthu chakudyacho, koma atayamba kudya, anthuwo anafuwula kuti, “Inu munthu wa Mulungu muli imfa mu mʼphikamu!” Ndipo sakanatha kudya chakudyacho.
41 Ngem kinuna ni Eliseo, “Mangiyegkayo iti bassit nga arina.” Inkabilna daytoy iti dungdong ket kinunana, “Idasaryo daytoy a para kadagiti tattao, tapno makapanganda.” Ket awanen a pulos iti makadangran a linaon ti banga.
Elisa anati, “Bweretsani ufa.” Iye anathira ufa mu mʼphikamo ndipo anati, “Perekani chakudyachi kwa anthu kuti adye.” Ndipo mu mʼphikamo munalibenso zoopsa.
42 Adda maysa a tao a naggapu iti Baal Salisa a napan iti tao ti Dios ken nangipan iti duapulo a tinapay a naaramid iti trigo nga adda iti sakona a kaburburas, ken kaburburas a bukbukel. Kinunana, “Itedmo daytoy kadagiti tattao tapno makapanganda.”
Munthu wina wochokera ku Baala-Salisa anabwera atamutengera munthu wa Mulungu malofu a barele makumi awiri opangidwa kuchokera ku zokolola zoyamba kucha, pamodzinso ndi ngala zatsopano za tirigu. Elisa anati kwa munthuyo, “Apatse anthu kuti adye.”
43 Kinuna ti adipenna,” Ania, idasarko kadi daytoy iti sangoanan ti sangagasut a lallaki?” Ngem kinuna ni Eliseo, “Itedmo daytoy kadagiti tattao, tapno makapanganda, ta ibagbaga ni Yahweh, 'Mangandanto ket addanto pay sumagmamano a mabati.'”
Mtumiki wake anafunsa kuti, “Kodi ndikachigawe motani chakudyachi kwa anthu 100?” Koma Elisa anamuwuzanso kuti, “Apatse anthu adye. Pakuti izi ndi zimene Yehova akunena kuti, ‘Iwo adzadya chakudyachi ndipo china chidzatsalako.’”
44 Isu nga indasar daytoy ti adipen iti sagoananda; nanganda ket adda pay dagiti nabati, kas ti sao nga inkari ni Yahweh.
Tsono iye anachipereka kwa anthuwo ndipo anadya china nʼkutsalako, molingana ndi mawu a Yehova.

< 2 Ar-ari 4 >