< 2 Cronicas 32 >

1 Kalpasan dagitoy a banbanag ken dagitoy a napudno nga aramid, immay ni Senakerib nga ari ti Asiria iti Juda; nagkampo isuna tapno rautenna dagiti nasarikedkedan a siudad, a ginandatna a sakupen tapno tagikuaenna.
Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
2 Idi nakita ni Hezekias nga immay ni Senakerib ket gandatna a rauten ti Jerusalem,
Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
3 inyumanna kadagiti opisialna ken kadagiti nabibileg a lallaki a serraanda dagiti pagayusan ti danum a rummuar iti siudad; tinulonganda isuna a nangaramid iti dayta.
iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
4 Adu ngarud a tattao ti naguummong ket sinerraanda dagiti amin a pagayusan ti danum ken dagiti waig nga agayus iti tengnga ti daga. Kinunada, “Ta apay koma nga umay dagiti ari ti Asiria ket agbirokda iti nabuslon a danum?”
Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
5 Timmured ni Hezekias ket tinarimaanna dagiti amin a narba a pader; nangipatakder isuna kadagiti pagwanawanan, ken kasta met kadagiti sabali pay a pader iti ruar. Pinalagdana met ti Milo iti siudad ni David, ken nagaramid isuna kadagiti adu nga igam ken kalasag.
Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
6 Nangdutok isuna kadagiti pangulo ti armada a mangidaulo kadagiti tattao. Inummongna amin ida iti plasa iti ruangan ti siudad ket nagsao iti pammabileg kadakuada. Kinunana,
Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
7 “bumileg ken tumuredkayo. Saankayo nga agbuteng wenno maupay gapu iti ari ti Asiria ken kadagiti amin a kakaduana nga armada, ta adda kaduatayo a napigpigsa ngem kadagiti kakaduana.
“Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
8 Ti laeng kaduana ket takiag a lasag, ngem ti kaduatayo ket ni Yahweh, a Diostayo, a mangtulong kadatayo, ken makiranget iti gubattayo.” Ket napatured dagiti tattao babaen kadagiti sasao ni Hezekias, nga ari ti Juda.
Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
9 Kalpasan daytoy, imbaon ni Senakerib nga ari ti Asiria idiay Jerusalem dagiti adipenna ( ita, adda isuna iti sango ti Lakis, ken kaduana dagiti amin nga armadana), a mapanda kenni Hezekias, nga ari ti Juda, ken kadagiti amin a tattao ti Juda nga adda idiay Jerusalem. Kinunana,
Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
10 “Kastoy ti kuna ni Senakerib nga ari ti Asiria: 'Ania aya ti pagtaltalkanyo tapno maibturanyo ti pannakalakub ti Jerusalem?
“Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
11 Saan kadi nga al-allilawennakayo laeng ni Hezekias, tapno iyawatnakayo iti pannakatay babaen iti panagbisin ken uwaw, tunggal ibagana, “Ispalennatayo ni Yahweh manipud iti ima ti ari ti Asiria”?
Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
12 Saan kadi a daytoy met laeng a Hezekias ti nangikkat kadagiti pagdaydayawan ken kadagiti altarna, ken binilinna ti Juda ken Jerusalem, “Maysa laeng nga altar ti pagdaydayawanyo, ken ditoy ti pangpuoranyo kadagiti datonyo?”
Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
13 Saanyo kadi nga ammo ti inaramidko ken dagiti kapuonak kadagiti amin a bunggoy dagiti tattao kadagiti dadduma a daga? Naispal aya dagiti didiosen dagiti tattao kadagiti daga dagiti dagada manipud iti pannakabalinko?
“Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
14 Kadagiti amin a didiosen dagidiay nasion a naan-anay a dinadael dagiti kapuonak, adda kadi didiosen a nakaispal kadagiti tattaona manipud kadagiti imak? Kasano koma a maispalnakayo ti Diosyo manipud iti pannakabalinko?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
15 Ita, saanyo nga itulok nga allilawennakayo ni Hezekias wenno allukoyennakayo iti kastoy a wagas. Saanyo a patpatien isuna, ta awan pay didiosen iti uray ania a nasion wenno pagarian ti nakaispal kadagiti tattaona manipud kadagiti imak, wenno manipud kadagiti ima dagiti kapuonak. Kasano pay ngarud a maispalnakayo ti Diosyo manipud kadagiti imak?’”
Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
16 Nagsao pay dagiti adipen ni Senakerib iti maibusor kenni Yahweh a Dios ken maibusor iti adipenna a ni Hezekias.
Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
17 Nagsurat pay ni Senakerib tapno laisenna ni Yahweh, a Dios ti Israel, ken tapno agsao iti maibusor kenkuana. Kinunana, “Kas iti saan a panangispal dagiti didiosen dagiti nasion iti daga kadagiti tattaoda manipud kadagiti imak, kasta met ngarud a saan a maispal ti Dios ni Hezekias dagiti tattaona manipud kadagiti imak.”
Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
18 Impukkawda iti pagsasao a Judio kadagiti tattao iti Jerusalem nga adda iti rabaw ti pader, tapno pagdanagen ken riribukenda ida, iti kasta ket masakupda ti siudad.
Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
19 Nagsaoda iti Dios ti Jerusalem a kas iti panagsaoda kadagiti didiosen dagiti dadduma a tattao iti daga, nga aramid laeng dagiti ima dagiti tattao.
Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
20 Nagkaragrag da Hezekias nga ari, ken ni profeta Isaias a putot a lalaki ni Amoz, gapu iti daytoy a banag ken immasugda iti langit.
Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
21 Nangibaon ni Yahweh iti anghel a nangpapatay kadagiti mannakiranget a lallaki, kadagiti papangulo ti armada, ken kadagiti opisiales ti ari iti kampo. Isu a nagawid ni Senakerib iti bukodna a daga a kasta unay ti bainna. Idi napan isuna iti balay ti didiosenna, pinatay isuna idiay dagiti sumagmamano kadagiti putotna babaen iti kampilan.
Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
22 Iti kastoy a wagas, insalakan ni Yahweh ni Hezekias ken dagiti agnanaed iti Jerusalem manipud iti ima ni Senakerib, nga ari ti Asiria, ken manipud iti ima dagiti dadduma, ken indalanna ida iti amin a wagas.
Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
23 Adu ti nangiyeg kadagiti sagut kenni Yahweh idiay Jerusalem ken kadagiti napapateg a banag kenni Hezekias, nga ari ti Juda, isu a mararaem isuna iti imatang dagiti amin a nasion manipud iti dayta a tiempo aginggana iti masakbayan.
Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
24 Kadagidi a tiempo, nagsakit ni Hezekias nga urayla dandanin a matay. Nagkararag isuna kenni Yahweh, a nagsao kenkuana ken nangted iti pagilasinan nga umimbag isuna.
Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
25 Ngem saan a sinubadan ni Hezekias ti panangtulong kenkuana ni Yahweh, gapu ta timmangsit isuna. Immay ngarud ti pungtot kenkuana, iti Juda ken Jerusalem.
Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
26 Nupay kasta, iti saan a nagbayag ket impakumbaba ni Hezekias ti natangsit a pusona, isuna ken dagiti agnanaed iti Jerusalem, isu a saan nga immay ti pungtot ni Yahweh kadakuada iti tiempo ni Hezekias.
Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
27 Addaan ni Hezekias iti adu a kinabaknang ken mararaem iti kasta unay. Nagpaaramid isuna kadagiti pagidulinan kadagiti pirak, balitok, agkakapateg a bato, bangbanglo, kasta met kadagiti kalasag ken kadagiti amin a kita dagiti napapateg nga alikamen.
Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
28 Addaan pay isuna kadagiti siled a pagidulinan kadagiti naapit a trigo, baro nga arak, ken lana; ken kadagiti koral a para iti amin a kita ti ayup; addaan met isuna iti arban ti ayup kadagiti kulonganda.
Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
29 Malaksid kadagitoy, nangipasdek isuna kadagiti siudad a para kadagiti adu unay nga arban ti karnero ken adu unay a dingwen, gapu ta pinabaknang unay isuna ti Dios.
Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
30 Ni Hezekias met laeng ti nangserra iti ubbog ti Gihon ken nangiturong kadagitoy iti daya a paset ti siudad ni David. Nagballigi ni Hezikias iti amin a proyektona.
Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
31 Nupay kasta, iti biang dagiti mangibagbagi kadagiti prinsepe iti Babilonia, nga imbaonda a mapan kenkuana tapno agsaludsod kadagiti makaammo maipanggep kadagiti nakaskasdaaw a pagilasinan a mapaspasamak iti dayta a daga, pinalubosan ti Dios nga aramiden ni Hezekias ti kaykayatna, tapno suotenna isuna, ken tapno ammoenna amin a linaon ti pusona.
Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
32 Kadagiti met dadduma a banag maipanggep kenni Hezekias, karaman ti panagtignayna iti napudno a katulagan, makitayo a naisurat dagitoy idiay Sirmata ni Profeta Isaias a putot a lalaki ni Amos, ken iti Libro dagiti Ar-ari ti Juda ken Israel.
Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
33 Pimmusay ni Hezekias ket intanemda isuna iti turod a pakaitantaneman dagiti kaputotan ni David. Iti pannakatayna, pinadayawan isuna ti entero a Juda ken dagiti agnanaed iti Jerusalem. Ni Manases a putotna a lalaki ti simmukat kenkuana nga ari.
Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Cronicas 32 >