< 1 Ar-ari 1 >

1 Lakay unayen ni Ari David. Binalkotda isuna kadagiti lupot, ngem saanen a bumara ti bagina.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 Isu a kinuna dagiti adipenna kenkuana, “Mangbirokkami koma iti maysa a balasang a birhen para iti apomi nga ari. Pagserbianna koma ti ari ken aywananna isuna. Agpungan koma isuna iti takiagna tapno bumara ti bagi ti apomi nga ari.”
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 Nangbirokda ngarud iti napintas a babai kadagiti amin a beddeng ti Israel. Nasarakanda ni Abisag a taga-Sunem ket inyegda isuna iti ari.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 Nakapinpintas unay ti babai. Pinagserbianna ti ari ken inaywananna isuna, ngem saan a sinagsagid isuna ti ari.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 Iti dayta a tiempo, ni Adoniha nga anak ni Haggit, intan-okna ti bagina, a kunana, “Siakon ti agbalin nga ari.” Isu a nangisagana isuna kadagiti karwahe ken kadagiti nakakabalio ken adda pay limapulo a lallaki nga agtaray nga umun-una kenkuana.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6 Saan a pulos a binabalaw isuna ti amana a kunana, “Apay nga inaramidmo daytoy wenno dayta?” Nataer met unay a lalaki ni Adonija, isuna ti simmaruno kenni Absalom a naiyanak.
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 Kinatulagna ni Joab nga anak ni Zeruyas ken ni Abiatar a padi. Simmurotda kenni Adoniha ken tinulonganda isuna.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 Ngem ni Zadok a padi, ni Benaias nga anak ni Jehoyada, ni Natan a profeta, ni Simei, ni Reihi, ken dagiti mamaingel a lallaki a tattao ni David ket saan a simmurot kenni Adoniha.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 Nangidaton ni Adoniha iti karnero, bakbaka, ken nalulukmeg nga urbon a baka iti ayan ti bato ti Zohelet nga abay ti En Rogel. Inawisna amin dagiti kakabsatna a lallaki, dagiti lallaki nga annak ti ari, ken amin a lallaki iti Juda nga adipen ti ari.
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 Ngem saanna nga inawis ni Natan a profeta, ni Benaias, dagiti mamaingel a lallaki, wenno ni Solomon a kabsatna.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Kalpasanna, kinasarita ni Natan ni Batseba nga ina ni Solomon, kinunana, “Saanmo kadi a nangngeg a nagbalinen nga ari ni Adoniha nga anak ni Haggit, ket saan nga ammo daytoy ni David nga apotayo?
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 Ita ngarud, denggem koma ti ibalakadko kenka tapno maisalakanmo ti biagmo ken ti biag ti anakmo a ni Solomon.
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 Mapanka kenni Ari David; ibagam kenkuana, 'Apok nga ari, saan kadi nga inkarim iti adipenmo, a kunam, “Awan duadua a ni Solomon nga anakmo ti sumukat kaniak nga agturay, ket agtugawto isuna iti tronok?” Apay ngarud nga agturturayen ni Adoniha?'
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 Bayat nga addaka sadiay a makisarsarita iti ari, sumarunoakto kenka ket patalgedak dagiti saom.”
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 Napan ngarud ni Batseba iti siled ti ari. Lakay unayen ti ari, ket ni Abisag a taga-Sunem, pagserserbianna ti ari.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 Nagruknoy ken nagrukob ni Batseba iti sangoanan ti ari. Ket kinuna ti ari, “Ania ti kayatmo?”
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 Kinunana kenkuana, “Apok, inkarim iti adipenmo babaen iti nagan ni Yahweh a Diosmo, a kunam, 'Awan duadua a ni Solomon nga anakmo ti sumukat kaniak nga agturay, ket agtugawto isuna iti tronok.'
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 Ita, kitaem, nagbalinen nga ari ni Adoniha, ket sika apok nga ari, saanmo nga ammo daytoy.
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 Nangidaton isuna kadagiti baka, kadagiti napalukmeg nga urbon a baka, ken nakaad-adu a karnero, ket inawisna amin nga annak ti ari, ni Abiatar a padi, ken ni Joab a pangulo ti armada, ngem saanna nga inawis ni Solomon nga adipenmo.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Apok nga ari, kumitkita amin kenka dagiti mata ti Israel, ur-urayenda nga ibagam kadakuada no siasino ti agtugaw iti tronom a sumukat kenka, apok.
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 Ta no saan ket mapasamakto, nga inton pumusayto ti apok, siak ken ti anakko a ni Solomon ket maibilangto a kriminal.”
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 Bayat a makisarsarita pay laeng isuna iti ari, simrek ni Natan a profeta.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 Imbaga dagiti adipen iti ari, “Adda ditoy ni Natan a profeta.” Idi simrek isuna iti ayan ti ari, nagkurno iti sangoanan ti ari.
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 Kinuna ni Natan, “Apok nga ari, pudno kadi nga imbagam, 'Ni Adoniha ti agturay kalpasan ti panagturayko, ket isuna ti agtugaw iti tronok?'
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 Ta simmalog isuna ita nga aldaw ket nangidaton kadagiti kalakian a baka, napalukmeg a baka, ken nakaad-adu a karnero, ket inawisna amin dagiti annak ti ari, dagiti papangulo ti armada, ken ni Abiatar a padi. Mangmangan ken agiinomda iti sangoananna a kunkunada, 'Agbiag ni Ari Adoniha!'
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 Ngem no maipanggep kaniak, siak nga adipenmo, ni Zadok a padi, ni Benaias nga anak ni Jehoyada, ken ti adipenmo a ni Solomon, ket saannakami nga inawis.
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 Naaramid kadi daytoy ti apok nga ari a saanna nga imbagbaga kadakami nga adipenmo, siasino ti rumbeng nga agtugaw iti trono kalpasan ti panagturayna?”
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 Ket simmungbat ni Ari David a kunana, “Paumayenyo ditoy ni Batseba.” Immay isuna iti ayan ti ari ket nagtakder iti sangoananna.
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 Nagsapata ti ari a kunana, “Iti nagan ni Yahweh nga adda iti agnanayon, a nangispal kaniak iti amin a peggad,
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 kas iti naikarikon kenka babaen iti nagan ni Yahweh a Dios ti Israel a kunak, 'Ni Solomon nga anakmo ti agturay kalpasan ti panagturayko, ket agtugawto isuna iti tronok a sumukat kaniak,' Aramidek daytoy ita nga aldaw.”
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 Ket nagkurno ni Batseba iti sangoanan ti ari ket kinunana, “Agbiag koma iti agnanayon ni Ari David nga apok!”
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 Kinuna ni Ari David, “Ayabanyo ditoy ni Zadok a padi, ni Natan a profeta, ken ni Benaias nga anak ni Jehoyada.” Immayda ngarud iti ayan ti ari.
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 Kinuna ti ari kadakuada, “Ikuyogyo dagiti adipen ti apoyo, ket pagsakayenyo ni Solomon nga anakko iti asnok ket ipanyo idiay Gihon.
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 Pulotan koma isuna ni Zadok a padi ken ni Natan a profeta tapno agbalin nga ari iti entero nga Israel ken puyotanyo ti tangguyob ket ipukkawyo, “Agbiag ni Ari Solomon!”
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 Kalpasanna, sumurotkayonto kenkuana, ket umayto isuna agtugaw iti tronok; ta agbalinto nga ari a sumukat kaniak. Dinutokak isuna a mangituray iti Israel ken Juda.”
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 Simmungbat ni Benaias nga anak ni Jehoyada iti ari, “Mapasamak koma dayta! Patalgedan koma daytoy ni Yahweh a Dios ti apok nga ari.
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 Kas iti pannakikaadda ni Yahweh iti apok nga ari, kasta koma met ti pannakikaaddana kenni Solomon, ket pagbalinen pay koma ni Yahweh a natantan-ok ti tronona ngem iti trono ni Ari David nga apok.”
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 Simmalog ngarud ni Zadok a padi, ni Natan a profeta, ni Benaias nga anak ni Jehoyada, ken dagiti Kereteo ken dagiti Peleteo ket pinagsakayda ni Solomon iti asno ni Ari David; impanda isuna idiay Gihon.
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 Innala ni Zadok a padi ti sinan-sara a pagkargaan iti lana manipud iti tolda ket pinulotanna ni Solomon. Kalpasanna, pinuyotanda ti tangguyob, ket kinuna amin dagiti tattao, “Agbiag ni Ari Solomon!”
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 Ket amin dagiti tattao, simmarunoda kenkuana a simmang-at, ket tinukar dagiti tattao dagiti plauta ket nagrag-oda iti kasta unay nga uray la aggungon ti daga iti ariwawada.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 Nangngeg daytoy ni Adoniha ken dagiti amin a sangaili a kakaduana bayat a malmalpas ti pannanganda. Idi nangngeg ni Joab ti uni ti tangguyob, kinunana, “Apay ngata a naariwawa iti siudad?”
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 Bayat nga agsasao pay laeng isuna, dimteng ni Jonatan nga anak ni Abiatar a padi. Kinuna ni Adoniha kenkuana, “Dumanonka, ta mapagtalkanka a tao ken mangiyeg ti naimbag a damag.”
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 Simmungbat ni Jonatan ket kinunana kenni Adoniha, “Ni Ari David nga apotayo, pinagbalinnan nga ari ni Solomon.
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 Ket impakuyog ti ari kenkuana ni Zadok a padi, ni Natan a profeta, ni Benaias nga anak ni Jehoyada, dagiti Kereteo ken dagiti Peleteo. Pinagsakayda ni Solomon iti asno ti ari.
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 Pinulotan isuna ni Zadok a padi ken ni Natan a profeta idiay Gihon, ket manipud sadiay, simmang-atda nga agraragsak, isu a naariwawa iti siudad. Daytoy ti ariwawa a nangngegyo.
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 Kasta met a nakatugawen ni Solomon iti trono ti pagarian.
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 Malaksid iti daytoy, immay dagiti adipen ti ari tapno bendisionanda ni Ari David nga apotayo, kunada, 'Pagbalinen koma ti Diosmo ti nagan ni Solomon a natantan-ok ngem iti naganmo, ken pagbalinenna a natantan-ok ti tronona ngem iti tronom.' Kalpasanna, nagdumog ti ari iti pagiddaanna.
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 Kinuna met ti ari, 'Madaydayaw ni Yahweh a Dios ti Israel, a nangted iti tao nga agtugaw iti tronok iti daytoy nga aldaw, ket nakita a mismo dayta dagiti matak.'”
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Ket nagbuteng amin dagiti sangaili ni Adoniha; timmakderda ket nagsipanawda.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 Nagbuteng ni Adoniha kenni Solomon, timmakder ket napan immiggem kadagiti sara iti altar.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 Ket adda nangibaga kenni Solomon iti daytoy a kunana, “Kitaenyo, mabuteng ni Adoniha kenni Ari Solomon, ta immiggem isuna kadagiti sara iti altar a kunkunana, 'Agkari koma nga umuna kaniak ni Ari Solomon a saanna a patayen ti adipenna babaen iti kampilan.'”
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 Kinuna ni Solomon, “No ipakitana a mapagtalkan isuna a tao, awan ti uray maysa a buokna a matnag iti daga, ngem no kinadangkes ti adda kenkuana, matay isuna.”
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 Isu a nangibaon ni Solomon iti lallaki a mapan mangibaba kenni Adoniha manipud iti altar. Napan isuna ket nagtamed kenni Ari Solomon, ket kinuna ni Solomon kenkuana, “Agawidka.”
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< 1 Ar-ari 1 >