< 2 Cronicas 26 >
1 Innala dagiti tattao ti Juda ni Uzzias nga agtawen iti 16 ket insaadda isuna nga ari a kas kasukat ti amana a ni Amazias.
Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
2 Isuna ti nangibangon manen iti Elat ket insublina daytoy iti Juda. Kalpasan dayta, pimmusay ti ari.
Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
3 Agtawen ni Uzzias iti 16 idi nangrugi nga agturay. Nagturay isuna iti 52 a tawen idiay Jerusalem. Jecolia ti nagan ti inana a taga-Jerusalem.
Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
4 Inaramidna ti umno iti imatang ni Yahweh, sinurotna dagiti pagulidan ti amana a ni Amazias, iti amin nga inaramidna.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
5 Napasnek isuna nga agtulnog iti Dios kadagidi aldaw ni Zacarias a mamalbalakad kenkuana maipapan iti panagtulnog iti Dios. Kabayatan iti tiempo a nagtulnog isuna kenni Yahweh, pinarang-ay isuna ti Dios.
Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
6 Napan ginubat ni Uzzias dagiti Filisteo. Rinebbana dagiti pader iti siudad ti Gat, Jamnia ken Asdod; nangbangon isuna kadagiti siudad iti pagilian ti Asdod ken kadagiti dadduma a lugar idiay Filistia.
Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
7 Tinulongan ti Dios iti pannakigubatna kadagiti Filisteo, kadagiti Arabo nga agnanaed iti Gurbaal ken kadagiti Meunita.
Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
8 Nagbuis dagiti Ammonita kenni Uzzias, ket nagdinnamag ti kinalatakna kadagiti dadduma a daga, uray pay iti pagserkan ti Egipto ta bimmileg isuna iti kasta unay.
Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
9 Malaksid iti daytoy, nangipatakder ni Uzzias kadagiti torre idiay Jerusalem iti Ruangan ti Suli, iti Ruangan ti Tanap, ken iti pagsikkoan ti bakud, ket pinatibkerna dagitoy.
Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
10 Nangipatakder pay isuna kadagiti torre a pagwanawanan iti let-ang ken nagkali iti adu a bubon ta adu ti ayupna kadagiti tanap ken kadagiti kapatadan. Addaan isuna kadagiti mannalon ken agay-aywan kadagiti ubas iti katurturodan a pagilian ken kadagiti nadam-eg a taltalon, ta pagay-ayatna ti panagtalon.
Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
11 Malaksid iti daytoy, addaan ni Uzzias iti armada a mannakigubat a sisasagana a makigubat, a nabingbingay babaen kadagiti bilangda a binilang da Jeiel nga eskriba, ken Maaseyas nga opisial iti babaen ti turay ni Hananias a maysa kadagiti mangidadaulo iti armada ti ari.
Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
12 Agdagup iti 2, 600 dagiti panguloen dagiti kapuonanda, a mannakigubat a lallaki.
Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
13 Adda 307, 500 a lallaki iti babaen ti panangidauloda a nalaing a makigubat, tapno tumulong iti ari a makiranget iti kabusor.
Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
14 Ni Uzzias ti nangted kadagiti masapsapul ti armada- kalasag, gayang, helmet, kabal, bai ken pana, ken kadagiti bato a pagpallatibong.
Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
15 Idiay Jerusalem, ket nangaramid isuna kadagiti makina, nga inembento dagiti nalalaing a lallaki tapno maikabil kadagiti torre ken kadagiti igid ti pader, nga isu ti pangitamaanda kadagiti bai ken dadakkel a batbato. Nagdinnamag ti kinalatakna agingga kadagiti adayo a dagdaga gapu ta tinulongan ti Dios iti kasta unay agingga a bimmileg isuna iti kasta unay.
Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
16 Ngem idi nagbalin a nabileg ni Uzzias, timmangsit isuna isu a nagtignay a sidadangkes; binusorna ni Yahweh a Diosna, ta simrek isuna iti balay ni Yahweh tapno agpuor iti insenso iti altar ti insenso.
Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
17 Sinaruno isuna ni Azarias a padi a kaduana ti walopulo a natutured a papadi ni Yahweh.
Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
18 Nilappedanda ni Uzzias nga ari ket kinunada kenkuana, “Saanmo a biang, ari Uzzias ti agpuor iti insenso kenni Yahweh ngem dagiti laeng papadi a putot a lallaki ni Aaron ti naikonsagrar kenni Yahweh tapno agpuor iti insenso ti makinbiang iti daytoy. Rummuarka iti nasantoan a disso ta nagsalungasingka. Saannakanto a padayawan ni Yahweh a Dios gapu iti daytoy.”
Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
19 Ket nakaunget ni Uzzias. Siiigem iti insensario tapno agpuor iti insenso. Nakapungtot isuna kadagiti papadi, ket dagus nga adda nagbettak a ketong iti mugingna iti sangoanan dagiti papadi iti uneg ti balay ni Yahweh, iti abay ti altar ti insenso.
Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
20 Kimmita kenkuana ni Azarias a kangatoan a padi ken dagiti amin a papadi ket naimatanganda ti ketong iti mugingna. Dagdagus nga impanawda isuna sadiay. Kinapudnona, nagdardaras a rimmuar isuna gapu ta dinusa ni Yahweh.
Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
21 Agketong ni Uzzias nga ari agingga iti aldaw ti ipapatayna, ken nagnaed iti naisina a balay, agsipud ta agketong isuna; gapu ta saan isuna a mapalubosan a mapan iti templo ni Yahweh. Ni Jotam a putotna a lalaki ti nangimaton iti palasio ken nangituray kadagiti tattao iti daga.
Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
22 Maipapan kadagiti dadduma a banbanag maipanggep kenni Uzzias, manipud rugi agingga iti maudi, ket nailanad iti insurat ni profeta Isaias a putot a lalaki ni Amos.
Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
23 Pimmusay ngarud ni Uzzias; intanemda isuna iti nakaitaneman dagiti kapuonanna iti pakaitantaneman a kukua dagiti Ar-ari, ta kinunada, “Maysa isuna nga agketong.” Ni Jotam a putotna a lalaki ti naisaad nga ari a kasukatna.
Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.