< I Samuel 1 >

1 Adda maysa a lalaki iti Rama Zofim, iti katurturodan a pagilian ti Efraim; ti naganna ket Elkana a putot ni Jehoram, ni Jehoram ket putot ni Eliu, ni Eliu ket putot ni Tuho, ni Tuho ket putot ni Zup, ni Elkana ket maysa nga Efraimita.
Panali munthu wina wochokera ku Ramataimu, Mzofimu wa ku dziko la mapiri la Efereimu. Iyeyu dzina lake anali Elikana ndipo anali mwana wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu wa fuko la Efereimu.
2 Addaan isuna iti dua nga asawa, Ana ti nagan ti umuna, ken Fenina ti nagan ti maikadua. Adda annak ni Fenina, ngem awan ti anak ni Ana.
Iye anali ndi akazi awiri, Hana ndi Penina. Penina anali ndi ana, koma Hana analibe.
3 Tinawen a mapan daytoy a lalaki idiay Silo a siudadna tapno agdayaw ken agidaton kenni Yahweh a mannakabalin amin. Adda sadiay dagiti dua a lallaki a putot ni Eli, da Ofni ken Finees, a papadi ni Yahweh.
Chaka ndi chaka Elikana ankachoka ku mudzi kwawo kupita ku Silo kukapembedza ndi kukapereka nsembe kwa Yehova Wamphamvuzonse. Ku Siloko kunali ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi amene anali ansembe a Yehova.
4 No kasta a dumteng ti aldaw iti tunggal tawen a panagidaton ni Elkana, kankanayon nga it-itedna kenni Fenina nga asawana ken kadagiti amin nga annakna a lallaki ken babbai dagiti paset ti karne.
Tsiku lopereka nsembe likafika Elikana amapereka magawo a nsembeyo kwa mkazi wake Penina ndi kwa ana ake onse aamuna ndi aakazi.
5 Ngem kenni Ana, kankanayon a mamidua ti kaadu ti it-itedna, ta ay-ayatenna ni Ana, uray no sinerraan ni Yahweh ti aanakanna.
Ngakhale ankamukonda Hana, koma ankamupatsa gawo limodzi popeza Yehova sanamupatse ana.
6 Nakaro ti panangumsi kenkuana ti kasalisalna tapno pagpulkokenna isuna, gapu ta inserra ni Yahweh ti aanakanna.
Tsono popeza Yehova sanamupatse Hana ana, mkazi mnzakeyo ankamuyamba dala ndi cholinga chomukwiyitsa.
7 Isu nga iti tinawen, no kasta a mapan isuna iti balay ni Yahweh a kaduana ti pamiliana, kankanayon a karkariten isuna ni Fenina. Masansan ngarud nga agsangit isuna ken saan a mangmangan.
Izi zimachitika chaka ndi chaka. Hana ankati akamapita ku Nyumba ya Yehova mkazi mnzakeyo ankamunyogodola. Choncho Hana ankangokhalira kulira osafuna ndi kudya komwe.
8 Kankanayon nga ibagbaga kenkuana ni Elkana nga asawana, “Ana, apay nga agsangitka? Apay a saanka a mangan? Apay nga agliddaang ti pusom? Saan kadi a nasaysayaatak kenka ngem kadagiti sangapulo nga annak?
Tsono mwamuna wake Elikana ankamufunsa kuti, “Hana ukulira chifukwa chiyani? Wakhumudwa ndi chiyani kuti sukufuna ndi kudya komwe? Kodi ine kwa iwe sindili woposa ana aamuna khumi?”
9 Iti maysa kadagitoy a padaya, timmakder ni Ana kalpasan ti pannangan ken panag-iinomda idiay Silo. Ita, nakatugaw ni Eli a padi iti tugawna iti igid ti pagserkan ti balay ni Yahweh.
Tsiku lina atatha kudya ndi kumwa ku Silo kuja, Hana anayimirira kukapemphera. Nthawiyi nʼkuti wansembe Eli atakhala pa mpando pa khomo la Nyumba ya Yehova.
10 Mariribukan unay ni Ana; nagkararag isuna kenni Yahweh ken nagsangit iti nasaem.
Hana anavutika mʼmoyo mwake, ndipo anapemphera kwa Yehova akulira kwambiri.
11 Nagsapata isuna ket kinunana, “Yahweh a mannakabalin amin, no makitam la koma ti panagrigat ti adipenmo ken lagipennak, ken saanmo a lipaten ti adipenmo, ngem ipaayam ketdi koma ti adipenmo iti anak a lalaki, ngarud, itedkonto isuna kenni Yahweh iti unos ti panagbiagna, ket awanto ti kartib a mangsagid iti ulona.
Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
12 Bayat nga agkarkararag isuna iti sangoanan ni Yahweh, sipsiputan ni Eli ti ngiwatna.
Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa.
13 Naimpusoan ti panagkararag ni Ana. Agkutkuti dagiti bibigna, ngem saan a mangngeg ti timekna. Impagarup ngarud ni Eli a nabartek isuna.
Hana ankapemphera chamumtima ndipo milomo yake inkangogwedera koma mawu ake samamveka. Choncho Eli anaganiza kuti anali ataledzera.
14 Kinuna ni Eli kenkuana, “Kasano pay kapaut ti panagbarbartekmo? Isardengmon ti panagin-inommo.”
Ndipo anamufunsa Hana kuti, “Kodi mukhala chiledzerere mpaka liti? Pitani, ayambe wakuchokani vinyo mwamwayo.”
15 Simmungbat ni Ana, “Saan, apok, maysaak a babai a naladingit unay ti espirituna. Saanak nga imminom iti arak wenno naingel a mainom, ngem ibagbagak iti sangoanan ni Yahweh dagiti nakaro a panagladingitko.”
Koma Hana anayankha kuti, “Sichoncho mbuye wanga. Ndakhala ndikumukhuthulira Yehova chisoni changa. Sindinamwe vinyo kapena chakumwa choledzeretsa chilichonse, popeza nthawi yonseyi ndakhala ndikupereka kwa Yehova nkhawa yayikulu ndi mavuto anga.
16 “Saanmo nga ibilang nga awan babainna a babai ti adipenmo; iyeb-ebkasko iti napalalo a pannakaibabain ken pannakarkaritko.”
Musaganize kuti mtumiki wanu ndi kukhala mkazi wachabechabe. Ine ndakhala ndi kupereka nkhawa yanga yayikulu ndi zowawa zanga.”
17 Ket simmungbat ni Eli, kinunana, “Mapanka a sitatalna; patgan koma ti Dios ti Israel ti kiniddawmo kenkuana.”
Eli anayankha, “Pitani mu mtendere, ndipo Mulungu wa Israeli akupatseni zimene mwamupemphazo.”
18 Kinuna ni Ana, “Nasayaat koma ti panangipapanmo iti adipenmo.” Ket pimmanaw ti babai ket nangan; saanen a naliday ti rupana.
Hana anati, “Mundikomerebe mtima mtumiki wanune.” Kenaka anachoka nakadya, ndipo sanaonekenso wachisoni.
19 Nasapada a bimmangon iti bigat ket nagdayawda kenni Yahweh, ket kalpasanna, nagsublida manen iti balayda idiay Rama. Kinaidda ni Elkana ni Ana nga asawana, ket nalagip isuna ni Yahweh.
Elikana ndi banja lake anadzuka mmawa mwake nakapemphera pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anabwerera kwawo ku Rama. Elikana anakhala pamodzi ndi mkazi wake, ndipo Yehova anamukumbuka Hanayo.
20 Idi dimteng ti tiempo, nagsikog ni Ana ket nagpasngay iti maysa a lalaki. Pinanagananna iti Samuel, kunana “Gapu ta dinawatko isuna kenni Yahweh.”
Motero Hana anakhala ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Samueli, popeza anati, “Ndinachita kumupempha kwa Yehova.”
21 Iti naminsan pay, simmang-at ni Elkana ken ti amin a pamiliana, tapno mangidatag iti tinawen a daton ken tapno tungpalenna ti sapatana.
Elikana ndi banja lake lonse anapita kukapereka nsembe ya pa chaka kwa Yehova ndi kukakwaniritsa malonjezo ake.
22 Ngem saan a napan ni Ana; kinunana iti asawana, “Saanak a mapan agingga a mapusot ti ubing, ket iyegkonto isuna, tapno agparang isuna iti sangoanan ni Yahweh ken agnaed sadiay iti agnanayon.”
Koma Hana sanapite nawo popeza anawuza mwamuna wake kuti, “Mwanayu akadzaleka kuyamwa, ndidzapita naye ndi kukamupereka pamaso pa Yehova ndipo adzakhala kumeneko moyo wake wonse.”
23 Kinuna ni Elkana nga asawana kenkuana, “Aramidem ti ammon a nasayaat kenka. Urayem agingga a mapusotmo isuna; patalgedan koma ngarud ni Yahweh ti saona.” Nagbati ngarud ti babai ken inaywananna ti anakna agingga a naipusotna isuna.
Elikana mwamuna wake anamuwuza kuti, “Chita chimene chakukomera. Tsala kuno mpaka utamusiyitsa kuyamwa, Yehova yekha akwaniritse mawu ake.” Choncho mkaziyo anatsala ku nyumba ndi kusamalira mwana wake mpaka atamuletsa kuyamwa.
24 Idi naipusot ni Ana ti anakna, inkuyogna isuna, nangitugot pay iti maysa a kalakian a baka a tallo ti tawenna, maysa nga efa a taraon, ken maysa a pagkargaan a lalat a naglaon iti arak, ket impanna isuna iti balay ni Yahweh idiay Silo. Ita, ubing pay ti anakna.
Atamuletsa kuyamwa, Hana anatenga mwanayo ali wachichepere, ndikupita naye ku nyumba ya Yehova ku Silo. Anatenga ngʼombe yamphongo ya zaka zitatu, ufa wa makilogalamu khumi, ndi thumba lachikopa la vinyo.
25 Pinartida ti kalakian a baka, ket impanda ti ubing kenni Eli.
Tsono anapha ngʼombe yamphongo ija ndi kupereka mwana uja kwa Eli.
26 Kinuna ni Ana, “O, apok! Agingga a sibibiagka, apok, siak ti babai a nagtakder idi iti abaymo nga agkarkararag kenni Yahweh.
Ndipo Hana anati kwa Eli, “Mbuye wanga, ine ndikunenetsadi pamaso panu kuti ndine mkazi uja amene anayima pamaso panu ndi kumapemphera kwa Yehova.
27 Ta daytoy nga ubing ket inkararagko ket inted ni Yahweh ti dinawatko kenkuana.
Ndinapempha mwana uyu, ndipo Yehova wandipatsa chimene ndinamupempha.
28 Intedkon isuna kenni Yahweh; agingga a sibibiag isuna ket agpaayto kenni Yahweh.” Ket sadiay, nagdayaw kenni Yahweh ni Elkana ken ti pamiliana.
Ndiye tsopano ine ndikumupereka kwa Yehova. Pa moyo wake wonse adzakhala wa Yehova.” Ndipo onse anapembedza Yehova kumeneko.

< I Samuel 1 >