< 2 Cronicas 29 >

1 Nangrugi nga agturay ni Hezekias a kas ari idi agtawen isuna iti 25; nagturay isuna iti 29 a tawen idiay Jerusalem. Abiha ti nagan ti inana; a putot a babai ni Zacarias.
Hezekiya anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 29. Dzina la amayi ake linali Abiya mwana wa Zekariya.
2 Inaramidna ti nalinteg iti imatang ni Yahweh ket sinurotna dagiti pagulidanan nga inaramid ni David a kapuonanna, iti amin a banag.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Davide abambo ake.
3 Iti umuna a tawen ti panagturayna, iti umuna a bulan, linukatan ni Hezekias dagiti ridaw ti balay ni Yahweh ket tinarimaanna dagitoy.
Pa chaka choyamba cha ulamuliro wake, iye anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova ndipo anazikonza.
4 Pinastrekna dagiti papadi ken dagiti Levita ket inummongna ida idiay paraangan iti akindaya a paset.
Iye analowetsamo ansembe ndi Alevi ndipo anawasonkhanitsa ku bwalo lakummawa
5 Kinunana kadakuada, “Dumngegkayo kaniak, dakayo a Levita! Ikonsagraryo dagiti bagiyo kenni Yahweh ket ikonsagraryo ti balay ni Yahweh a Dios dagiti kapuonanyo, ket ikkatenyo dagiti banbanag a mangtulaw iti nasantoan a disso.
ndipo anati: “Mverani, inu Alevi! Dziyeretseni tsopano ndiponso muyeretse Nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu. Muchotse zodetsa zonse ku malo opatulika.
6 Ta nagsalungasing dagiti kapuonantayo ket inaramidda ti dakes iti imatang ni Yahweh a Diostayo; linaksidda isuna, binaybay-anda ti lugar a pagnanaedan ni Yahweh ket tinallikudanda daytoy.
Makolo athu anali osakhulupirika ndipo anachita zoyipa pa maso pa Yehova Mulungu wathu ndi kumusiya Yehovayo. Iwo anatembenuka ndi kusiya malo okhalako Yehova ndi kumufulatira.
7 Inserrada pay dagiti ridaw ti balkon ken ineddepda dagiti pagsilawan; saanda a nagpuor iti insensio wenno kadagiti daton a naan-anay a maipuor idiay nasantoan a disso ti Dios ti Israel.
Iwowo anatsekanso zitseko zapakhonde ndi kuzimitsa nyale. Sanafukize lubani kapena kupereka nsembe zopsereza ku malo opatulika a Mulungu wa Israeli.
8 Ngarud, nagdissuor ti pungtot ni Yahweh iti Juda ken Jerusalem, ket inaramidna ida a maysa a banag nga um-umsien, pagbutbutngan, ken pakababainan, kas makitayo kadagiti bukodyo a mata.
Kotero, Yehova anakwiyira Yuda ndi Yerusalemu. Iye anawasandutsa chinthu chochititsa mantha, choopsa ndiponso chonyozedwa monga momwe mukuonera ndi maso anuwa lero lino.
9 Daytoy ti gapuna a natay dagiti ammatayo iti paggugubatan, ket naipanaw a kas balud dagiti annaktayo, ken dagiti assawatayo gapu iti daytoy.
Ichi nʼchifukwa chake makolo athu anaperekedwa ku lupanga ndipo nʼchifukwa chake ana athu aamuna ndi aakazi ndi akazi athu ali ku ukapolo.
10 Ita, adda iti pusok a makitulag kenni Yahweh a Dios ti Israel tapno bumaaw ti napalalo a pungtotna kadatayo.
Tsono ine ndikuganiza zochita pangano ndi Yehova Mulungu wa Israeli, kuti mkwiyo wake woopsawu utichokere.
11 Annakko, saankayo ita nga agtaktak ta pinilinakayo ni Yahweh a tumakder iti sangoananna, nga agdayaw kenkuana ken agbalin nga ad-adipenna ken agpuor iti insenso.”
Ana anga, musanyalanyaze tsopano, pakuti Yehova wakusankhani kuti muziyima pamaso pake ndi kumutumikira Iye, kugwira ntchito pamaso pake ndi kufukiza lubani.”
12 Rinugian dagiti Levita ti trabahoda; manipud kadagiti Kohatita ket da Mahat a putot a lalaki ni Amasai, ken Joel a putot a lalaki ni Azarias, ken manipud kadagiti tattao ti Merari ket da Kis a putot a lalaki ni Abdi ken ni Azarias a putot a lalaki ni Jehalelel; ken manipud kadagiti Gersonita ket da Joa a putot a lalaki ni Zimma ken Eden a putot a lalaki ni Joa;
Ndipo Alevi awa anakonzeka kugwira ntchito: Kuchokera ku banja la Kohati, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoweli mwana wa Azariya; kuchokera ku banja la Merari, Kisi mwana wa Abidi ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; kuchokera ku banja la Geresoni, Yowa mwana wa Zima ndi Edeni mwana wa Yowa;
13 manipud kadagiti putot a lalaki ni Elizafan ket da Simri ken Jeuel; ken manipud kadagiti putot a lalaki ni Asaf ket da Zacarias ken Mattanias;
kuchokera kwa zidzukulu za Elizafani, Simiri ndi Yeiyeli; kuchokera kwa zidzukulu za Asafu, Zekariya ndi Mataniya;
14 manipud kadagiti putot a lalaki ni Heman ket da Jehuel ken Simei; ken manipud kadagiti putot a lalaki ni Jedutun ket da Semaias ken Uzziel.
kuchokera kwa zidzukulu za Hemani, Yehieli ndi Simei; kuchokera kwa zidzukulu za Yedutuni, Semaya ndi Uzieli.
15 Inummongda dagiti kakabsatda, inkonsagrarda dagiti bagida kenni Yahweh sada simrek a kas imbilin ti ari ken kas panangtungpalda kadagiti sasao ni Yahweh a panangdalus iti balay ni Yahweh.
Atasonkhanitsa abale awo ndi kudziyeretsa, iwo anapita kukayeretsa Nyumba ya Yehova, monga inalamulira mfumu, potsatira mawu a Yehova.
16 Immuneg dagiti papadi iti kaunegan a paset ti balay ni Yahweh tapno dalusanda daytoy; inruarda amin a makarurod a nasarakanda iti uneg ti templo ni Yahweh iti paraangan ti balay. Inruar dagiti Levita daytoy ket impanda idiay waig ti Kidron.
Ansembe analowa ku malo opatulika a Yehova kukayeretsako. Anatulutsira ku bwalo la Nyumba ya Yehova chilichonse chodetsedwa chimene anachipeza mʼNyumba ya Yehova. Alevi anatenga zimenezo ndi kupita nazo ku chigwa cha Kidroni.
17 Ita, inrugida ti pannakaikonsagrar ti balay ni Yahweh iti umuna nga aldaw iti umuna a bulan ket iti maikawalo nga aldaw ti bulan nadanonda ti balkon ni Yahweh. Inkonsagrarda ti balay ni Yahweh iti walo nga aldaw. Iti maika-16 nga aldaw iti umuna a bulan ket nalpasda.
Iwo anayamba mwambo woyeretsawu tsiku loyamba la mwezi woyamba ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu la mweziwo anafika pa khonde la nyumba ya Yehova. Tsono anachita mwambo woyeretsa Nyumba ya Yehova ija masiku asanu ndi atatu, ndipo anamaliza pa tsiku la 16 mwezi woyamba.
18 Kalpasanna, napanda kenni Hezekias nga ari, iti uneg ti palasio ket kinunada, “Nadalusanmin ti entero a balay ni Yahweh, ti altar para iti daton a naan-anay a maipuor agraman ti amin nga alikamen daytoy, ken ti lamisaan a pakaikabilan ti nasagradoan a tinapay agraman ti amin nga alikamen daytoy.
Ndipo anapita kwa mfumu Hezekiya ndi kukafotokoza kuti, “Ife tayeretsa Nyumba ya Mulungu yonse, guwa lansembe zopsereza ndi ziwiya zake zonse, ndiponso tebulo limene timayikapo buledi wopatulika pamodzi ndi zinthu zake zonse.
19 Malaksid iti daytoy, insaganami ken indatagmi kenni Yahweh dagiti amin nga alikamen nga imbelleng ni Ari Ahaz idi nangsalungasing isuna bayat ti panagturayna. Adtoy, addada iti sangoanan ti altar ni Yahweh.”
Takonza ndi kuyeretsa zinthu zonse zimene mfumu Ahazi anazichotsa mwa kusakhulupirika kwake pamene anali mfumu. Taziyika kutsogolo kwa guwa la Yehova.”
20 Ket iti kinabigatanna, bimmangon a nasapa ni Hezekias nga ari ket inummongna dagiti mangidadaulo iti siudad; simmang-at isuna iti balay ni Yahweh.
Mmamawa tsiku linalo, mfumu Hezekiya inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu a mu mzindawo ndipo inapita ku Nyumba ya Yehova.
21 Nangiyegda iti pito a toro a baka, pito a karnero, pito nga urbon a karnero ken pito a kalakian a kalding a kas daton para iti pakapakawanan ti basol ti pagarian, ti Juda, ken iti santuario. Binilinna dagiti papadi a putot a lallaki ni Aaron nga idatonda dagitoy iti rabaw ti altar ni Yahweh.
Iwo anabweretsa ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ziwiri monga nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo la ufumu, la malo opatulika ndi Yuda. Tsono mfumu inalamula ansembe, zidzukulu za Aaroni, kuti apereke zimenezi pa guwa lansembe la Yehova.
22 Isu a pinartida dagiti toro a baka, ket inwarsi dagiti papadi ti dara dagitoy iti altar. Pinartida dagiti karnero ket inwarsida ti dara dagitoy iti altar; pinartida pay dagiti urbon a karnero ket inwarsida ti dara dagitoy iti altar.
Choncho anthuwo anapha ngʼombe zazimunazo ndipo ansembe anatenga magazi ake ndi kuwawaza pa guwa lansembe, kenaka anapha nkhosa zazimuna zija ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe; anaphanso ana ankhosa aja ndipo anawaza magazi ake pa guwa lansembe.
23 Impanda dagiti kalakian a kalding iti sangoanan ti ari ken iti gimong ket impatayda dagiti imada kadagitoy a kas daton a gapu iti basol.
Mbuzi zoperekedwa chifukwa cha tchimo zija zinabweretsedwa pamaso pa mfumu ndi anthu onse, ndipo anasanjika manja awo pa izo.
24 Pinarti dagiti papadi dagitoy ket imbukbokda dagiti dara iti altar a kas daton a pangikkat kadagiti amin a basol dagiti tattao ti Israel; ta imbilin ti ari a maidaton ti daton a maipuor ken dagiti daton gapu iti basol a maipaay iti entero nga Israel.
Kenaka ansembe anapha mbuzizo ndipo anapereka magazi ake pa guwa, kuti ukhale mwambo wofafanizira machimo a Aisraeli onse, pakuti mfumu inalamula kuti nsembe yopsereza ndi yopepesera machimo zichitike chifukwa cha Aisraeli onse.
25 Impuesto ni Hezekias dagiti Levita iti balay ni Yahweh nga agtokar kadagiti piangpiang, kadagiti arpa ken kadagiti lira, impuestona ida segun iti bilin da David, Gad a mammadto ti ari, ken Natan a profeta; ta ti bilin ket nagtaud kenni Yahweh babaen kadagiti profetana.
Iye anayika Alevi mʼNyumba ya Yehova ali ndi ziwaya za malipenga, azeze ndi apangwe potsata lamulo la Davide, Gadi mlosi wa mfumu ndi mneneri Natani. Pakuti Yehova ndiye analamula zimenezi kudzera mwa aneneri.
26 Timmakder dagiti Levita nga iggemda dagiti instrumento ni David, ken dagiti papadi a siiigem kadagiti trumpeta.
Kotero Alevi anayima okonzekera atanyamula zoyimbira za Davide ndiponso ansembe atanyamula malipenga awo.
27 Binilin ida ni Hezekias nga idatonda ti daton a maipuor iti rabaw ti altar. Idi mangrugi ti panagidaton iti daton a maipuor, nagkanta metten dagiti tattao iti pagdaydayaw kenni Yahweh a nadanggayan kadagiti trumpeta agraman kadagiti instrumento ni David nga ari ti Israel.
Hezekiya analamulira kuti apereke nsembe zopsereza pa guwa. Pamene amayamba kupereka nsembezo, kuyimbira Yehova kunayambikanso, pamodzi ndi malipenga ndi zipangizo zoyimbira za Davide mfumu ya Israeli.
28 Nagdaydayaw ti amin a taripnong, ket nagtuloy ti panagkanta dagiti kumakanta, ken panagtukar dagiti trumutrumpeta; nagtultuloy amin dagitoy agingga a nalpas ti pannakaidaton ti daton a maipuor.
Anthu onse anawerama pansi ndi kulambira, pamene oyimba amayimba ndi malipenga. Izi zonse zinapitirira mpaka pa mapeto pa nsembe zopsereza.
29 Idi nalpas ti panagidatonda, nagparintumeng ket nagdaydayaw ti ari ken amin nga adda sadiay.
Zopereka zitatha, mfumu ndi wina aliyense amene anali naye anagwada pansi ndi kulambira.
30 Maysa pay, imbaga ni Hezekias nga ari ken dagiti mangidadaulo nga agkanta dagiti Levita iti pagdaydayaw kenni Yahweh nga insurat ni David ken ni Asaf a mammadto. Sirarag-o a nagkantada kadagiti pagdaydayaw, ket nagparintumeng ken nagdaydayawda iti Dios.
Mfumu Hezekiya ndi akuluakulu ake analamulira Alevi kuti atamande Yehova potsata mawu a Davide ndi mlosi Asafu. Kotero anayimba nyimbo zamatamando mokondwera ndipo anaweramitsa mitu yawo ndi kulambira.
31 Ket kinuna ni Hezekias, “Ita ta naikonsagraryon dagiti bagiyo kenni Yahweh. Umaykayo ditoy ket mangitugotkayo kadagiti daton ken kadagiti sagutyo a pagyaman kenni Yahweh.” Nangiyeg ti taripnong kadagiti datdaton ken sagsagut a pagyaman; amin a nagboluntario ket nangiyegda kadagiti daton a maipuor.
Kenaka Hezekiya anati, “Inu mwadzipereka tsopano kwa Yehova. Bwerani ndipo mufike ndi nsembe ndi zopereka zachiyamiko ku Nyumba ya Yehova.” Choncho anthu onse anabweretsa nsembe ndi zopereka zachiyamiko, ndipo anthu onse amene anali ofuna mu mtima mwawo anabweretsa nsembe zopsereza.
32 Ti bilang dagiti daton a maipuor nga inyeg ti taripnong ket 70 a toro a baka, 100 a karnero ken 200 nga urbon a karnero. Amin dagitoy ket maipuor a daton kenni Yahweh.
Chiwerengero cha nsembe zopsereza chimene anthu onse anabweretsa chinali ngʼombe zazimuna makumi asanu ndi awiri, nkhosa zazimuna 100, ana ankhosa aamuna 200 ndipo zonsezi zinali za nsembe yopsereza kwa Yehova.
33 Dagiti ayup a naidatag kenni Yahweh ket 600 a baka ken 3, 000 a karnero.
Ziweto zimene zinapatulidwa kukhala nsembe zinalipo ngʼombe zazimuna 600, nkhosa ndi mbuzi 3,000.
34 Ngem sumagmamano laeng dagiti papadi a manglalat kadagiti amin daton a maipuor, isu a tinulongan ida dagiti kakabsatda a Levita agingga a nalpas ti trabaho, ken agingga a naikonsagrar dagiti papadi ti bagida kenni Yahweh; ta ad-adda ti panangikalikagum dagiti Levita iti pannakakonsagrarda ngem kadagiti papadi.
Koma ansembe anali ochepa kuti asende zonse zopsereza. Choncho abale awo Alevi anawathandiza mpaka ntchito yonse inatha ndipo mpaka ansembe ena atadziyeretsa, pakuti Alevi anachita changu kudziyeretsa kulekana ndi momwe anachitira ansembe.
35 Malaksid iti nakaad-adu unay a daton a maipuor, naidaton dagitoy a napakuyogan iti taba dagiti sagut a pakikappia, ken adda sagut nga arak iti tunggal daton a maipuor. Isu a ti panagdaydayaw iti balay ni Yahweh ket nairugi manen.
Panali nsembe zopsereza zochuluka, pamodzi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano ndi nsembe yachakumwa imene imachitika pamodzi ndi nsembe yopsereza. Kotero ntchito ya mʼNyumba ya Mulungu inakhazikitsidwanso.
36 Naragsakan ni Hezekias, ken dagiti amin a tattao gapu iti insagana ti Dios para kadagiti tattao; ta apagbiit a nalpas ti trabaho.
Hezekiya ndi anthu onse anakondwera pa zimene Mulungu anachitira anthu ake, chifukwa zinachita mwamsangamsanga.

< 2 Cronicas 29 >