< I Samuel 28 >

1 Ket napasamak kadagidiay nga aldaw nga inummong dagiti Filisteo dagiti armadada para iti gubat tapno makirangetda iti Israel. Kinuna ni Akis kenni David, “Ipasiguradom a makikuyogka iti armadak a mapan rumaut, sika ken dagiti tattaom.”
Mʼmasiku amenewo Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo kuti akamenyane ndi Aisraeli. Akisi anawuza Davide kuti, “Udziwe kuti iwe pamodzi ndi anthu ako mudzapita nane ku nkhondo.”
2 Kinuna ni David kenni Akis, “Maammoamto ngarud no ania ti kabaelan nga aramiden ti adipenmo.” Kinuna ni Akis kenni David, “Isu a sikanto ti mangsalaknib kaniak agingga a sibibiagak.”
Davide anayankha kuti, “Tsono inu mudzaona zimene mtumiki wanune ndingachite.” Akisi anayankha kuti, “Chabwino ine ndidzakuyika iwe kukhala mlonda wanga moyo wako wonse.”
3 Ita, natayen ni Samuel; nagladingit ti entero nga Israel ket intabonda isuna idiay Rama, iti bukodna nga ili. Ita, imparit ni Saul iti daga ti pannakiuman kadagiti natay wenno kadagiti espiritu.
Nthawi imeneyi nʼkuti Samueli atamwalira, ndipo Aisraeli onse anamulira namuyika mʼmanda ku mzinda wake wa Rama. Sauli anali atachotsa mʼdzikomo anthu owombeza mawula ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa.
4 Naguummong dagiti Filisteo ket immayda nagkampo idiay Sunem; ket inummong ni Saul ti Israel ket nagkampoda iti Gilboa.
Tsono Afilisti anasonkhana nabwera kudzamanga misasa yawo ku Sunemu. Nayenso Sauli anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kumanga misasa yawo ku Gilibowa.
5 Idi nakita ni Saul ti armada dagiti Filisteo, nagbuteng isuna ket kasta unay ti panagkibba-kibba ti barukongna.
Sauli ataona gulu lankhondo la Afilisti anaopa ndipo ananjenjemera kwambiri.
6 Idi nagkararag ni Saul kenni Yahweh tapno agpatulong, saan isuna a sinungbatan ni Yahweh—uray babaen kadagiti tagtagainep wenno babaen iti Urim wenno babaen kadagiti profeta.
Choncho Sauli anafunsa nzeru kwa Yehova koma Yehova sanamuyankhe ngakhale kudzera mʼmaloto, kapena mwa Urimu ngakhalenso kudzera mwa aneneri.
7 Ket kinuna ni Saul kadagiti adipenna, “Ibirokandak iti babai a makium-uman kadagiti natay tapno mapanak makiuman kenkuana.” Kinuna dagiti adipenna kenkuana, “Wen, adda maysa a babai idiay Endor a makium-uman kadagiti natay.”
Kenaka Sauli anawuza nduna zake kuti, “Mundipezere mkazi amene amawombeza mawula kuti ndipite ndikafunse kwa iye.” Nduna zakezo zinamuyankha kuti, “Alipo mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ku Endori.”
8 Nanglimlimo ni Saul, nagarruat iti sabali a pagan-anay, ket napan a kaduana ti dua a lallaki; rabii a napanda iti ayan ti babai. Kinunana, “Makiumanka para kaniak, pangngaasim, babaen iti pannakisaritam kadagiti natay, awagam ti siasinoman nga inaganak.
Kotero Sauli anadzizimbayitsa navala zovala zachilendo. Tsono iye pamodzi ndi anthu awiri anapita nakafika kwa mkazi uja usiku, ndipo anamupempha kuti, “Chonde ndifunsireni nzeru kwa mizimu ya anthu akufa. Koma makamaka munditulutsire mzimu wa amene ndimutchule.”
9 Kinuna ti babai kenkuana, “Saanmo aya nga ammmo ti inaramid ni Saul, no kasano ti panangiparitna iti daga iti pannakiuman kadagiti natay wenno kadagiti espiritu. Isu nga apay a kayatnak a palab-ogan, tapno ipapataynak?”
Koma mkaziyo anayankha kuti, “Ndithu inu mukudziwa chimene Sauli anachita. Paja iye anachotsa mʼdziko muno anthu onse owombeza ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Chifukwa chiyani mukutchera moyo wanga msampha kuti ndiphedwe?”
10 Nagsapata ni Saul kenkuana iti nagan ni Yahweh a kinunana, “Iti nagan ni Yahweh nga adda iti agnanayon, awan ti pannusa a mapasamakto kenka gapu iti daytoy a banag.”
Koma Sauli analonjeza mkaziyo molumbira nati, “Pali Yehova wamoyo, iweyo sudzalangidwa chifukwa cha zimenezi.”
11 Ket kinuna ti babai, “Siasino ngarud ti awagak para kenka?” Kinuna ni Saul, “Awagam ni Samuel para kaniak.”
Kenaka mkaziyo anafunsa, “Ndikuyitanireni yani?” Iye anati, “Undiyitanire Samueli.”
12 Idi nakita ti babai ni Samuel, nagriaw isuna ket nagsao kenni Saul a kinunana, “Apay nga inallilawnak? Sika ni Saul.”
Pamene mkaziyo anaona Samueli anakuwa kwambiri, nawuza Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani inu mwandipusitsa? Inu ndinu Sauli!”
13 Kinuna ti ari kenkuana, “Saanka nga agbuteng. Ania ti makitam?” Kinuna ti babai kenni Saul, “Makitkitak ti maysa a dios a rum-rummuar manipud iti daga.”
Mfumuyo inamuwuza kuti, “Usaope. Kodi ukuona chiyani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Ndikuona mzimu ukutuluka pansi.”
14 Kinunana kenkuana, “Ania ti langana?” Kinuna ti babai, “Maysa a lakay ti rum-rumuar; nakakagay iti atiddog.” Ammon ni Saul a dayta ni Samuel, ket nagrukob isuna iti daga a mangipakita iti panagraemna kenkuana.
Sauli anafunsa, “Kodi mzimuwo ukuoneka motani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Amene akutuluka ndi munthu wokalamba ndipo wavala mkanjo.” Apo Sauli anadziwa kuti anali Samueli ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
15 Kinuna ni Samuel kenni Saul, “Apay a sininganak ken inawagannak?” Simmungbat ni Saul, “Mariribokanak unay, ta gubgubatendak dagiti Filisteo, ken binaybay-annakon ti Dios ket saannakon a sungsungbatan, uray babaen kadagiti profeta, wenno babaen kadagiti tagtagainep. Isu nga inawaganka, tapno ipakaammom kaniak no ania ti aramidek.”
Samueli anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandivutitsa pondiyitana kuti ndibwere kuno?” Sauli anayankha kuti, “Ine ndavutika kwambiri mʼmaloto. Afilisti akumenyana nane, ndipo Mulungu wandifulatira. Iye sakundiyankhulanso, ngakhale kudzera mwa aneneri kapena maloto. Choncho ndakuyitanani kuti mundiwuze zoti ndichite.”
16 Kinuna ni Samuel, “Ania ngarud ti kiddawem kaniak, ita ta pinanawannakan ni Yahweh ken nagbalin isunan a kabusormo?
Samueli anati, “Nʼchifukwa chiyani ukundifunsa ine, pakuti tsopano Yehova wakufulatira ndipo wasanduka mdani wako?
17 Inaramid ni Yahweh kenka ti imbagana nga aramidenna. Inikkat ni Yahweh ti pagarian manipud kadagiti imam ket intedna daytoy iti sabali—kenni David.
Yehova wakuchita zimene ananeneratu kudzera mwa ine. Yehova wachotsa ufumu mʼmanja mwako ndipo waupereka kwa mnansi wako, kwa Davide.
18 Gapu ta saanmo a tinungpal ti timek ni Yahweh ken saanmo nga impalak-am ti kasta unay a pungtotna kadagiti Amalekita, isu't gapuna nga inaramidna daytoy ita kenka.
Yehova wachita zimenezi lero chifukwa sunamvere mawu ake ndipo sunawawonongeretu Aamaleki.
19 Maysa pay, iyawatnakanto ni Yahweh ken ti Israel iti ima dagiti Filisteo. Inton bigat, sika ken dagiti annakmo ket maitiponto kaniak. Iyawatto met ni Yahweh ti armada ti Israel iti ima dagiti Filisteo.”
Yehova adzapereka ndithu iweyo pamodzi ndi Aisraeli kwa Afilisti. Ndipo mmawa iweyo ndi ana ako mudzakhala ndi ine kuno. Ndithu Yehova adzapereka gulu lankhondo la Aisraeli kwa Afilisti.”
20 Ket dagus a napasag ni Saul iti daga ket kasta unay ti butengna gapu kadagiti imbaga ni Samuel. Kimmapsut isuna, ta saan isuna a nangan iti nagmalmalem, uray iti dayta a nagpatnag.
Nthawi yomweyo Sauli anagwa pansi atadzazidwa ndi mantha chifukwa cha mawu a Samueli. Analibenso mphamvu, pakuti sanadye tsiku lonse.
21 Immasideg ti babai kenni Saul ket nakitana a mariribokan unay isuna, kinunana kenkuana, “Kitaem, dinengngeg ti adipenmo a babai ti timekmo; impustak ti biagko ket dimngegak kadagiti sasao nga imbagam kaniak.
Mkazi uja tsono anasendera kufupi ndi Sauli, ndipo ataona kuti Sauli akuchita mantha, anamuwuza kuti, “Taonani, mdzakazi wanune ndakumverani. Ndayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndamvera zimene munandiwuza.
22 Ita ngarud, ipakpakaasik kenka, denggem met ti timek ti adipenmo a babai, ken ipalubosmo a mangidasarak iti bassit a taraon iti sangoanam. Manganka tapno pumigsaka iti panagawidmo.”
Tsono inunso mumvere mawu a mdzakazi wanune. Mundilole kuti ndikupatseni ka buledi pangʼono kuti mukhale ndi mphamvu zoyendera pa ulendo wanu.”
23 Ngem nagkedked ni Saul ket kinunana, “Saanak a mangan.” Ngem impapilit dagiti adipen ni Saul, kasta met ti babai ket dimngeg isuna iti timekda. Timmakder ngarud manipud iti daga ket nagtugaw iti pagiddaan.
Iye anakana ndipo anati, “Ayi, ine sindidya.” Koma nduna zake pamodzi ndi mkaziyo anamuwumiriza, ndipo anawamvera. Choncho anadzuka pansi nakhala pa bedi.
24 Addaan ti babai iti napalukmeg a baka iti balayna; nagdardaras a nangparti iti daytoy; nangala iti arina, minasana daytoy, ket linutona daytoy a tinapay nga awan laokna a lebadurana.
Mkaziyo anali ndi mwana wangʼombe wonenepa ndipo anamupha mwachangu. Anatenga ufa nawukanyanga ndipo anaphika buledi wopanda yisiti.
25 Inyegna daytoy iti sangoanan ni Saul ken kadagiti adipenna, ket nanganda. Kalpasanna, nagrubbuatda ket pimmanawda iti dayta a rabii.
Tsono anapereka bulediyo kwa Sauli ndi nduna zake ndipo anadya. Pambuyo pake ananyamuka kupita kwawo usiku womwewo.

< I Samuel 28 >