< 1 Ar-ari 22 >

1 Tallo a tawen ti naglabas nga awan ti gubat iti nagbaetan ti Aram ken Israel.
Kwa zaka zitatu panalibe nkhondo pakati pa Aramu ndi Israeli.
2 Ket napasamak nga iti maikatlo a tawen, napan ni Jehosafat nga ari ti Juda iti ari ti Israel.
Koma pa chaka chachitatu, Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita kukacheza ndi mfumu ya ku Israeli.
3 Ita, kinuna ti ari ti Israel kadagiti adipenna, “Ammoyo kadi a ti Ramot Galaad ket kukuatayo, ngem awan ti ar-aramidentayo tapno maalatayo daytoy manipud iti ima ti ari ti Aram?”
Mfumu ya ku Israeli nʼkuti itawuza atumiki ake kuti, “Kodi inu simukudziwa kuti Ramoti Giliyadi ndi dera lathu ndipo ife palibe chimene tikuchita kuti tilitenge deralo mʼmanja mwa mfumu ya Aramu?”
4 Isu a kinunana kenni Jehosafat, “Kaduaannak kadi a maki-gubat idiay Ramot Galaad?” Simmungbat ni Jehosafat iti ari ti Israel, “Agserbiak kenka, agbalin dagiti tattaok a tattaom, ken dagiti kabaliok a kabaliom.”
Tsono iye anafunsa Yehosafati kuti, “Kodi udzapita nane ku nkhondo ku Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha mfumu ya ku Israeli kuti, “Ine ndili monga inu, anthu anga monga anthu anu, akavalo anga monga akavalo anu.”
5 Kinuna ni Jehosafat iti ari ti Israel, “Pangaasim ta kiddawem ti panangidalan manipud iti sao ni Yahweh no ania ti rumbeng nga aramidem nga umuna.”
Koma Yehosafati anawuzanso mfumu ya ku Israeli kuti, “Poyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
6 Ket inummong ti ari ti Israel dagiti amin a profeta, nga uppat a gasut a lallaki, ket kinunana kadakuada, “Mapanak kadi makigubat idiay Ramot Galaad, wenno saan?” Kinunada, “Rautem, ta iyawatto ti Apo daytoy iti ari.”
Choncho mfumu ya Israeli inasonkhanitsa pamodzi aneneri okwanira 400, ndipo inawafunsa kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena ndileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Ambuye waupereka mzindawo mʼmanja mwa mfumu.”
7 Ngem kinuna ni Jehosafat, “Awan kadin ditoy ti sabali pay a profeta ni Yahweh a mabalintayo a pagkiddawan iti balakad?”
Koma Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi kuno kulibenso mneneri wina wa Yehova kumene ife tingakafunsireko nzeru?”
8 Kinuna ti ari ti Israel kenni Jehosafat, “Adda pay maysa a tao a mabalintayo a pagkiddawan iti balakad manipud kenni Yahweh a tumulong, ni Micaias nga anak ni Imla, ngem kagurak isuna ta saan a mangipadpadto iti aniaman a nasayaat a banag maipanggep kaniak, pasig a kinarigat laeng.” Ngem kinuna ni Jehosafat, “Saan koma nga ibaga ti ari dayta.”
Mfumu ya ku Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife tingakafunsire kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa iyeyo samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa nthawi zonse. Dzina lake ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu musatero.”
9 Ket nangayab ti ari ti Israel iti opisial ket binilinna, “Iyegyo a dagus ni Micaias nga anak ni Imla.”
Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa atumiki ake ndipo inati, “Kayitane Mikaya mwana wa Imula msangamsanga.”
10 Ita, nakatugaw ni Ahab nga ari ti Israel ken ni Jehosafat nga ari ti Juda kadagiti tronoda, nakakawesda kadagiti kawes ti ari, iti nawaya a lugar iti pagserekan iti ruangan ti Samaria, ket nangipadto amin dagiti profeta, iti sangoananda.
Atavala mikanjo yawo yaufumu, mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopondera tirigu pafupi ndi chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
11 Nangaramid ni Zedekia nga anak ni Kenaana kadagiti landok a sinan sara ket kinunana, “Kastoy ti imbaga ni Yahweh: 'Babaen kadagitoy ket sangdoenyonto dagiti taga-Aram agingga a maibusda.”
Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana nʼkuti atapanga nyanga zachitsulo ndipo iye ananenera kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi, inu mudzagunda nazo Aaramu mpaka iwo atawonongeka.’”
12 Kasta met laeng ti impadto dagiti amin a profeta, a kunada, “Darupenyo ti Ramot Galaad ket agballigikayo, ta iyawat ni Yahweh daytoy iti ari.”
Aneneri ena onse ananenera zomwezonso. Iwo anati, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
13 Nagsao kenkuana ti mensahero a napan nangayab kenni Micaias, a kunana, “Ita dumngegka, pasig a nasayaat a banbanag dagiti sasao nga imbaga dagiti profeta ti ari. Pangngaasim ta kasta met koma ti sawem ket nasayaat a banbanag ti ibagam.”
Wamthenga amene anapita kukayitana Mikaya anamuwuza kuti, “Taonani, aneneri onse monga munthu mmodzi akunenera za kupambana kwa mfumu. Mawu anunso akhale ogwirizana ndi mawu awo, ndipo mukayankhule zabwino.”
14 Simmungbat ni Micaias, “Iti nagan ni Yahweh nga adda iti agnanayon, ti ibaga ni Yahweh kaniak ti sawek.”
Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndikawawuza zokhazo zimene Yehova akandiwuze.”
15 Idi napan isuna iti ayan ti ari, kinuna ti ari kenkuana, “Micaias, mapankami kadi makigubat idiay Ramot Galaad, wenno saan?” Simmungbat ni Micaias, “Rautem ket parmekem. Iyawatto ni Yaweh daytoy iti ima ti ari.”
Atafika, Ahabu anamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Pitani ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”
16 Ket kinuna ti ari kenkuana, “Namin-ano a daras nga imbagak kenka nga ikarim nga ibagam laeng kaniak ti kinapudno iti nagan ni Yahweh?”
Ahabu anati kwa iye, “Kodi ndikulumbiritse kangati kuti undiwuze zoona zokhazokha mʼdzina la Yehova?”
17 Isu a kinuna ni Micaias, “Nakitak ti entero nga Israel a nawarawara kadagiti banbantay, kasla da la karnero nga awan iti mangipaspastor, ket kinuna ni Yahweh, 'Awan ti mangipaspastor kadagitoy. Agsubli koma ti tunggal tao iti balayna a sitatalged.”’
Pamenepo Mikaya anayankha kuti, “Ndinaona Aisraeli onse atamwazikana pa mapiri ngati nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mwamtendere.’”
18 Isu a kinuna ti ari ti Israel kenni Jehosafat, “Saan kadi nga imbagak kenka a saan isuna nga agipadto iti nasayaat maipanggep kaniak, ngem didigra laeng?”
Mfumu ya ku Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti ameneyu samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa zokhazokha?”
19 Ket kinuna ni Micaias, “Denggem ngarud ti sao ni Yahweh: Nakitak ni Yahweh a nakatugaw iti tronona, ken dagiti amin a buybuyot ti langit ket agtaktakder iti makannawan ken iti makannigidna.
Mikaya anapitiriza kuyankhula nati, “Tsono imvani mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu, gulu lonse la kumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi ku dzanja lake lamanzere.
20 Kinuna ni Yahweh, 'Siasino ti mangallilaw kenni Ahab, tapno mapan isuna ken maparmek idiay Ramot Galaad?' Ket nagduduma ti insungbat ti tunggal maysa.
Ndipo Yehova anati, ‘Kodi ndani amene akamukope Ahabu kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi, nʼkukafera komweko?’” “Wina anapereka maganizo ena ndipo winanso maganizo ena.
21 Ket adda maysa nga espiritu a nagpasango, nagtakder iti sangoanan ni Yahweh, ket kinunana, 'Siak ti mangallilaw kenkuana.' Kinuna ni Yahweh kenkuana, 'Kasano?'
Potsirizira, mzimu wina unabwera ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, ‘Ine ndidzamukopa.’”
22 Simmungbat ti espiritu, 'Mapanak ken agbalinak nga agul-ulbod nga espiritu iti ngiwat dagiti amin a profetana.' Simmungbat ni Yahweh, 'Allilawem isuna, ket agballigikanto. Mapanka ket aramiden ti imbagam.'
Yehova anafunsa kuti, “Ukamukopa bwanji?” Mzimuwo unati, “Ndidzapita ndi kukakhala mzimu wabodza pakamwa pa aneneri ake onse.” Yehova anati, “‘Iwe udzamukopadi. Pita kachite zomwezo.’
23 Ita kitaem, nangikabil ni Yahweh iti agul-ulbod nga espiritu iti ngiwat dagiti amin a profetam, ket nangituyang ni Yahweh ti didigra para kenka.”
“Ndipo tsopano taonani, Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anu onsewa. Yehova waneneratu kuti mukaona mavuto.”
24 Kalpasanna immasideg ni Zedekaia nga anak ni Kenaana, tinungpana ni Micaias, ket kinunana, “Kasano a rimmuar kaniak ti Espiritu ni Yahweh tapno makitungtong kenka?”
Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi namenya Mikaya patsaya. Iye anafunsa Mikaya kuti, “Kodi mzimu wa Yehova unadzera njira iti pamene umatuluka mwa ine kuti uziyankhula ndi iwe?”
25 Kinuna ni Micaias, “Kitaem, maammoamto dayta, iti dayta nga aldaw, inton agtarayka nga aglemmeng iti akin uneg a siled.
Mikaya anayankha kuti, “Udzaona pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
26 Kinuna ti ari ti Israel iti adipena, “Tiliwem ni Micaias ket iyapanmo kenni Amon, a gobernador ti siudad, kenni Joas, nga anakko.
Pamenepo mfumu ya ku Israeli inalamula kuti, “Mugwireni Mikaya ndipo mubwerere naye kwa Amoni mkulu wa mzinda, ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu
27 Ibagam kenkuana, 'Kuna ti ari, Ibaludyo daytoy a tao ket bassit a tinapay ti ipakanyo ken ikkanyo ti laeng ti bassit a danum, agingga a makasangpetak a sitatalged.”’
ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyikeni mʼndende munthu uyu ndipo musamupatse chakudya china koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwerera mwamtendere.’”
28 Ket kinuna ni Micaias, “No makasublika a sitatalged, saan ngarud a nagsao ni Yahweh kaniak.” Ket kinunana pay, “Denggenyo daytoy, dakayo amin a tattao.”
Mikaya ananena kuti, “Ngati mudzabwerera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo iye anapitiriza kunena kuti, “Gwiritsitsani mawu angawa, anthu inu nonse!”
29 Napan ngarud ni Ahab nga ari ti Israel, ken ni Jehosafat nga ari ti Juda idiay Ramot Galaad.
Choncho mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
30 Kinuna ti ari ti Israel kenni Jehosafat, “Manglimlimoak ket mapanak iti paggugubatan, ngem ikawesmo dagiti pagan-anaymo a kas ari.” Isu a nanglimlimo ngarud ti ari ti Israel ket napan iti paggugubatan.
Mfumu ya ku Israeli inawuza Yehosafati kuti, “Ine ndidzalowa mu nkhondoyi modzibisa, koma inu muvale zovala zanu zaufumu.” Choncho mfumu ya ku Israeli inadzibisa ndi kupita ku nkhondo.
31 Ita, binilin ti ari ti Aram dagiti tallo pulo ket dua a kapitan ti karwahena, a kunana, “Saanyo a darupen uray siasinoman kadagiti soldado. Ketdi, darupenyo laeng ti ari ti Israel.”
Tsono mfumu ya ku Aramu nʼkuti italamulira anthu ake 32 olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu, koma mfumu ya ku Israeli.”
32 Ket idi nakita dagiti kapitan dagiti karwahe ni Jehosafat kinunada, “Sigurado a dayta ti ari ti Israel.” Dinarupda isuna, ket nagriaw ni Jehosafat.
Olamulira magaleta ataona Yehosafati, ankaganiza kuti, “Ndithu iyi ndiye mfumu ya ku Israeli.” Choncho anabwerera kukamenyana naye, koma Yehosafati atafuwula,
33 Ket idi nakita dagiti mangidadaulo kadagiti karwahe a saan nga isu ti ari ti Israel, saandan nga intuloy iti panangkamatda kenkuana.
olamulira akavalo anaona kuti sanali mfumu ya ku Israeli ndipo analeka kumuthamangitsa.
34 Ngem adda maysa a lalaki a nangipasaksak lattan iti panana ket natamaan ti ari ti Israel iti nagsaipan ti kabalna. Ket kinuna ni Ahab iti mangiturturong iti karwahena, “Agsublita ken ipanawnak ditoy paggugubatan, ta nasugatanak iti nakaro.”
Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndi kulasa mfumu ya ku Israeli polumikizira malaya ake odzitetezera. Mfumu inawuza woyendetsa galeta lake kuti, “Tembenuka ndipo undichotse pa nkhondo pano pakuti ndalasidwa.”
35 Kimarkaro ti gubat iti dayta nga aldaw, ket sisasadag ti ari iti karwahena a nakasango kadagiti taga-Aram. Natay isuna iti karabianna. Nagsayasay ti darana manipud iti sugatna iti datar iti karwahe.
Nkhondo inakula kwambiri tsiku limenelo, ndipo mfumu inakhala tsonga mʼgaleta lake moyangʼanana ndi Aaramu. Magazi ake ankayenderera pansi kuchokera mʼgaleta, ndipo pa nthawi ya madzulo inamwalira.
36 Ket idi lumlumneken ti init, impukkaw dagiti armada, a kunada, “Agsubli ti tunggal maysa iti siudadna, ken tunggal maysa iti rehionna!”
Pamene dzuwa linkalowa, kunamveka mfuwu wa nkhondo kuti, “Munthu aliyense apite ku mzinda wa kwawo, aliyense apite ku dziko la kwawo!”
37 Natay ngarud ni Ahab ket impanda idiay Samaria, ket impunponda isuna idiay Samaria.
Ndipo mfumu ija inafa, nabwera nayo ku Samariya, ndipo anayika mʼmanda kumeneko.
38 Binugwanda ti karwahe iti pagdigosan idiay Samaria, ket dinilpatan dagiti aso ti darana (ditoy ti pagdigdigusan dagiti balangkantis), kas iti sao nga imbaga ni Yahweh.
Anatsuka galeta lija pa dziwe la ku Samariya (pamene ankasamba akazi achiwerewere) ndipo agalu ananyambita magazi a mfumuyo, monga momwe Yehova ananenera.
39 Maipapan kadagiti dadduma a banbanag maipanggep kenni Ahab, amin nga inaramidna, ti impatakderna a marfil a balay, ken amin a siudad nga imbangonna saan kadi a naisurat dagitoy iti Libro dagiti Pakasaritaan dagiti Ar-ari ti Israel?
Tsono ntchito zina za Ahabu, kuphatikiza zonse anazichita, nyumba yaufumu imene anamanga yokutidwa ndi minyanga ya njovu, mizinda yotetezedwa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
40 Pimmusay ngarud ni Ahab, ket ni Ahazias nga anakna a lalaki ti nagbalin nga ari a simmukat kenkuana.
Ahabu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
41 Ket nangrugi a nagturay idiay Juda ni Jehosafat nga anak ni Asa idi maikapat a tawen a panagturay ni Ahab nga ari ti Israel.
Yehosafati, mwana wa Asa anakhala mfumu ya ku Yuda chaka chachinayi cha Ahabu mfumu ya ku Israeli.
42 Tallopulo ket lima ti tawen ni Jehosafat idi nagturay isuna, ket nagturay isuna iti duapulo ket lima a tawen idiay Jerusalem. Ti nagan ti inana ket Azuba, nga anak a babai ni Silhi.
Yehosafati anali wa zaka 35 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira ku Yerusalemu zaka 25. Amayi ake anali Azuba mwana wa Silihi.
43 Nagbiag isuna iti wagas ni Asa nga amana; saanna a tinallikudan dagitoy; inaramidna no ania ti nasayaat iti imatang ni Yahweh. Nupay kasta, saan pay a naikkat dagiti disso a pagdaydayawan. Agidatdaton ken agpupuor latta iti insenso dagiti tattao kadagiti disso a pagdaydayawan.
Pa zinthu zonse, Yehosafati anayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanachite zotsutsana ndi machitidwe a abambo ake. Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova. Komabe, malo azipembedzo sanawawononge, ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
44 Nakipagkapia ni Jehosafat iti ari ti Israel.
Yehosafati anakhala mwamtendere ndi mfumu ya ku Israeli.
45 Maipapan kadagiti dadduma a banbanag maipangep kenni Jehosafat, ken ti kinabileg nga impakitana ken no kasano a nangabak isuna iti gubat, saan kadi a naisurat dagitoy iti Libro dagiti Pakasaritaan dagiti Ar-ari ti Juda?
Ntchito zake zina za Yehosafati, zinthu zimene anachita ndi zamphamvu zimene anaonetsa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Yuda?
46 Pinapanawna manipud iti daga dagiti nabatbati a balangkantis a natda kadagiti al-aldaw ti amana a ni Asa.
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zachiwerewere mwa chipembedzo amene anatsalira pa nthawi ya ulamuliro wa Asa, abambo ake.
47 Awan ti ari idiay Edom, ngem nagturay ti pannakabagi ti ari sadiay.
Nthawi imeneyo kunalibe mfumu ku Edomu, amene ankalamulira anali munthu woyikidwa ndi mfumu ya ku Yuda.
48 Nangaramid ni Jehosafat kadagiti barko a paglayag a mapan idiay Ofir gapu iti balitok, ngem saanda a nakadanon gapu ta nadadael dagiti barko idiay Ezion Geber.
Yehosafati anapanga sitima zapamadzi zopita ku Ofiri kukatenga golide, koma sitimazo sizinayende chifukwa zinawonongeka ku Ezioni Geberi.
49 Ket kinuna ni Ahazias nga anak ni Ahab kenni Jehosafat, “Ipalubosmo koma a makilayag dagiti adipenko kadagiti adipenmo kadagiti barko.” Ngem saan nga immannugot ni Jehosafat.
Nthawi imeneyo Ahaziya mwana wa Ahabu anawuza Yehosafati kuti, “Anthu anga ayende pa madzi pamodzi ndi anthu anu,” koma Yehosafati anakana.
50 Pimmusay ni Jehosafat ket naitabon a kaduada iti siudad ni David, a kapuonanna; ni Jehoram nga anakna ti nagbalin nga ari a simmukat kenkuana.
Ndipo Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
51 Nagturay ni Ahazias nga anak ni Ahab iti Israel idiay Samaria idi maikasangapulo ket pito a tawen a panagturay ni Jehoshafat nga ari ti Juda, ket nagturay isuna iti dua a tawen iti Israel.
Ahaziya mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya ku Israeli ku Samariya mʼchaka cha 17 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
52 Dakes ti inaramidna iti imatang ni Yahweh ken nagbiag iti wagas ti amana, ken iti wagas ti inana, ken iti wagas ni Jeroboam nga anak ni Nabat, ket iti kasta insungsongna ti Israel nga agbasol.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, chifukwa anayenda mʼnjira za abambo ndi amayi ake komanso mʼnjira za Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli.
53 Nagserbi isuna kenni Baal ken dinayawna isuna, isu a pinagpungtotna ni Yahweh, a Dios ti Israel, a kas iti inaramid ti amana.
Potumikira ndi kupembedza Baala, iye anakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli, monga momwe anachitira abambo ake.

< 1 Ar-ari 22 >