< 1 Corinto 10 >

1 Kayatko a maamoanyo, kakabsat a lallaki ken babbai, a dagiti ammatayo ket addada amin iti babaen ti ulep ken limmasatda amin iti baybay.
Pakuti sindikufuna kuti inu mukhale osadziwa zenizeni, abale, kuti makolo athu anatsogozedwa ndi mtambo ndikuti onse anawoloka nyanja.
2 Nabautisaranda amin kenni Moises iti ulep ken iti baybay,
Ndipo onse anabatizidwa mwa Mose mu mtambo ndi mʼnyanja.
3 ken nanganda amin iti maymaysa a naespirituan a taraon.
Onse anadya chakudya chimodzi chauzimu
4 Imminomda amin iti maymaysa a naespirituan a mainom. Ta imminomda manipud iti naespirituan a bato a simmurot kadakuada, ken dayta a bato ket ni Cristo.
ndipo anamwa chakumwa chimodzi chauzimu; popeza anamwa kuchokera mʼthanthwe lomwe anayenda nalo, ndipo thanthwe limeneli linali Khristu.
5 Ngem saan unay a naay-ayo ti Dios iti kaadduan kadakuada, ket naiwara dagiti bangkayda iti let-ang.
Ngakhale zinali choncho, Mulungu sanakondwere ndi ambiri a iwo, motero ambiri mwa iwo anafera mʼchipululu.
6 Ita, pagtuladan dagitoy a banbanag para kadatayo, tapno saantayo nga agtarigagay kadagiti dakes a banbanag a kas iti inaramidda.
Tsono zinthu izi zinachitika kuti zikhale chitsanzo, kuti ife tisayike mitima yathu pa zinthu zoyipa monga anachitira makolo athuwo.
7 Saankayo nga agbalin a managrukbab kadagiti didiosen, a kas kadagiti dadduma kadakuada. Daytoy ket kas iti naisurat, “Nagtugaw a nangan ken uminom dagiti tattao, ken timmakder nga agsala nga addaan iti tarigagay a kinaderrep.”
Musakhale anthu opembedza mafano, monga analili ena mwa iwo. Pakuti zalembedwa kuti, “Anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.”
8 Saantayo nga agaramid iti kinaderrep, a kas iti inaramid ti kaadduan kadakuada. Duapulo ket tallo a ribo ti natay iti maysa nga aldaw gapu iti daytoy.
Tisachite chigololo monga ena mwa iwo anachitira ndipo tsiku limodzi anafapo anthu 23,000.
9 Saantayo a suoten ni Cristo, a kas iti inaramid ti kaadduan kadakuada ket nadadaelda babaen kadagiti ul-uleg.
Tisamuyese Khristu, monga ena mwa iwo anachitira ndipo anaphedwa ndi njoka.
10 Ken saankayo nga agtanabutob, a kas ti inaramid ti kaadduan kadakuada, ket nadadaelda babaen iti anghel ti patay.
Ndipo osamawiringula, monga ena mwa iwo anachitira naphedwa ndi mngelo wowononga.
11 Ita, napasamak dagitoy a banbanag kadakuada a kas pagtuladan maipaay kadatayo. Naisuratda maipaay iti pakasursuruantayo - maipaay kadatayo nga immayan ti pagpatinggaan ti panawen. (aiōn g165)
Zinthu izi zinawachitikira kuti zikhale chitsanzo ndipo zinalembedwa kuti zikhale chenjezo kwa ife, amene tiyandikira nthawi ya kutha kwa zonse. (aiōn g165)
12 Ngarud, ti siasinoman a mangipagarup a makatakder ket agannad koma a saan a matinnag.
Choncho, ngati mukuganiza kuti mwayima mwamphamvu, samalani mungagwe!
13 Awan ti sulisog nga immay kadakayo a saan a gagangay iti amin a sangkataoan. Ngem ketdi, napudno ti Dios. Saanna nga ipalubos a masulisogkayo iti labes ti kabaelanyo. Iti sulisog ket ipaayna met laeng ti wagas tapno makalisi, tapno maibturanyo daytoy.
Palibe mayesero amene mwakumana nawo oposa amene anthu ena onse anakumana nawo. Mulungu ngokhulupirika; sadzalola kuti inu muyesedwe koposa muyeso umene mutha kupirira. Koma pamene mwayesedwa, Iyenso adzakupatsani njira yopambanira mayeserowo.
14 Ngarud, ay-ayatek, umadayokayo kadagiti panagrukbab kadagiti didiosen.
Choncho abwenzi anga okondedwa, lekani kupembedza mafano.
15 Agsaoak kadakayo a kas nanakman a tattao, tapno mabalinyo nga ukomen ti ibagbagak.
Ndikuyankhula kwa a anthu anzeru zawo, nokha muweruze pa zimene ndikunenazi.
16 Ti kopa ti bendision a binendisyonantayo, saan kadi a pannakibingay daytoy iti dara ni Cristo? Ti tinapay a pinisitayo, saan kadi a pannakibingay daytoy iti bagi ni Cristo?
Pamene tidalitsa chikho cha Mgonero wa Ambuye, mothokoza Mulungu, kodi sitikugawana magazi a Khristu? Nanga buledi amene timanyemayo, kodi sitikugawana thupi la Khristu?
17 Gapu ta adda maysa a tinapay, datayo nga adu ket maymaysa a bagi. Mangalatayo amin iti maysa a tinapay a sangsangkamaysa.
Pakuti buledi ndi mmodzi yekha, ifenso ngakhale tili ambiri, ndife thupi limodzi, popeza tonse timagawana buledi mmodzi yemweyo.
18 Kitaenyo dagiti tattao ti Israel: saan kadi a dagiti mangmangan kadagiti naidaton ket karaman iti altar?
Taganizirani zimene amachita Aisraeli. Kodi onse amene amadya zoperekedwa nsembe, samachita nawo miyambo ya pa guwapo?
19 Ania ngarud ti ibagbagak? A ti maysa a didiosen ket adda mamaayna? Wenno dayta a taraon a naidaton iti didiosen ket adda mamaayna?
Kodi ndikutanthauza kuti nsembe zoperekedwa kwa mafano ndi kanthu konse, kapena kuti mafano ndi kanthu konse?
20 Ngem ibagak ti maipanggep kadagiti banbanag a daton dagiti pagano a Hentil, nga indatdatonda dagitoy a banbanag kadagiti demonio ket saan nga iti Dios. Saanko kayat a makikadduakayo kadagiti demonio!
Ayi. Nsembe za osakhulupirira zimaperekedwa kwa ziwanda, osati kwa Mulungu, ndipo sindikufuna kuti muziyanjana ndi ziwandazo.
21 Saankayo a mabalin nga uminom iti kopa ti Apo ken iti kopa dagiti demonio. Saankayo a mabalin a makilangen iti lamisan iti Apo ken iti lamisaan dagiti demonio.
Simungamwe chikho cha Ambuye, ndi kukamweranso chikho cha ziwanda. Simungadyere pa tebulo la Ambuye ndiponso la ziwanda.
22 Wenno pagpungtutentayo kadi ti Apo iti imon? Napigpigsatayo kadi ngem isuna?
Kodi tikufuna kuwutsa mkwiyo wa Ambuye? Kodi ndife amphamvu kuposa Iye?
23 “Nainkalintegan amin a banbanag,” ngem saan nga amin a banag ket mangipaay iti pagimbagam. “Nainkalintegan amin a banbanag,” ngem saan nga amin a banag ket mangpabileg kadagiti tattao.
Mutha kunena kuti, “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zili za phindu. “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zimathandiza.
24 Awan ti rumbeng a mangbirok ti bukodna a pagimbagan. Ngem ketdi, biruken koma ti tunggal maysa ti pagimbagan iti kaarrubana.
Munthu aliyense asafunefune zokomera iye yekha, koma zokomeranso ena.
25 Mabalinyo a kanen ti aniaman a lako idiay pagtagtagilakuan, nga awan ti pannakariribuk iti konsensia.
Idyani nyama iliyonse imene amagulitsa pa msika, osafunsa mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu.
26 Ta “Ti daga ket kukua ti Apo, ken ti linaonna daytoy.”
Popeza kuti, “Dziko lapansi ndi la Ambuye ndi zonse za mʼmenemo ndi zake.”
27 No awisennaka a mangan ti saan a namati ket kayat mo iti mapan, kanem ti aniaman a naikabil iti sangoanam nga awan ti pannakariribuk iti konsensia.
Ngati wosakhulupirira akuyitanani kuti mukadye naye, inuyo ndi kuvomera kupitako, mukadye chilichonse chimene akakupatseni ndipo musakafunse mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu.
28 Ngem no ibaga ti maysa a tao kenka, “Daytoy a taraon ket naggapu iti daton ti pagano,” saanmo a kanen daytoy. Daytoy ket para iti pagimbagan ti nangipaka-ammo kenka, ken para iti pagimbagan iti konsensia.
Koma ngati wina akuwuzani kuti, “Izi zaperekedwa nsembe,” musadye zimenezo, pofuna kuthandiza amene wakuwuzaniyo komanso chifukwa cha chikumbumtima.
29 Saanko a kayat a sawen a ti bukodyo a konsensia, ngem ti konsensia iti sabali a tao. Ta apay koma a maukom ti wayawayak babaen ti konsensia iti sabali?
Ndikunena za chikumbumtima cha winayo osati chanu. Tsono mungafunse kuti, nʼchifukwa chiyani ufulu wanga ukuphwanyidwa chifukwa cha chikumbumtima cha munthu wina?
30 No aglak-amak iti taraon nga addaan iti panagyaman, apay a mapabpabainannak para iti dayta a nagyamanakon?
Ngati ndikuyamika Mulungu chifukwa cha chakudya, nanga munthu angandinyoze bwanji pa zinthu zomwe ndayamikira nazo Mulungu?
31 Ngarud, no mangan wenno uminomkayo man, wenno aniaman nga aramidenyo, aramidenyo amin para iti pakaidayawan ti Dios.
Nʼchifukwa chake chilichonse mungadye kapena kumwa, kapena chimene mungachite, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu.
32 Saanyo a pasaktan dagiti Judio wenno dagiti Griego, wenno ti iglesia ti Dios.
Musakhumudwitse aliyense, kaya ndi Myuda, Mgriki, kapena mpingo wa Mulungu.
33 Padasenyo kas iti panangpadasko nga ay-ayoen dagiti amin a tattao kadagiti amin a banbanag. Saanko a birbiroken ti pagimbagak, ngem ti para iti kaaduan. Ar-aramidek daytoy tapno mabalinda a maisalakan.
Mu zonse ndikuyesetsa kukondweretsa aliyense mʼnjira iliyonse. Popeza sindikufunafuna zokondweretsa ine ndekha koma zokomera ambiri kuti apulumutsidwe.

< 1 Corinto 10 >