< 1 Cronicas 22 >
1 Ket kinuna ni David, “Ditoyto ti pakaipatakderan ti balay ni Yahweh a Dios, agraman ti altar para kadagiti daton a naan-anay a mapuoran nga idatag ti Israel.”
Ndipo Davide anati, “Nyumba ya Yehova Mulungu idzakhala pano, ndiponso guwa lansembe zopsereza za Israeli.”
2 Binilin ngarud ni David dagiti adipenna nga ummongenda dagiti gangannaet nga agnanaed iti daga ti Israel. Dinutokanna ida a paratikap kadagiti bato tapno maipatakder ti balay ni Yahweh.
Choncho Davide analamula kuti asonkhanitse alendo onse amene amakhala mu Israeli ndipo kuchokera pakati pawo anasankha amisiri a miyala kuti aseme miyala yomangira nyumba ya Mulungu.
3 Nangted ni David iti adu a landok tapno maaramid a lansa nga agpaay kadagiti ridaw dagiti pagserkan, ken para kadagiti bisagra. Nangted pay isuna iti adu a bronse a saan a matimbang
Ndipo anapereka zitsulo zambiri zopangira misomali ya zitseko za pa zipata ndi zolumikiza zake. Anaperekanso mkuwa wochuluka wokanika kuwuyeza.
4 ken adu a kayo ti sedro a saan a mabilang. (Nangiyeg dagiti taga-Sidon ken taga-Tiro kenni David iti adu unay a tabla ti sedro.)
Iye anaperekanso mitengo yambiri ya mkungudza, yosawerengeka, pakuti anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo anabweretsa yambiri kwa Davide.
5 Kinuna ni David, “Ubing pay ken awan pay kapadasanna ti anakko a ni Solomon, ket masapul a naisangsangayan ti kinapintas ti balay a maipatakder para kenni Yahweh, tapno agbalin a nalatak ken nadayag kadagiti amin a sabali a daga. Isu nga isaganak ti pannakaipatakder daytoy.” Kasta unay ngarud ti inaramid ni David a panagsagana sakbay ti ipapatayna.
Davide anati, “Mwana wanga Solomoni ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Koma nyumba yomwe timangire Yehova iyenera kukhala yaulemerero, yotchuka ndi yokongola pamaso pa anthu a mitundu yonse. Choncho ndikonzekeratu zambiri.” Motero Davide anayikonzekera kwambiri asanamwalire.
6 Pinaayabanna ngarud ni Solomon nga anakna ket binilinna a mangipatakder iti balay nga agpaay kenni Yahweh a Dios ti Israel.
Tsono iye anayitana Solomoni mwana wake ndipo anamulamula kuti adzamangire nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
7 Kinuna ni David kenni Solomon, “Anakko, pinanggepko a siak ti mangipatakder iti balay para iti nagan ni Yahweh a Diosko.
Davide anati kwa Solomoni, “Mwana wanga, ine ndinali ndi maganizo oti ndimangire nyumba Dzina la Yehova Mulungu wanga.
8 Ngem immay kaniak ni Yahweh a kunana, 'Nangpasayasayka iti adu a dara ken nakirangetka iti adu a gubat. Saanka a mangipatakder iti maysa a balay nga agpaay iti naganko, gapu ta nangpasayasayka iti adu a dara iti daga iti imatangko.
Koma Yehova anandiyankhula kuti, ‘Iwe wapha anthu ambiri ndiponso wachita nkhondo zambiri. Sumangira dzina langa nyumba chifukwa wapha anthu ambiri pa dziko lapansi pamaso panga.
9 Nupay kasta, maaddaankanto iti anak a lalaki nga addaan kapia. Ikkakto isuna iti inana kadagiti amin a kabusorna iti amin a disso. Ta ti nagannanto ket Solomon, ket ipaaykonto ti kapia ken talna iti Israel kadagiti al-aldawna.
Koma udzabala mwana wamwamuna amene adzakhala munthu wamtendere ndi wabata ndipo ndidzamupatsa mpumulo kuchokera kwa adani ake onse a mbali zonse. Dzina lake adzatchedwa Solomoni ndipo Ine ndidzapereka mtendere ndi bata kwa Israeli pa nthawi ya ulamuliro wake.
10 Mangipatakderto isuna iti balay nga agpaay iti naganko. Agbalinto isuna nga anakko ken siakto ti amana. Patibkerekto iti agnanayon ti trono ti pagarianna iti entero nga Israel.”'
Iye ndiye adzandimangire nyumba. Adzakhala mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake. Ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake waufumu mʼdziko la Israeli mpaka muyaya.’”
11 Ita, anakko, adda koma a kanayon ni Yahweh kenka ken pagballigiennaka. Ipatakdermo koma ti balay ni Yahweh a Diosmo, kas imbagana nga aramidem.
“Tsopano mwana wanga, Yehova akhale nawe ndipo upambane ndi kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wako, monga momwe Iye ananenera kuti udzatero.
12 Ni Yahweh laeng ti mangted kenka iti pannakaammo ken pannakaawat, tapno matungpalmo ti linteg ni Yahweh a Diosmo, inton isaadnaka a mangidaulo iti entero nga Israel.
Yehova akupatse nzeru ndi kumvetsetsa pamene Iye adzakuyika kukhala wolamulira Israeli, kuti udzasunge malamulo a Yehova Mulungu wako.
13 Ket agballigikanto, no tungpalem a naimbag dagiti paglintegan ken bilin nga inted ni Yahweh kenni Moises maipapan iti Israel. Bumilegka ken tumuredka. Saanka nga agbuteng ken maupay.
Ndipo udzapambana ngati udzamvera mosamala malangizo ndi malamulo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kudzera mwa Mose. Khala wamphamvu ndi wolimba mtima. Usachite mantha kapena kutaya mtima.
14 Ita, kitaem, inkarigatak nga insagana para iti balay ni Yahweh ti 100, 000 a talento ti balitok, maysa a milion a talento ti pirak, adu a bronse ken landok. Nangisaganaak pay iti kayo ken bato. Masapul a nayunam pay dagitoy.
“Ine movutikira kwambiri ndapereka ku Nyumba ya Mulungu matani 3,400 agolide, matani 34,000 asiliva, ndiponso mkuwa ndi chitsulo, matabwa ndi miyala. Ndipo iwe utha kuwonjezerapo pa zimenezi.
15 Adu dagiti trabahador a kaduam: dagiti paratikap iti bato, dagiti kumakabite, karpentero, ken dagiti saan a mabilang a nalalaing a kumikitikit iti aniaman a kita,
Iwe uli ndi antchito ambiri: osema miyala, amisiri a miyala, ndi amisiri a matabwa, komanso anthu ambiri aluso la ntchito zosiyanasiyana,
16 a makabael a mangtrabaho iti balitok, pirak, bronse ken landok. Isu a rugiamon ti agtrabaho, ket ni Yahweh koma ti makikaadda kenka.”
zagolide ndi zasiliva, zamkuwa, zazitsulo, amisiri osawerengeka. Tsopano yamba ntchito, ndipo Yehova akhale nawe.”
17 Binilin pay ni David dagiti amin a mangidadaulo ti Israel a tulonganda ni Solomon nga anakna, a kunana,
Tsono Davide analamula atsogoleri onse a Israeli kuti athandize Solomoni mwana wake.
18 “Kaduayo ni Yahweh a Diosyo ket inikkannakayo iti kappia iti amin a disso. Impaimana kaniak dagiti agnanaed iti rehion. Ti rehion ket naparmek iti sangoanan ni Yahweh ken dagiti tattaona.
Iye anawawuza kuti, “Kodi Yehova Mulungu, sali nanu? Ndipo Iye siwakupatsani mpumulo mbali zonse? Pakuti Iyeyo wapereka eni nthaka kwa inu ndipo dziko lili pa ulamuliro wa Yehova ndi anthu ake.
19 Ita, sapulenyo ni Yahweh a Diosyo iti amin a puso ken kararuayo. Agsaganakayo a mangibangon iti nasantoan a lugar ni Yahweh a Dios. Kalpasanna, mabalinyo nga iyeg ti lakasa ti tulag ni Yahweh ken dagiti banbanag a kukua ti Dios iti balay a naipatakder para iti nagan ni Yahweh.”
Tsono perekani mtima wanu ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu. Yambani kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti mubweretse Bokosi la Chipangano la Yehova ndi zinthu zopatulika za Mulungu mʼNyumba ya Mulungu imene idzamangidwa chifukwa cha dzina la Yehova.”