< 2 Cronicas 20 >

1 Kalpasan daytoy, immay a makigubat kenni Jehosafat dagiti tattao ti Moab ken Ammon agraman dagiti kakaduada a Meunita.
Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
2 Ket adda sumagmamano a nangipadamag kenni Jehosafat, a kunada, “Adda dakkel a bunggoy nga um-umay manipud iti ballasiw ti Natay a Baybay, manipud Aram tapno umaydaka rauten. Adtoy, addadan idiay Hazazontamar” (dayta ket, Engedi).
Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
3 Nagbuteng ni Jehosafat ket sipapasnek a binirokna ni Yahweh. Imbilinna ti panagayunar iti entero a Juda.
Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
4 Naguummong ti Juda tapno dawatenda ti pammagbaga ni Yahweh; immayda manipud kadagiti amin a siudad ti Juda tapno dawatenda ti pammagbaga ni Yahweh.
Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
5 Timmakder ni Jehosafat iti taripnong ti Juda ken Jerusalem, iti balay ni Yahweh, iti sangoanan ti baro a paraangan.
Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
6 Kinunana, “O Yahweh a Dios dagiti kapuonanmi, saan kadi a sika ti Dios ti langit? Ken saan kadi a sika ti mangiturturay kadagiti amin a pagarian kadagiti nasion? Adda kadagita imam ti bileg ken pannakabalin, isu nga awan ti siasinoman a makabael a bumusor kenka.
ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
7 O Diosmi, saan kadi a pinapanawmo dagiti agnanaed iti daytoy a daga iti sangoanan dagiti tattaom nga Israel, ket intedmo daytoy kadagiti kaputotan ni Abraham iti agnanayon?
Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
8 Nagnaedda iti daytoy ket nangipatakderda iti nasantoan a lugar para iti naganmo, a kunada,
Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
9 'No adda didigra nga umay kadakami-ti gubat, wenno sakit, wenno bisin-tumakderkami iti sangoanan daytoy a balay, ken iti sangoanam (ta ti naganmo ket adda iti daytoy a balay), ket umasogkami kenka iti panagrigatmi, ket denggennakami ket isalakannakami.'
‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
10 Kitaem ita, adda ditoy dagiti tattao ti Ammon, Moab, ken Bantay Seir, a saanmo nga impalubos a sakupen ti Israel, idi rimmuarda iti daga ti Egipto; ngem ketdi, naglikaw ti Israel ket saanda ida a dinadael.
“Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
11 Kitaem no kasano ti panangsupapakda kadakami; um-umayda a mangpapanaw kadakami iti dagam nga intedmo kadakami a tawidenmi.
Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
12 O Diosmi, saanmo kadi nga ukomen ida? Ta awan bilegmi a mangsaranget iti daytoy a nakadakdakkel nga armada nga um-umay a mangraut kadakami.” Saanmi nga ammo ti aramidenmi, ngem dumawdawatkami iti tulongmo.”
Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
13 Nagtakder ti amin a Juda iti sangoanan ni Yahweh, a kadduada dagiti ubbingda, assawada, ken annakda.
Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
14 Ket iti tengnga ti taripnong, immay ti Espiritu ni Yahweh kenni Jahaziel a putot a lalaki ni Zacarias a putot a lalaki ni Benaias a putot a lalaki ni Jeiel a putot a lalaki ni Matanaias a Levita, maysa kadagiti putot a lalaki ni Asap.
Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
15 Kinuna ni Jahaziel, “Dumngegkayo, amin a Juda ken dakayo nga agnanaed iti Jerusalem, ken Ari a Jehosafat: “Kastoy ti kuna ni Yahweh kadakayo: 'Saankayo nga agbuteng; saankayo a maupay gapu iti daytoy a dakkel nga armada. Ta ti gubat ket saan a para kadakayo, ngem iti Dios.
Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
16 Sumalogkayo a mangsaranget kadakuada inton bigat. Kitaenyo, sumangsang-atda idiay bessang ti Ziz. Masarakanyo ida iti pungto ti tanap, sakbay iti let-ang ti Jeruel.
Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
17 Saanen a masapul a makirangetkayo iti daytoy a gubat. Agtalinaedkayo iti puestoyo, aguraykayo, ket kitaenyo ti panangispal ni Yahweh kadakayo, Juda ken Jerusalem. Saankayo nga agbuteng wenno maupay. Inkay makigubat kadakuada inton bigat, ta adda ni Yahweh kadakayo.”
Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
18 Nagrukob ni Jehosafat iti daga. Nagrukob iti sangoanan ni Yahweh ti amin a Juda ken dagiti agnanaed iti Jerusalem, ket nagdaydayawda kenkuana.
Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
19 Timmakder dagiti Levita a kaputotan dagiti Koatitas ken Koreitas ket nagdaydayawda kenni Yahweh a Dios ti Israel iti nakapigpigsa a timek.
Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
20 Bimmangonda a nasapa iti kabigatanna ket napanda iti let-ang ti Tekoa. Bayat a rumrummuarda, timmakder ni Jehosafat ket kinunana, “Dumngegkayo kaniak, Juda, ken dakayo nga agnanaed iti Jerusalem! Agtalekkayo kenni Yahweh a Diosyo, ket saranayennakayonto. Agtalekkayo kadagiti profetana, ket agballigikayonto.”
Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
21 Idi nakiuman isuna kadagiti tattao, dinutokanna dagiti agkanta kadagiti panangidaydayaw kenni Yahweh gapu iti nasantoan a dayagna, bayat a magmagnada iti sangoanan ti armada, kankantaenda, “Agyamankami kenni Yahweh; ta agnanayon ti kinapudnona iti tulagna.”
Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
22 Idi rugianda ti agkanta ken agdayaw, pinagririnnanget ni Yahweh dagiti tattao ti Ammon, Moab ken Bantay Seir, nga um-umay a mangraut iti Juda. Naparmekda.
Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
23 Ta dagiti tattao ti Ammon ken Moab ket nakiranget kadagiti agnanaed iti Bantay Seir, tapno naan-anay a mapapatay ken madadaelda ida. Idi naparmekda dagiti tattao ti Bantay Seir, isudan ti nagraranget.
Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
24 Idi nakadanon ti Juda iti lugar a matannawaganda ti let-ang, nakitada dagiti armada. Adtoy, nataydan, napasagda iti daga; awan iti nakalasat.
Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
25 Idi napan ni Jehosafat ken dagiti tattao tapno agsamsamda, nakasarakda kadagiti nakaad-adu a kinabaknang ken napapateg nga alahas, a sinamsamda para kadagiti bagbagida, ad-adu dagitoy ngem iti kabaelanda nga awiten. Tallo nga aldaw a binunagda dagiti samsam, nakaad-adu unay dagitoy.
Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
26 Iti maika-uppat nga aldaw, naguummongda iti tanap ti Beraca. Indaydayawda sadiay ni Yahweh, isu a ti nagan dayta a lugar ket ti “tanap ti Beraca” agingga kadagitoy nga aldaw.
Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
27 Kalpasanna ket indauloan ida ni Jehosafat nga agsubli idiay Jerusalem nga addaan rag-o; ta pinagrag-o ida ni Yahweh kadagiti kabusorda.
Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
28 Simmangpetda idiay Jerusalem ket napanda iti balay ni Yahweh a nabuyogan iti uni dagiti lira, arpa ken trumpeta.
Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
29 Nagbuteng iti Dios dagiti amin a pagarian kadagiti nasion idi nadamagda a nakiranget ni Yahweh kadagiti kabusor ti Israel.
Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
30 Natalna ngarud ti pagarian ni Jehosafat, ta inikkan ti Diosna isuna iti kappia iti aglawlawna.
Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
31 Nagturay ni Jehosafat iti entero a Juda: agtawen isuna iti 35 idi nangrugi nga agturay, ket nagturay isuna idiay Jerusalem iti 25 a tawen. Azuba ti nagan ti inana, a putot a babai ni Silhi.
Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
32 Sinurotna dagiti wagas ni Asa nga amana; saanna a tinallikudan dagitoy; inaramidna ti ummo iti imatang ni Yahweh.
Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
33 Nupay kasta, saan pay a naikkat dagiti lugar a pagdaydayawan, saan pay met a pimmasnek dagiti tattao iti panagdaydayawda iti Dios dagiti kapuonanda.
Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
34 Dagiti dadduma a banbanag maipanggep kenni Jehosafat, manipud iti rugi agingga iti maudi, ket naisurat iti pakasaritaan ni Jehu a putot a lalaki ni Hanani, a nailanad iti Libro dagiti Ar-ari ti Israel.
Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
35 Kalpasan daytoy, nakitulag ni Jehosafat nga ari ti Juda kenni Ahazias nga ari ti Israel, nga adu a kinadakes ti inaramidna.
Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
36 Nakitulag isuna kenkuana nga agaramidda kadagiti barko nga aglayag iti taaw. Inaramidda dagiti barko idiay Eziongeber.
Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
37 Ket nangipadto ni Eliezer a putot a lalaki ni Dodavahu a taga-Maresias, iti maibusor kenni Jehosafat; kinunana, “Gapu ta nakitulagka kenni Ahazias, dinadael ni Yahweh dagiti inaramidyo.” Nadadael dagiti barko tapno saanda a makapaglayag.
Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.

< 2 Cronicas 20 >